< Yeremiya 19 >
1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
Thus he said Yahweh go and you will buy a bottle of a potter of earthenware and some of [the] elders of the people and some of [the] elders of the priests.
2 ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
And you will go out to [the] valley of Ben Hinnom which [is at] [the] entrance of [the] gate of (the potsherd *Q(k)*) and you will proclaim there the words which I will speak to you.
3 Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
And you will say hear [the] word of Yahweh O kings of Judah and [the] inhabitants of Jerusalem thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel here I [am] about to bring calamity on the place this which every [one who] hears of it they will tingle ears his.
4 Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
Because - that they have forsaken me and they have treated as foreign the place this and they have made smoke in it to gods other which not they knew them they and ancestors their and [the] kings of Judah and they have filled the place this [the] blood of innocent [ones].
5 Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
And they have built [the] high places of Baal to burn children their in the fire burnt offerings to Baal which not I commanded and not I spoke and not it came up on heart my.
6 Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
Therefore here! days [are] coming [the] utterance of Yahweh and not it will be called to the place this again Topheth and [the] valley of Ben Hinnom that except [the] valley of slaughter.
7 “‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
And I will make void [the] plan of Judah and Jerusalem in the place this and I will make fall them by the sword before enemies their and by [the] hand of [those who] seek life their and I will give corpse[s] their to food to [the] bird[s] of the heavens and to [the] animal[s] of the earth.
8 Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
And I will make the city this into a waste and into a hissing every [one who] passes by at it he will be appalled and he may hiss on all wounds its.
9 Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
And I will make eat them [the] flesh of sons their and [the] flesh of daughters their and everyone [the] flesh of neighbor his they will eat in [the] siege and in [the] distress which they will press them enemies their and [those who] seek life their.
10 “Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
And you will break the bottle to [the] eyes of the men who go with you.
11 ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
And you will say to them thus he says - Yahweh of hosts thus I will break the people this and the city this just as someone breaks [the] vessel of the potter which not it will be able to be repaired again and in Topheth people will bury from not room to bury.
12 Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
Thus I will do to the place this [the] utterance of Yahweh and to inhabitants its and to make the city this like Topheth.
13 Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
And they will be [the] houses of Jerusalem and [the] houses of [the] kings of Judah like [the] place of Topheth the unclean [things] to all the houses which people made smoke on roofs their to all [the] host of the heavens and they poured out drink offerings to gods other.
14 Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
And he came Jeremiah from Topheth where he had sent him Yahweh there to prophesy and he stood in [the] court of [the] house of Yahweh and he said to all the people.
15 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”
Thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel here I ([am] about to bring *Q(k)*) to the city this and on all cities its all the calamity which I have spoken on it for they have stiffened neck their to not to hear words my.