< Yeremiya 18 >
1 Yehova anawuza Yeremiya kuti,
Slovo, kteréž se stalo k Jeremiášovi od Hospodina, řkoucí:
2 “Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.”
Vstaň a sejdi do domu hrnčířova, a tam způsobím to, abys slyšel slova má.
3 Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero.
I sešel jsem do domu hrnčířova, a aj, on dělal dílo na kruzích.
4 Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.
Když se pak zkazila nádoba v ruce hrnčířově, kterouž on dělal z hliny, tehdy zase udělal z ní nádobu jinou, jakouž se dobře líbilo hrnčíři udělati.
5 Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
I stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
6 “Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya.
Zdaliž jako hrnčíř tento nemohl bych nakládati s vámi, ó dome Izraelský? dí Hospodin. Aj, jakož hlina v ruce hrnčíře, tak jste vy v ruce mé, ó dome Izraelský.
7 Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga,
Mluvil-li bych proti národu a proti království, že je v okamžení vypléním a zkazím, i vyhubím,
8 ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira.
Však odvrátil-li by se národ ten od nešlechetnosti své, proti němuž bych mluvil: i já litoval bych toho zlého, kteréž jsem myslil učiniti jemu.
9 Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu.
Zase mluvil-li bych o národu a o království, že je v okamžení vzdělám a vštípím,
10 Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.
Však činil-li by, což zlého jest před očima mýma, neposlouchaje hlasu mého: i já litoval bych dobrodiní toho, kteréž bych řekl učiniti jemu.
11 “Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’
Protož nyní rci mužům Judským i obyvatelům Jeruzalémským, řka: Takto praví Hospodin: Aj, já strojím na vás zlou věc, a obrátím na vás pohromu; navraťtež se již jeden každý od cesty své zlé, a polepšte cest svých i předsevzetí svých.
12 Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’”
Kteřížto řekli: To nic, nebo za myšlénkami svými půjdeme, a jeden každý zdání srdce svého nešlechetného vykonávati budeme.
13 Yehova akuti, “Uwafunse anthu a mitundu ina kuti: Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi? Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita chinthu choopsa kwambiri.
Protož takto praví Hospodin: Vyptejte se nyní mezi pohany, slýchal-li kdo takové věci? Mrzkosti veliké dopustila se panna Izraelská.
14 Kodi chisanu chimatha pa matanthwe otsetsereka a phiri la Lebanoni? Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
Zdaliž kdo pohrdá čerstvou vodou Libánskou z skály? Zdaž pohrdají vodami studenými odjinud běžícími?
15 Komatu anthu anga andiyiwala; akufukiza lubani kwa mafano achabechabe. Amapunthwa mʼnjira zawo zakale. Amayenda mʼnjira zachidule ndi kusiya njira zabwino.
Lid pak můj zapomenuvše se na mne, kadí marnosti. Nebo k úrazu je přivodí na cestách jejich, na stezkách starobylých, chodíce stezkami cesty neprotřené,
16 Dziko lawo amalisandutsa chipululu, chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse; onse odutsapo adzadabwa kwambiri ndipo adzapukusa mitu yawo.
Tak abych musil obrátiti zemi jejich v poušť na odivu věčnou; každý, kdož by šel skrze ni, aby se užasl, a pokynul hlavou svou.
17 Ngati mphepo yochokera kummawa, ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo; ndidzawafulatira osawathandiza pa tsiku la mavuto awo.”
Větrem východním rozptýlím je před nepřítelem; hřbetem a ne tváří pohledím na ně v čas bídy jejich.
18 Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”
I řekli: Poďte a vymyslme proti Jeremiášovi nějakou chytrost; neboť nezhyne zákon od kněze, ani rada od moudrého, ani slovo od proroka. Poďte a zarazme jej jazykem, a nemějme pozoru na žádná slova jeho.
19 Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni; imvani zimene adani anga akunena za ine!
Pozoruj mne, Hospodine, a slyš hlas těch, kteříž se vadí se mnou.
20 Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino? Komabe iwo andikumbira dzenje. Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu kudzawapempherera kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
Zdaliž má odplacováno býti za dobré zlým, že mi jámu kopají? Rozpomeň se, že jsem se postavoval před oblíčejem tvým, abych se přimlouval k jejich dobrému, a odvrátil prchlivost tvou od nich.
21 Choncho langani ana awo ndi njala; aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga. Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye; amuna awo aphedwe ndi mliri, anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
Protož dopusť na syny jejich hlad, a způsob to, ať jsou násilně zmordování mečem, a nechť jsou ženy jejich osiřelé a ovdovělé, a muži jejich ať jsou ukrutně zmordováni, a mládenci jejich zbiti mečem v boji.
22 Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe. Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo ndipo atchera msampha mapazi anga.
Nechť jest slýchati křik z domů jejich, když přivedeš na ně vojsko náhle. Nebo vykopali jámu, aby popadli mne, a osídla polékli nohám mým;
23 Koma Inu Yehova, mukudziwa ziwembu zawo zonse zofuna kundipha. Musawakhululukire zolakwa zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu. Agonjetsedwe pamaso panu; muwalange muli wokwiya.”
Ješto ty, Hospodine, povědom jsi vší rady jejich o mém usmrcení. Nebuď milostiv nepravosti jejich, a hříchu jejich před tváří svou neshlazuj, ale nechť jsou k úrazu dostrčeni před oblíčejem tvým, a v čas prchlivosti své s nimi zacházej.