< Yeremiya 17 >

1 “Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
“The sin of Judah is written with a pen of iron, With the point of a diamond, Engraved on the tablet of their heart, And on the horns of your altars,
2 Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
As their sons remember their altars and their Asherim, By the green tree, by the high hills.
3 Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
O My mountain in the field—your strength, All your treasures—I give for a prey, Your high places for sin in all your borders.
4 Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
And you have let go—even through yourself, Of your inheritance that I gave to you, And I have caused you to serve your enemies, In a land that you have not known, For you have kindled a fire in My anger, It burns for all time.”
5 Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
Thus said YHWH: “Cursed [is] the man who trusts in man, And has made flesh his arm, And whose heart turns from YHWH.
6 Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
And he has been as a naked thing in a desert, And does not see when good comes, And has inhabited parched places in a wilderness, A salt land, and not inhabited.
7 “Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
Blessed [is] the man who trusts in YHWH, And whose confidence has been YHWH.
8 Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
And has been as a tree planted by waters, And he sends forth his roots by a stream, And he does not see when heat comes, And his leaf has been green, And he is not sorrowful in a year of scarcity, Nor does he cease from making fruit.
9 Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
The heart [is] deceitful above all things, And it [is] incurable—who knows it?
10 “Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
I, YHWH, search the heart, try the reins, Even to give to each according to his way, According to the fruit of his doings.
11 Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
A partridge hatching, and not bringing forth, [Is] one making wealth, and not by right, In the midst of his days he forsakes it, And in his latter end—he is a fool.”
12 Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
A throne of glory on high from the beginning, The place of our sanctuary,
13 Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
The hope of Israel [is] YHWH, All forsaking You are ashamed. “And My apostates are written in the earth, For they have forsaken YHWH, A fountain of living waters.”
14 Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
Heal me, O YHWH, and I am healed, Save me, and I am saved, For You [are] my praise.
15 Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
Behold, they are saying to me: “Where [is] the word of YHWH? Pray, let it come.”
16 Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
And I did not hurry from feeding after You, And I have not desired the desperate day, You have known the produce of my lips, It has been before Your face,
17 Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
Do not be to me for a terror, You [are] my hope in a day of calamity.
18 Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
Let my pursuers be ashamed, And do not let me be ashamed—me! Let them be frightened, And do not let me be frightened—me! Bring in on them a day of calamity, And destroy them a second time [with] destruction.
19 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
Thus said YHWH to me: “Go, and you have stood in the gate of the sons of the people, by which kings of Judah come in, and by which they go out, and in all gates of Jerusalem,
20 Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
and you have said to them: Hear a word of YHWH, you kings of Judah, and all Judah, and all inhabitants of Jerusalem, who are coming in by these gates,”
21 Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
Thus said YHWH: “Take heed to yourselves, And you do not bear a burden on the day of rest, Nor have you brought [it] in by the gates of Jerusalem.
22 Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
Nor do you take out a burden from your houses on the day of rest, Indeed, you do not do any work, And you have sanctified the day of rest, As I have commanded your fathers.
23 Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
And they have not listened nor inclined their ear, And they stiffen their neck not to hear, And not to receive instruction.
24 Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
And it has been, if you certainly listen to Me,” A declaration of YHWH, “So as not to bring in a burden by the gates of this city on the day of rest, And to sanctify the day of rest, So as not to do any work in it—
25 Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
Then kings and princes have entered by the gates of this city, Sitting on the throne of David, Riding in a chariot, and on horses, They, and their princes, the man of Judah, And inhabitants of Jerusalem, And this city has remained for all time.
26 Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
And they have come in from cities of Judah, And from outskirts of Jerusalem, And from the land of Benjamin, And from the low country, And from the hill-country, And from the south, Bringing in burnt-offering, and sacrifice, And present, and frankincense, And bringing praise [to] the house of YHWH.
27 Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”
And if you do not listen to Me to sanctify the day of rest, And so as not to bear a burden, And to come in at the gates of Jerusalem on the day of rest, Then I have kindled a fire in its gates, And it has consumed the high places of Jerusalem, And it is not quenched!”

< Yeremiya 17 >