< Yeremiya 19 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
So sprach Jehovah: Gehe hin und kaufe einen Krug vom Töpfer des Geschirrs, und mit etlichen von den Ältesten des Volkes und von den Ältesten der Priester.
2 ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
Und gehe hinaus nach der Schlucht Ben-Hinnoms, das am Eingang zum Tore der Scherben ist, und rufe aus allda die Worte, die Ich zu dir reden werde,
3 Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
Und sprich: Höret das Wort Jehovahs, Könige Jehudahs und Bewohner Jerusalems! So spricht Jehovah der Heerscharen, der Gott Israels: Siehe, Ich bringe Böses über diesen Ort, daß jedem, der es hört, seine Ohren gellen werden.
4 Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
Darum, daß sie Mich verließen und diesen Ort Mir entfremdeten und darin anderen Göttern räucherten, die sie nicht kannten, weder sie noch ihre Väter, noch Jehudahs Könige, und diesen Ort mit dem Blut Unschuldiger erfüllten;
5 Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
Und dem Baal Opferhöhen bauten, um im Feuer ihre Söhne zu verbrennen als Brandopfer dem Baal, was Ich nicht geboten, noch geredet hatte: und was Mir nicht ins Herz aufgestiegen war.
6 Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
Darum, seht, es kommen Tage, spricht Jehovah, daß diesen Ort man nicht mehr Topheth und die Schlucht Ben-Hinnom, sondern die Schlucht des Würgens nennen wird.
7 “‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
Und vereiteln will Ich an diesem Ort den Rat Jehudahs und Jerusalems, und sie durch das Schwert vor ihren Feinden fallen lassen, und durch die Hand derer, die nach ihrer Seele trachten und ihren Leichnam zum Fraß dem Gevögel des Himmels und dem Getier der Erde geben.
8 Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Und diese Stadt will Ich zur Verwüstung machen und zum Gezisch. Ein jeder, der an ihr vorübergeht, soll ob ihr erstaunen und zischen über alle ihre Schläge,
9 Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
Und lasse sie essen das Fleisch ihrer Söhne und das Fleisch ihrer Töchter, und der Mann wird das Fleisch seines Genossen essen in der Belagerung und der Beängstigung, mit der sie ihre Feinde und die, so ihnen nach der Seele trachten, beängstigen.
10 “Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
Und du sollst den Krug zerbrechen vor der Männer Augen, die mit dir gegangen sind,
11 ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
Und sollst zu ihnen sprechen: Also spricht Jehovah der Heerscharen: So zerbreche Ich dieses Volk und diese Stadt, wie einer des Töpfers Gefäß zerbricht, daß man es nicht wieder heilen kann. Und in Topheth werden sie begraben, weil sonst kein Ort mehr ist zu begraben.
12 Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
So werde Ich, spricht Jehovah, diesem Ort und seinen Bewohnern tun, daß Ich diese Stadt wie Topheth mache.
13 Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
Und es sollen die Häuser Jerusalems und die Häuser der Könige Jehudahs, die unreinen, werden wie der Ort Topheth, alle die Häuser, auf deren Dächern sie geräuchert allem Heer der Himmel, und Trankopfer gegossen anderen Göttern.
14 Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
Und Jirmejahu kam von Topheth, wo Jehovah ihn hingesandt zu weissagen, und stand in dem Vorhof von Jehovahs Haus und sprach zu allem Volk:
15 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”
So spricht Jehovah der Heerscharen, der Gott Israels: Siehe, Ich bringe herein über diese Stadt und über alle ihre Städte all das Böse, das Ich über sie geredet habe, weil sie ihren Nacken verhärten und auf Meine Worte nicht hören.

< Yeremiya 19 >