< Yeremiya 17 >

1 “Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
TUHAN berkata, "Hai bangsa Yehuda, dosamu telah terukir pada hatimu dan pada semua sudut mezbah-mezbahmu dengan pena besi yang bermata pena dari intan.
2 Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
Orang-orangmu beribadat pada mezbah-mezbah dan tiang-tiang berhala yang telah didirikan untuk Dewi Asyera di setiap pohon yang rindang, di puncak-puncak bukit,
3 Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
dan di gunung-gunung di luar kota. Karena semua tempat penyembahan berhala yang telah kamu dirikan di seluruh negeri dan karena segala dosa yang telah kamu lakukan, maka Aku akan membuat musuh-musuhmu mengangkut segala harta dan kekayaanmu.
4 Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
Kamu akan terpaksa menyerahkan tanah yang telah Kuberikan kepadamu, dan Aku akan membuat kamu mengabdi kepada musuhmu di negeri yang sama sekali asing bagimu. Aku melakukan semuanya itu karena kemarahan-Ku telah meluap seperti api yang menyala dan tak dapat dipadamkan."
5 Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
TUHAN berkata, "Apabila orang meninggalkan Aku, Tuhannya, dan berharap kepada manusia serta bersandar pada kekuatannya, maka Aku akan menghukum dia.
6 Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
Ia seperti tanaman yang tumbuh di padang, di tanah tandus, sunyi sepi dan bergaram, tak pernah ia mengalami kebaikan.
7 “Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
Tapi orang yang berharap kepada-Ku akan Kuberkati selalu.
8 Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
Ia bagaikan pohon di tepi sungai yang mengalir; akarnya merambat sampai ke air. Ia tak takut musim kemarau, daun-daunnya selalu hijau. Sekalipun negeri dilanda kekeringan, ia tak gelisah sebab ia selalu menghasilkan buah.
9 Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
Hati manusia tak dapat diduga, paling licik dari segala-galanya dan terlalu parah penyakitnya.
10 “Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
Aku, TUHAN, menyelidiki hati, batin manusia Kuuji. Setiap orang akan Kubalas menurut tingkah lakunya, dan Kuperlakukan sesuai dengan perbuatannya."
11 Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
Bagaikan burung mengerami telur yang bukan miliknya, begitulah orang yang tak jujur mendapat harta. Pada usia setengah baya ia akan kehilangan semua hartanya. Pada akhir hidupnya terbukti ia orang yang bodoh sekali.
12 Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
Rumah TUHAN kita seperti takhta yang mulia, di gunung yang tinggi sejak semula.
13 Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
TUHAN, Engkaulah harapan Israel, umat-Mu; semua yang meninggalkan Engkau akan menjadi malu. Mereka akan lenyap dari dunia ini dan pergi ke dunia orang mati. Sebab, Engkau sumber air kehidupan telah mereka tinggalkan, ya TUHAN.
14 Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
TUHAN, sembuhkanlah aku, maka aku akan menjadi sehat. Selamatkanlah aku, maka aku akan selamat. Engkau saja yang kumuliakan!
15 Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
Orang berkata kepadaku, "Di mana semua ancaman TUHAN itu? Biarlah sekarang dilaksanakan!"
16 Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
Tapi, ya TUHAN, tak pernah aku mendesak supaya Engkau mendatangkan celaka atas mereka. Aku tidak juga menginginkan supaya mereka ditimpa kemalangan. Engkau tahu itu, TUHAN. Engkau tahu apa yang kuucapkan.
17 Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
Janganlah Engkau menjadi sesuatu yang menakutkan hatiku. Engkau tempat pengungsian bagiku bila datang kesukaran.
18 Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
Semoga yang mengejar dan menindas aku, Kaupermalukan dan Kaupenuhi dengan ketakutan. Tetapi janganlah berbuat begitu terhadap aku, ya TUHAN. Datangkanlah malapetaka ke atas mereka sampai mereka hancur binasa.
19 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
TUHAN berkata kepadaku, "Yeremia, pergilah ke Pintu Gerbang Rakyat yang dilalui raja-raja Yehuda apabila mereka keluar masuk kota. Pergilah juga ke semua pintu gerbang lainnya di Yerusalem.
20 Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
Sampaikanlah pesan-Ku kepada raja-raja dan semua orang Yehuda serta seluruh penduduk Yerusalem yang lewat di pintu-pintu itu.
21 Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
Katakanlah begini: 'Jika kamu tidak ingin mati, janganlah mengangkut barang pada hari Sabat, atau membawanya masuk melalui pintu-pintu gerbang Yerusalem.
22 Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
Jangan bekerja atau membawa barang apa pun keluar dari rumahmu pada hari Sabat. Khususkanlah hari itu untuk Aku seperti yang telah Kuperintahkan kepada leluhurmu.
23 Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
Tapi leluhurmu tidak mau mendengarkan atau memperhatikan apa yang Kukatakan. Mereka keras kepala, dan tidak mau taat atau ditegur.
24 Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
Taatilah semua perintah-Ku. Jangan mengangkut barang apa pun melalui pintu gerbang kota ini pada hari Sabat. Khususkanlah, hari Sabat untuk Aku, dan janganlah mengerjakan apa pun pada hari itu.
25 Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
Jika kamu sungguh-sungguh menjalankan perintah-perintah-Ku itu, maka raja-raja dan pejabat-pejabat yang memerintah seperti Daud akan memasuki gerbang-gerbang kota Yerusalem. Mereka bersama orang Yehuda dan penduduk Yerusalem, akan mengendarai kereta kuda, sehingga kota Yerusalem menjadi ramai sekali.
26 Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
Orang-orang akan datang dari kota-kota Yehuda, dan dari desa-desa di sekitar Yerusalem; mereka akan datang dari wilayah Benyamin, dari daerah kaki bukit, dari daerah pegunungan, dan dari Yehuda bagian selatan. Mereka akan membawa ke Rumah-Ku binatang-binatang kurban, baik yang untuk dibakar maupun yang tidak, juga persembahan gandum dan kemenyan serta persembahan syukur.
27 Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”
Semua itu akan terjadi apabila kamu taat kepada-Ku dan mengkhususkan hari Sabat untuk Aku. Jangan mengangkut barang apa pun lewat pintu-pintu gerbang Yerusalem pada hari itu. Kalau kamu melanggar perintah-perintah-Ku itu, pintu-pintu gerbang Yerusalem serta istana-istananya akan Kubakar habis dan api itu tak akan dapat dipadamkan.'"

< Yeremiya 17 >