< Yeremiya 2 >

1 Yehova anandiwuza kuti,
La parole de Yahvé me fut adressée, en ces termes:
2 “Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
« Va, et proclame aux oreilles de Jérusalem: « Yahvé dit », « Je me souviens pour vous de la gentillesse de votre jeunesse, votre amour en tant que mariée, comment tu m'as poursuivi dans le désert, dans une terre qui n'a pas été ensemencée.
3 Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
Israël était la sainteté pour Yahvé, les prémices de son accroissement. Tous ceux qui le dévorent seront tenus pour coupables. Le malheur viendra sur eux, dit Yahvé. »
4 Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
Écoutez la parole de Yahvé, maison de Jacob, et toutes les familles de la maison d'Israël!
5 Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
Yahvé dit, « Quelle iniquité vos pères ont-ils trouvée en moi, qu'ils se sont éloignés de moi, et ont marché après une vanité sans valeur, et sont devenus sans valeur?
6 Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
Ils n'ont pas dit: « Où est l'Éternel qui nous a fait monter du pays d'Égypte? qui nous a conduit dans le désert, à travers un pays de déserts et de fosses, à travers un pays de sécheresse et d'ombre de la mort, à travers une terre que personne n'a traversée, et où aucun homme ne vivait?
7 Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
Je vous ai fait entrer dans un pays abondant. pour manger ses fruits et ses bienfaits; mais quand vous êtes entrés, vous avez souillé mon pays, et ont fait de mon héritage une abomination.
8 Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
Les prêtres ne disaient pas: « Où est Yahvé? et ceux qui s'occupent de la loi ne me connaissaient pas. Les dirigeants ont aussi transgressé mes règles, et les prophètes ont prophétisé par Baal et suivi des choses qui ne profitent pas.
9 “Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
« C'est pourquoi je contesterai encore avec vous, dit Yahvé, « et je me disputerai avec les enfants de vos enfants ».
10 Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
Car passez dans les îles de Kittim, et regardez. Envoie à Kedar, et réfléchis bien, et voir s'il y a eu une telle chose.
11 Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
Une nation a changé ses dieux, qui ne sont pas vraiment des dieux? Mais mon peuple a changé sa gloire pour ce qui ne profite pas.
12 Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
« Cieux, soyez étonnés de ce qui suit et avoir horriblement peur. Soyez très désolés », dit Yahvé.
13 “Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
« Car mon peuple a commis deux maux: ils m'ont abandonné, moi, la source d'eau vive, et se sont taillés des citernes: des citernes cassées qui ne peuvent pas contenir d'eau.
14 Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
Israël est-il un esclave? Est-il né dans l'esclavage? Pourquoi est-il devenu un captif?
15 Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
Les jeunes lions ont rugi contre lui et ont élevé leur voix. Ils ont fait de ses terres des déchets. Ses villes sont brûlées, sans habitant.
16 Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
Les enfants de Memphis et de Tachpanès ont brisé la couronne de ta tête.
17 Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
« N'est-ce pas vous qui l'avez provoqué? en ce que tu as abandonné Yahvé ton Dieu, quand il te conduisait par le chemin?
18 Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
Maintenant, que gagnez-vous à aller en Égypte, pour boire les eaux du Shihor? Ou bien, pourquoi voulez-vous aller jusqu'en Assyrie, pour boire les eaux du fleuve?
19 Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
« Ta propre méchanceté te corrigera, et votre retour en arrière vous réprimandera. Sachez donc et voyez que c'est une chose mauvaise et amère, que tu as abandonné Yahvé ton Dieu, et que ma crainte ne soit pas en vous, dit le Seigneur, Yahvé des Armées.
20 “Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
« Car il y a longtemps que j'ai brisé ton joug, et briser vos liens. Tu as dit: « Je ne servirai pas ». car sur chaque haute colline et sous chaque arbre vert, tu t'es incliné, jouant la prostituée.
21 Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
Pourtant, je t'avais planté une vigne noble, une semence pure et fidèle. Comment donc êtes-vous devenus pour moi les branches dégénérées d'une vigne étrangère?
22 Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
Car si tu te laves avec de la lessive, et utiliser beaucoup de savon, mais ton iniquité est marquée devant moi », dit le Seigneur Yahvé.
23 “Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
« Comment pouvez-vous dire: « Je ne suis pas souillé »? Je ne me suis pas attaqué aux Baals? Voyez votre chemin dans la vallée. Sachez ce que vous avez fait. Tu es un dromadaire rapide qui parcourt ses chemins,
24 wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
un âne sauvage habitué au désert, qui renifle le vent dans sa soif. Quand elle est en chaleur, qui peut la repousser? Tous ceux qui la cherchent ne se lasseront pas. Dans son mois, ils la trouveront.
25 Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
« Empêchez vos pieds d'être nus, et votre gorge de la soif. Mais tu as dit: « C'est en vain ». Non, car j'ai aimé des étrangers, et je les suivrai.
26 “Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
Comme le voleur a honte quand on le trouve, et la maison d'Israël a honte... eux, leurs rois, leurs princes, leurs prêtres et leurs prophètes,
27 Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
qui disent au bois: « Tu es mon père ». et une pierre: « Tu m'as donné naissance ». car ils m'ont tourné le dos, et non leur visage, mais au moment de leur détresse, ils diront: « Lève-toi et sauve-nous! ».
28 Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
« Mais où sont vos dieux que vous vous êtes faits? Laissez-les se lever, s'ils peuvent vous sauver au moment où vous êtes dans le pétrin, car tu as autant de dieux que tu as de villes, ô Juda.
29 “Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
« Pourquoi voulez-vous me disputer? Vous avez tous péché contre moi, dit Yahvé.
30 “Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
« C'est en vain que j'ai frappé tes enfants. Ils n'ont reçu aucune correction. Votre propre épée a dévoré vos prophètes, comme un lion destructeur.
31 “Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
Génération, considère la parole de Yahvé. Ai-je été un désert pour Israël? Ou une terre de ténèbres épaisses? Pourquoi mon peuple dit-il: « Nous nous sommes détachés »? Nous ne viendrons plus chez toi »?
32 Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
« Une vierge peut-elle oublier ses ornements, ou une mariée sa tenue? Mais mon peuple m'a oublié pendant des jours sans nombre.
33 Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
Comme tu prépares bien ton chemin pour chercher l'amour! C'est pourquoi tu as même enseigné tes voies aux méchantes femmes.
34 Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
Le sang des âmes des pauvres innocents se trouve aussi dans tes jupes. Vous ne les avez pas trouvés en train d'entrer par effraction, mais c'est à cause de toutes ces choses.
35 inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
Tu as pourtant dit: « Je suis innocent. Sa colère s'est détournée de moi. « Voici, je vais vous juger, parce que tu dis: « Je n'ai pas péché ».
36 Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
Pourquoi faites-vous tant d'efforts pour changer vos habitudes? Tu auras aussi honte de l'Égypte, comme vous avez eu honte de l'Assyrie.
37 Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.
Vous quitterez aussi ce lieu avec les mains sur la tête; car Yahvé a rejeté ceux en qui vous vous êtes confiés, et vous ne prospérerez pas avec eux.

< Yeremiya 2 >