< Yeremiya 17 >
1 “Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
Le péché de Juda a été écrit avec une plume de fer et avec une pointe de diamant, et gravé sur l’étendue de leur cœur et sur les cornes de leurs autels.
2 Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
Puisque leurs fils se sont souvenus de leurs autels, et de leurs bois sacrés, et des arbres couverts de feuilles, sur les montagnes élevées,
3 Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
Offrant des sacrifices dans la campagne, j’abandonnerai au pillage ta force et tous tes trésors, et tes hauts lieux à cause de tes péchés commis dans tous tes confins.
4 Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
Et tu seras laissée seule privée de ton héritage que je t’ai donné, et je te rendrai l’esclave de tes ennemis dans une terre que tu ignores, parce que tu as allumé un feu dans ma fureur; jusqu’à jamais il brûlera.
5 Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
Voici ce que dit le Seigneur: Maudit l’homme qui se confie dans l’homme, qui se fait un bras de chair, et dont le cœur se retire du Seigneur.
6 Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
Il sera comme le tamaris qui est dans le désert et il ne verra pas le bonheur, lorsqu’il viendra; mais il habitera dans la sécheresse au désert, dans une terre de salure et inhabitable.
7 “Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
Béni l’homme qui se confie dans le Seigneur, et dont le Seigneur sera l’espérance.
8 Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
Et il sera comme un arbre que l’on transplante sur le bord des eaux, qui étend ses racines vers l’eau qui l’humecte; il ne craindra pas la chaleur, lorsqu’elle viendra. Et sa feuille sera verte, et au temps de la sécheresse il ne sera pas en peine, et jamais il ne cessera de faire du fruit.
9 Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
Le cœur de tous est dépravé et inscrutable; qui le connaîtra?
10 “Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
C’est moi, le Seigneur qui scrute le cœur, et qui éprouve les reins; qui donne à chacun selon sa voie et selon le fruit de ses inventions.
11 Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
La perdrix a couvé des œufs qu’elle n’a pas pondus, ainsi l’injuste a amassé des richesses, mais non avec justice; au milieu de ses jours il abandonnera ses richesses, et à son dernier moment, il sera reconnu insensé.
12 Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
Le trône de gloire, élevé depuis le commencement, est le lieu de notre sanctification.
13 Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
Seigneur, l’attente d’Israël, tous ceux qui vous abandonnent seront confondus; ceux qui se retirent de vous seront écrits sur la terre, parce qu’ils ont abandonné la source des eaux vives, le Seigneur.
14 Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
Guérissez-moi, Seigneur, et je serai guéri; sauvez-moi, et je serai sauvé; parce que ma louange, c’est vous.
15 Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
Voilà qu’eux-mêmes me disent: Où est la parole du Seigneur? qu’elle vienne.
16 Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
Et moi je n’ai pas été troublé, en vous suivant comme pasteur; et le jour d’un homme, je ne l’ai pas désiré, vous le savez. Ce qui est sorti de mes lèvres a été juste en votre présence.
17 Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
Ne me soyez pas à effroi, mon espoir, c’est vous, au jour de l’affliction.
18 Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
Qu’ils soient confondus, ceux qui me persécutent, et que je ne sois pas confondu moi-même; qu’ils tremblent de peur, eux, et que je ne tremble pas moi-même; amenez sur eux un jour d’affliction, et d’un double brisement, brisez-les.
19 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
Voici ce que me dit le Seigneur: Va, et tiens-toi à la porte des fils du peuple, par laquelle les rois de Juda entrent et sortent, et à toutes les portes de Jérusalem;
20 Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
Et tu leur diras: Ecoutez la parole du Seigneur, rois de Juda, tout Juda, et vous tous, habitants de Jérusalem, qui entrez par ces portes.
21 Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
Voici ce que dit le Seigneur: Gardez vos âmes, ne portez point de fardeaux au jour du sabbat, et n’en introduisez point par les portes de Jérusalem.
22 Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
Et ne faites pas sortir de fardeaux hors de vos maisons au jour du sabbat, et vous ne ferez aucun travail; mais sanctifiez le jour du sabbat comme je l’ai ordonné à vos pères.
23 Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
Et ils n’ont pas entendu, et ils n’ont pas incliné leur oreille; mais ils ont rendu leur cou inflexible, afin de ne pas m’entendre, et de ne pas recevoir mes instructions.
24 Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
Et il arrivera que si vous m’écoutez, dit le Seigneur, en sorte que vous n’introduisiez point de fardeaux par les portes de cette ville au jour du sabbat, et si vous sanctifiez le jour du sabbat, si vous ne faites en ce jour aucun travail,
25 Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
Il entrera par les portes de cette ville des rois et des princes qui s’assiéront sur le trône de David, qui seront montés sur leurs chars et sur leurs chevaux, eux et leurs princes, et les hommes de Juda, et les habitants de Jérusalem; et cette ville sera habitée éternellement.
26 Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
Et ils viendront des villes de Juda, et des environs de Jérusalem, et de la terre de Benjamin, et des plaines, et des montagnes, et du midi, portant des holocaustes et des victimes, des sacrifices et de l’encens, et ils les apporteront en offrande dans la maison du Seigneur.
27 Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”
Mais si vous ne m’écoutez pas, si vous ne sanctifiez pas le jour du sabbat, en ne portant point de fardeaux, et n’en introduisant point par les portes de Jérusalem au jour du sabbat, je mettrai le feu à ses portes; et il dévorera les maisons de Jérusalem, et il ne s’éteindra pas.