< Yeremiya 18 >

1 Yehova anawuza Yeremiya kuti,
[the] word which to be to(wards) Jeremiah from with LORD to/for to say
2 “Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.”
to arise: rise and to go down house: home [the] to form: potter and there [to] to hear: hear you [obj] word my
3 Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero.
and to go down house: home [the] to form: potter (and behold he/she/it *Q(K)*) to make: [do] work upon [the] wheel
4 Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.
and to ruin [the] article/utensil which he/she/it to make in/on/with clay in/on/with hand [the] to form: potter and to return: again and to make him article/utensil another like/as as which to smooth in/on/with eye: appearance [the] to form: potter to/for to make: do
5 Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
and to be word LORD to(wards) me to/for to say
6 “Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya.
like/as to form: potter [the] this not be able to/for to make: do to/for you house: household Israel utterance LORD behold like/as clay in/on/with hand [the] to form: potter so you(m. p.) in/on/with hand my house: household Israel
7 Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga,
moment to speak: promise upon nation and upon kingdom to/for to uproot and to/for to tear and to/for to perish
8 ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira.
and to return: turn back [the] nation [the] he/she/it from distress: evil his which to speak: speak upon him and to be sorry: relent upon [the] distress: harm which to devise: devise to/for to make: do to/for him
9 Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu.
and moment to speak: promise upon nation and upon kingdom to/for to build and to/for to plant
10 Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.
and to make: do ([the] bad: evil *Q(K)*) in/on/with eye: seeing my to/for lest to hear: hear in/on/with voice my and to be sorry: relent upon [the] welfare which to say to/for be good [obj] him
11 “Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’
and now to say please to(wards) man: anyone Judah and upon to dwell Jerusalem to/for to say thus to say LORD behold I to form: plan upon you distress: harm and to devise: devise upon you plot to return: return please man: anyone from way: conduct his [the] bad: evil and be good way: conduct your and deed your
12 Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’”
and to say to despair for after plot our to go: follow and man: anyone stubbornness heart his [the] bad: evil to make: do
13 Yehova akuti, “Uwafunse anthu a mitundu ina kuti: Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi? Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita chinthu choopsa kwambiri.
to/for so thus to say LORD to ask please in/on/with nation who? to hear: hear like/as these horror to make: do much virgin Israel
14 Kodi chisanu chimatha pa matanthwe otsetsereka a phiri la Lebanoni? Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
to leave: forsake from rock Sirion snow Lebanon if: surely yes to uproot water be a stranger cool to flow
15 Komatu anthu anga andiyiwala; akufukiza lubani kwa mafano achabechabe. Amapunthwa mʼnjira zawo zakale. Amayenda mʼnjira zachidule ndi kusiya njira zabwino.
for to forget me people my to/for vanity: vain to offer: offer and to stumble them in/on/with way: road their path forever: antiquity to/for to go: walk path way: road not to build
16 Dziko lawo amalisandutsa chipululu, chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse; onse odutsapo adzadabwa kwambiri ndipo adzapukusa mitu yawo.
to/for to set: make land: country/planet their to/for horror: appalled (piping *Q(K)*) forever: enduring all to pass upon her be desolate: appalled and to wander in/on/with head his
17 Ngati mphepo yochokera kummawa, ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo; ndidzawafulatira osawathandiza pa tsiku la mavuto awo.”
like/as spirit: breath east to scatter them to/for face: before enemy neck and not face to see: see them in/on/with day calamity their
18 Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”
and to say to go: come! and to devise: devise upon Jeremiah plot for not to perish instruction from priest and counsel from wise and word from prophet to go: come! and to smite him in/on/with tongue and not to listen to(wards) all word his
19 Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni; imvani zimene adani anga akunena za ine!
to listen [emph?] LORD to(wards) me and to hear: hear to/for voice opponent my
20 Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino? Komabe iwo andikumbira dzenje. Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu kudzawapempherera kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
to complete underneath: instead welfare distress: evil for to pierce pit to/for soul: life my to remember to stand: stand I to/for face: before your to/for to speak: speak upon them welfare to/for to return: turn back [obj] rage your from them
21 Choncho langani ana awo ndi njala; aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga. Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye; amuna awo aphedwe ndi mliri, anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
to/for so to give: give [obj] son: child their to/for famine and to pour them upon hand: power sword and to be woman: wife their childless and widow and human their to be to kill death youth their to smite sword in/on/with battle
22 Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe. Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo ndipo atchera msampha mapazi anga.
to hear: hear outcry from house: home their for to come (in): bring upon them band suddenly for to pierce (pit *Q(K)*) to/for to capture me and snare to hide to/for foot my
23 Koma Inu Yehova, mukudziwa ziwembu zawo zonse zofuna kundipha. Musawakhululukire zolakwa zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu. Agonjetsedwe pamaso panu; muwalange muli wokwiya.”
and you(m. s.) LORD to know [obj] all counsel their upon me to/for death not to atone upon iniquity: crime their and sin their from to/for face: before your not to wipe (and to be *Q(K)*) to stumble to/for face: before your in/on/with time face: anger your to make: do in/on/with them

< Yeremiya 18 >