< Yeremiya 19 >
1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
Tak mówi PAN: Idź i kup dzban gliniany od garncarza, [weź] ze sobą [kilka osób] spośród starszych ludu i starszych kapłanów;
2 ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
Wyjdź do doliny syna Hinnom, która znajduje się przy wejściu do Bramy Wschodniej, [i] głoś tam słowa, które do ciebie będę mówić.
3 Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
Powiedz: Słuchajcie słowa PANA, królowie Judy i mieszkańcy Jerozolimy! Tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Oto sprowadzę nieszczęście na to miejsce, a każdemu, kto usłyszy, zaszumi w uszach.
4 Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
Ponieważ mnie opuścili i zbezcześcili to miejsce, paląc w nim kadzidło innym bogom, których nie znali oni ani ich ojcowie oraz królowie Judy, i napełnili to miejsce krwią niewinnych;
5 Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
I pobudowali wyżyny Baalowi, aby spalić swoich synów w ogniu jako całopalenia dla Baala, czego im nie nakazałem ani nie mówiłem i [co] nie przyszło mi nawet na myśl.
6 Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
Dlatego oto nadchodzą dni, mówi PAN, w których to miejsce nie będzie już nazywane Tofet ani Doliną Syna Hinnom, ale Doliną Rzezi.
7 “‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
I wniwecz obrócę radę Judy i Jerozolimy na tym miejscu i sprawię, że padną od miecza przed swoimi wrogami i od ręki tych, którzy czyhają na ich życie. I wydam ich trupy na pożarcie ptactwu nieba i zwierzętom ziemi.
8 Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Wydam także to miasto na spustoszenie i na świstanie; każdy, kto będzie przechodził obok, zdumieje się i będzie świstać z powodu wszystkich jego plag.
9 Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
I sprawię, że będą jeść ciała swoich synów i ciała swoich córek, a każdy [z nich] będzie jeść ciało swego bliźniego podczas oblężenia i w ucisku, którymi ścisną ich wrogowie i ci, którzy czyhają na ich życie.
10 “Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
Potem stłucz [ten] dzban na oczach tych mężczyzn, którzy pójdą z tobą;
11 ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
I powiedz im: Tak mówi PAN zastępów: Tak samo rozbiję ten lud i to miasto, jak tłucze się naczynie garncarskie, którego nie można potem naprawić. I będą grzebać zmarłych w Tofet, bo nie będzie innego miejsca na grzebanie.
12 Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
Tak uczynię temu miejscu, mówi PAN, i jego mieszkańcom, i postąpię z tym miastem tak jak z Tofet.
13 Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
I domy Jerozolimy i domy królów Judy będą nieczyste jak to miejsce Tofet z powodu wszystkich domów, na których dachach palili kadzidło wszystkim zastępom nieba i wylewali ofiary z płynów innym bogom.
14 Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
Wtedy Jeremiasz wrócił z Tofet, dokąd wysłał go PAN, aby tam prorokował, stanął na dziedzińcu domu PANA i powiedział do całego ludu:
15 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”
Tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Oto sprowadzę na to miasto i na wszystkie okoliczne miasta całe to nieszczęście, które zapowiedziałem przeciwko niemu, bo zatwardzili swój kark, aby nie słuchać moich słów.