< Yeremiya 17 >

1 “Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
“Ekibi kya Yuda kiwandiikiddwa n’ekkalaamu ey’ekyuma n’ejjinja essongovu; kirambiddwa ku mitima gyabwe ne ku mayembe g’ebyoto byabwe.
2 Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
N’abaana baabwe basinziza ku byoto bya bakatonda ba Asera ebiri ku buli muti oguyimiridde era ne ku busozi obuwanvu.
3 Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
Olusozi lwange oluli mu nsi, obugagga bwammwe n’ebintu byo eby’omuwendo byonna, ndibiwaayo byonna binyagibwe n’ebifo byammwe ebigulumivu kwe musaddaakira olw’ekibi ekibunye mu nsi yonna.
4 Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
Musango gwo ggwe nti olifiirwa ensi gye nakuwa okuba omugabo gwo, ndikufuula muddu wa balabe bo mu nsi gy’otomanyangako, kubanga mu busungu bwange omuliro gukoleezeddwa ogunaayakanga emirembe gyonna.”
5 Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
Bw’ati bw’ayogera Mukama nti, Akolimiddwa oyo eyeesiga omuntu era eyeesiga omubiri okuba amaanyi ge, era alina omutima oguva ku Katonda.
6 Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
Aliba ng’ekisaka mu ddungu, ataliraba birungi bwe birijja, naye alibeera mu biwalakate mu ddungu, ensi ey’omunnyo omutali abeeramu.
7 “Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
Naye alina omukisa omusajja oyo eyeesiga Mukama, nga Mukama ly’essuubi lye.
8 Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
Ali ng’omuti ogusimbiddwa awali amazzi, ne gulandiza emirandira gyagwo ku mabbali g’omugga, nga wadde omusana gujja, tegutya n’amakoola gaagwo tegawotoka, so tegulyeraliikirira mu mwaka ogw’ekyeya era teguliremwa kubala bibala.
9 Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
Omutima mulimba okusinga ebintu byonna, era gulwadde endwadde etawonyezeka. Ani ayinza okugutegeera?
10 “Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
“Nze Mukama nkebera omutima, ngezesa emmeeme, okuwa buli muntu ng’amakubo ge bwe gali, ng’ebikolwa bye bwe biri.”
11 Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
Ng’enkwale bw’eyalula amagi geetebiikanga, bw’atyo bw’abeera oyo afuna obugagga mu makubo amakyamu; obulamu bwe nga bwakabeerawo kaseera buseera, bulimuggwaako era oluvannyuma alizuulibwa nga musiru.
12 Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
Ekifo kyaffe ekitukuvu, ntebe ey’ekitiibwa eyagulumizibwa okuva ku lubereberye.
13 Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
Ayi Mukama essuubi lya Isirayiri, bonna abakuvaako baliswala. Abo abakuvaako ne bakuleka baliba ng’abawandiikiddwa mu nfuufu, kubanga bavudde ku Mukama, oluzzi olw’amazzi amalamu.
14 Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
Mponya, Ayi Mukama, nange nnaawona, ndokola nange nnaalokoka, kubanga ggwe gwe ntendereza.
15 Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
Tobakkiriza kuŋŋamba nti, “Ekigambo kya Mukama kiri ludda wa? Ka kituukirire nno kaakano!”
16 Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
Sirekeddaawo kuba musumba wa ndiga zo, omanyi nga sikusabanga kubaleetako nnaku. Byonna ebiva mu kamwa kange tebikukwekeddwa, obimanyi.
17 Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
Toba wa ntiisa gye ndi, ggwe oli buddukiro bwange mu kiseera eky’okulabiramu ennaku.
18 Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
Abo abanjigganya leka baswale, era onkuume nneme kuswala; leka bagwemu ekyekango nze onkuume nneme okwekanga, batuuse ku lunaku olw’ekikangabwa, bazikiririze ddala.
19 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
Bw’ati Mukama bwe yaŋŋamba nti, “Genda oyimirire ku mulyango gw’abantu, bakabaka ba Yuda mwe bayingirira n’okufuluma; yimirira ne ku nzigi endala eza Yerusaalemi.
20 Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
Bagambe nti, ‘Muwulirize ekigambo kya Mukama mmwe bakabaka ba Yuda n’abantu bonna ababeera mu Yerusaalemi, abayita mu miryango gy’ekibuga.
21 Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
Bw’ati bw’ayogera Mukama nti, Weegendereze oleme kufulumya mugugu gwonna mu nnyumba yo wadde okukola omulimu gwonna ku ssabbiiti, naye mukuume olunaku lwa Ssabbiiti nga lutukuvu nga temulukolerako mulimu gwonna,
22 Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
era kuuma olunaku lwa Ssabbiiti nga lutukuvu nga bwe nalagira bajjajjammwe.’
23 Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
Naye tebaawuliriza wadde okukkiriza okunenyezebwa.
24 Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
Kyokka bwe muneegendereza ne muŋŋondera, bw’ayogera Mukama, ‘ne mutayisa kintu kyonna kye mwetisse mu miryango gy’ekibuga ku ssabbiiti, naye ne mukuuma olwa Ssabbiiti nga lutukuvu obutakolerako mulimu gwonna,
25 Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
olwo bakabaka abatuula ku ntebe ya Dawudi bajja kuyita mu miryango gy’ekibuga n’abakungu baabwe. Bo n’abakungu baabwe baakujja ng’abamu bavuga amagaali abalala nga beebagadde embalaasi, nga bawerekeddwako abasajja ba Yuda n’abo abali mu Yerusaalemi era ekibuga kino kiribeerwamu emirembe gyonna.
26 Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
Abantu balijja okuva mu bibuga bya Yuda ne mu byalo ebiriraanye Yerusaalemi, okuva mu bitundu bya Benyamini ne mu biwonvu ne mu nsozi z’ebugwanjuba, n’okuva mu nsi ey’ensozi ey’e Negevu, nga baleeta ebiweebwayo ebyokebwa, ne ssaddaaka, ebiweebwayo eby’empeke, n’obubaane era n’ebiweebwayo eby’okwebaza mu nnyumba ya Mukama.
27 Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”
Naye bwe mutaŋŋondere kukuuma lunaku lwa Ssabbiiti nga lutukuvu ne mwetikkirako emigugu gyammwe nga mufuluma mu nguudo za Yerusaalemi ku lunaku olwa Ssabbiiti, ndikoleeza omuliro ogutazikira mu miryango gya Yerusaalemi oguliyokya ebigo byakyo.’”

< Yeremiya 17 >