< Yeremiya 20 >

1 Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
Or Paschhur, fils du sacrificateur Immer, qui était chef de la maison de l'Éternel, entendit Jérémie qui prophétisait ces choses.
2 Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
Alors Pashhur frappa Jérémie, le prophète, et le mit dans les ceps qui se trouvaient à la porte supérieure de Benjamin, dans la maison de l'Éternel.
3 Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
Le lendemain, Paschhur fit sortir Jérémie des ceps. Jérémie lui dit: « Yahvé n'a pas donné à ton nom le nom de Pashhur, mais celui de Magormissabib.
4 Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
Car Yahvé a dit: « Voici, je vais faire de toi une terreur pour toi-même et pour tous tes amis. Ils tomberont par l'épée de leurs ennemis, et tes yeux le verront. Je livrerai tout Juda entre les mains du roi de Babylone, qui les emmènera captifs à Babylone et les tuera par l'épée.
5 Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
Et je livrerai toutes les richesses de cette ville, tous ses biens et tous ses objets précieux, oui, je livrerai tous les trésors des rois de Juda entre les mains de leurs ennemis. Ils les feront prisonniers, les prendront et les emmèneront à Babylone.
6 Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
Toi, Pashhur, et tous ceux qui habitent dans ta maison, vous irez en captivité. Vous viendrez à Babylone, et là vous mourrez, et là vous serez enterrés, vous et tous vos amis, à qui vous avez prophétisé faussement.'"
7 Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
Yahvé, tu m'as persuadé, et j'ai été persuadé. Tu es plus fort que moi, et tu l'as emporté. Je suis devenu la risée de toute la journée. Tout le monde se moque de moi.
8 Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
Car aussi souvent que je parle, je crie; Je crie: « Violence et destruction! » parce que la parole de Yahvé est devenue un opprobre pour moi, et une dérision, toute la journée.
9 Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
Si je dis cela, je ne ferai pas mention de lui, ou de parler encore en son nom, alors il y a dans mon cœur comme un feu brûlant enfermé dans mes os. Je suis fatigué de tout retenir. Je ne peux pas.
10 Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
Car j'ai entendu la diffamation de beaucoup: « Terreur de tous les côtés! Dénoncez, et nous le dénoncerons! » disent tous mes amis familiers, ceux qui guettent ma chute. « Peut-être sera-t-il persuadé, et nous l'emporterons sur lui, et nous prendrons notre revanche sur lui. »
11 Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
Mais Yahvé est avec moi comme un grand puissant. C'est pourquoi mes persécuteurs vont trébucher, et ils ne l'emporteront pas. Ils seront totalement déçus parce qu'ils n'ont pas fait preuve de sagesse, même avec un déshonneur éternel qui ne sera jamais oublié.
12 Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
Mais Yahvé des armées, qui éprouve les justes, qui voit le cœur et l'esprit, laissez-moi voir votre vengeance sur eux, car je vous ai révélé ma cause.
13 Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
Chantez à Yahvé! Louez Yahvé, car il a délivré l'âme du malheureux de la main des méchants.
14 Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
Maudit soit le jour où je suis né. Ne laissez pas le jour où ma mère m'a enfanté être béni.
15 Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
Maudit soit l'homme qui a apporté des nouvelles à mon père, en disant, « Un garçon est né pour toi », ce qui le rend très heureux.
16 Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
Que cet homme soit comme les villes que l'Éternel a détruites, et ne s'est pas repenti. Qu'il entende un cri le matin, et de crier à l'heure du midi,
17 Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
parce qu'il ne m'a pas tué depuis le ventre de ma mère. Donc ma mère aurait été ma tombe, et ses entrailles toujours grandes.
18 Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?
Pourquoi suis-je sorti du ventre de ma mère pour voir le travail et la douleur? que mes jours soient consumés par la honte?

< Yeremiya 20 >