< Yeremiya 2 >
1 Yehova anandiwuza kuti,
La parole de Yahweh me fut adressée en ces termes:
2 “Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
Va et crie aux oreilles de Jérusalem en ces termes: Ainsi parle Yahweh: Je me suis souvenu de la piété de ta jeunesse, de l’amour de tes fiançailles, alors que tu me suivais au désert, au pays qu’on n’ensemence pas.
3 Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
Israël était la chose consacré à Yahweh, les prémices de son revenu; quiconque en mangeait se rendait coupable; le malheur fondait sur lui, — oracle de Yahweh.
4 Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
Ecoutez la parole de Yahweh, maison de Jacob, et vous toutes, familles de la maison d’Israël:
5 Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
Ainsi parle Yahweh: Quelle iniquité vos pères ont-ils trouvé en moi, pour s’éloigner de moi, pour suivre la vanité et devenir eux-mêmes vanité?
6 Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
Ils n’ont pas dit: « Où est Yahweh, qui nous a fait monter du pays d’Égypte, qui nous a guidés dans le désert, dans le pays aride et crevassé, dans le pays de sécheresse et d’ombre de mort, dans le pays où nul homme ne passe, et où personne n’habite? »
7 Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
Et je vous ai fait venir dans un pays semblable à un verger, pour en manger les fruits et les biens, et, une fois entrés, vous avez souillé mon pays, et fait de mon héritage une abomination.
8 Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
Les prêtres n’ont pas dit: « Où est Yahweh? » Les dépositaires de la loi ne m’ont pas connu; les pasteurs m’ont été infidèles, et les prophètes ont prophétisé par Baal; et ils ont suivi ceux qui ne sont d’aucun secours.
9 “Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
Aussi je veux encore plaider contre vous, — oracle de Yahweh, et je plaiderai contre les enfants de vos enfants.
10 Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
Passez donc aux îles de Céthim et regardez; envoyez à Cédar et observez bien; et voyez s’il y a là rien de semblable.
11 Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
Une nation change-t-elle de dieux? — Et encore ce ne sont pas des dieux!... Et mon peuple a changé sa gloire contre ce qui ne sert à rien!
12 Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
Cieux, étonnez-vous-en, frémissez d’horreur et soyez stupéfaits, oracle de Yahweh!
13 “Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
Car mon peuple a fait double mal: ils m’ont abandonné, moi, la source des eaux vives, pour se creuser des citernes, des citernes crevassées, qui ne retiennent pas l’eau.
14 Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
Israël est-il un esclave, est-il né d’un esclave dans la maison? Pourquoi donc est-il traité comme un butin?
15 Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
Contre lui les lionceaux rugissent, poussent leurs cris, et ils mettent son pays en dévastation. Ses villes sont incendiées, sans d’habitants.
16 Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
Même les fils de Noph et de Taphnès te tondent le crâne!
17 Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
Cela ne t’arrive-t-il pas parce que tu as abandonné Yahweh, ton Dieu, au temps où il te dirigeait dans la voie?
18 Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
Et maintenant qu’as-tu à faire sur la route de l’Égypte, pour aller boire l’eau du Nil, et qu’as-tu à faire sur la route de l’Assyrie, pour aller boire l’eau du fleuve?
19 Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
Ton impiété te châtie et tes rébellions te punissent! Sache donc et vois combien il est mauvais et amer d’avoir abandonné Yahweh, ton Dieu, et de n’avoir de moi aucune crainte, — oracle du Seigneur Yahweh des armées.
20 “Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Car depuis longtemps tu as brisé ton joug, tu as rompu tes liens et tu as dit: « Je ne servirai plus! » Car sur toute colline élevée et sous ton arbre vert tu t’es étendue, comme une courtisane.
21 Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
Et moi, je t’avais plantée comme une vigne excellente, tout entière d’une souche franche. Comment t’es-tu changée pour moi en sarments bâtards d’une vigne étrangère?
22 Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
Oui, quand tu te laverais à la soude, et que tu prodiguerais la potasse, ton iniquité ferait tache devant moi, — oracle du Seigneur Yahweh.
23 “Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
Comment dis-tu: « Je ne me suis pas souillée; je ne suis pas allée après les Baals? » Vois les traces de tes pas dans la Vallée; reconnais ce que tu as fait! Chamelle légère, croisant ses pas en tout sens,
24 wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
onagre habituée au désert, dans l’ardeur de sa passion, elle aspire l’air: qui l’empêchera de satisfaire son désir? Nul de ceux qui la recherchent n’a à se fatiguer; ils la trouvent en son mois.
25 Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
Prends garde que ton pied ne se trouve à nu, et que ton gosier ne se dessèche! Mais tu dis: « Inutile! Non, car j’aime les étrangers et j’irai après eux! »
26 “Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
Comme un voleur pris sur le fait est couvert de honte, ainsi ont été confondus la maison d’Israël, eux, leurs rois, leurs chefs, leurs prêtres et leurs prophètes,
27 Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
qui disent au bois: « Tu es mon père, » et à la pierre: « Tu m’as mis au monde. » Car ils m’ont tourné le dos, et non la face, et au temps de leur malheur ils disent: « Lève-toi et sauve-nous! »
28 Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
Où sont donc les dieux que tu t’es faits? Qu’ils se lèvent, s’ils peuvent te sauver au temps de ton malheur! Car aussi nombreux que tes villes sont tes dieux, ô Juda.
29 “Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
Pourquoi plaidez-vous contre moi? Vous m’avez tous été infidèles, — oracle de Yahweh.
30 “Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
C’est en vain que j’ai frappé vos fils; ils n’en ont pas retiré d’instruction; votre épée a dévoré vos prophètes, comme un lion destructeur.
31 “Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
Quelle race vous êtes! Considérez la parole de Yahweh: Ai-je été pour Israël un désert, un pays d’épaisses ténèbres? Pourquoi mon peuple a-t-il dit: « Nous sommes libres, nous ne reviendrons pas à vous? »
32 Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
Une vierge oublie-t-elle sa parure, une fiancée sa ceinture? Et mon peuple m’a oublié depuis des jours sans nombre!
33 Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
Que tu sais bien disposer tes voies pour chercher l’amour! Pour cela, même avec le crime tu familiarises tes voies!
34 Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
Jusque sur les pans de tes vêtements, on trouve le sang des pauvres innocents; tu ne les avais pas surpris en délit d’effraction, mais tu les as tués pour toutes ces choses.
35 inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
Et tu dis: « Oui, je suis innocente; certainement sa colère s’est détournée de moi. » Me voici pour te faire le procès sur ce que tu dis: « Je n’ai pas péché! »
36 Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
Quelle hâte tu mets à changer ta voie! Tu seras rendue confuse par l’Égypte, comme tu l’as été par l’Assyrie.
37 Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.
De là aussi tu reviendras, les mains sur la tête; car Yahweh a rejeté ceux en qui tu mets ta confiance, et tu ne réussiras pas avec eux.