< Yeremiya 17 >

1 “Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
Judas Synd er skreven med en Jerngriffel, med Æggen af en Demant; den er indgravet paa deres Hjertes Tavle og paa deres Altres Horn,
2 Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
ligesom deres Børn ihukomme deres Altre og deres Astartebilleder, ved de grønne Træer, ved Højenes Toppe.
3 Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
Mit Bjerg paa Marken, dit Gods, ja, alt dit Liggendefæ vil jeg give hen til Rov, ja, dine Høje for Synden inden alle dine Landemærker.
4 Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
Og du skal drage ud, og det ved din egen Skyld, fra din Arv, som jeg gav dig, og jeg vil gøre, at du skal tjene dine Fjender i et Land, som du ikke kender; thi I have optændt en Ild i min Vrede, den skal brænde evindelig.
5 Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
Saa siger Herren: Forbandet er den Mand, som forlader sig paa Mennesket og holder Kød for sin Arm, og hvis Hjerte viger fra Herren.
6 Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
Og han skal være som den enlige paa den øde Mark og skal ikke se, at der kommer godt; men han skal bo paa de forbrændte Steder i Ørken, i et Saltland, som ikke kan bebos.
7 “Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
Velsignet den Mand, som forlader sig paa Herren, og hvis Tillid Herren er!
8 Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
Thi han skal være ligesom et Træ, plantet ved Vand, og som udskyder sine Rødder ved Bækken, og som ikke frygter, naar der kommer Hede, og hvis Blad skal være grønt, og som ikke hænger mat, naar et tørt Aar kommer, og ikke lader af at bære Frugt.
9 Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
Hjertet er bedrageligt, mere end alle Ting, og det er sygt; hvo kan kende det?
10 “Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
Jeg Herren er den, som ransager Hjertet og prøver Nyrer, og det for at give hver efter sine Veje, efter sine Idrætters Frugt.
11 Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
Som en Agerhøne, der samler Æg, som den ikke selv har lagt, saaledes er den, som forhverver sig Rigdom, men ikke med Ret; han skal forlade den midt i sine Dage og være en Daare paa sit sidste.
12 Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
Herlighedens Trone, Højheden af Begyndelsen, var vor Helligdoms Sted.
13 Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
Israels Forhaabning, Herre! Alle, som forlade dig, skulle beskæmmes; de, som affalde fra dig, skulle skrives i Jorden, thi de forlode Herren, de levende Vandes Kilde.
14 Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
Herre! læg mig, saa læges jeg; frels mig, saa frelses jeg; thi du er min Ros.
15 Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
Se, de sige til mig: Hvor er Herrens Ord? lad det dog komme!
16 Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
Men jeg søgte ikke at unddrage mig fra som Hyrde at følge dig, jeg har heller ikke begæret den smertelige Dag, du ved det; hvad der er udgaaet af mine Læber, det er for dit Ansigt.
17 Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
Vær mig ikke til Forfærdelse; du er min Tilflugt paa Ulykkens Dag.
18 Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
Lad dem, som forfølge mig, beskæmmes, men lad ikke mig beskæmmes; lad dem forfærdes, men lad ikke mig forfærdes; lad Ulykkens Dag komme over dem, og slaa dem ned med et dobbelt Slag!
19 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
Saa sagde Herren til mig: Gak, og stil dig i Folkets Børns Port, igennem hvilken Judas Konger komme ind, og igennem hvilke de gaa ud, og i alle Jerusalems Porte!
20 Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
Og du skal sige til dem: Hører Herrens Ord, I Judas Konger og al Juda og alle Indbyggere i Jerusalem, I, som gaa ind ad disse Porte.
21 Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
Saa siger Herren: Tager eder i Vare for eders Sjæles Skyld; og bærer ingen Byrde paa Sabbatens Dag, og fører den ikke ind ad Jerusalems Porte.
22 Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
Og I skulle ingen Byrde føre ud af eders Huse paa Sabbatens Dag, og I skulle intet Arbejde gøre; men I skulle helligholde Sabbatens Dag, som jeg bød eders Fædre.
23 Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
Men de hørte ikke og laante ikke Øre, men forhærdede deres Nakke for ikke at høre og for ej at annamme Lære.
24 Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
Og det skal ske, dersom I høre mig, siger. Herren, saa I ikke føre nogen Byrde ind ad denne Stads Porte paa Sabbatens Dag, men derimod holde Sabbatens Dag hellig og ikke gøre noget Arbejde paa den:
25 Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
Da skal der ind ad denne Stads Porte komme Konger og Fyrster, som sidde paa Davids Trone, og som fare paa Vogne og paa Heste, de og deres Fyrster, Judas Mænd og Indbyggerne i Jerusalem; og denne Stad skal blive evindelig.
26 Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
Og de skulle komme fra Judas Stæder og fra Jerusalems Omegn og fra Benjamins Land og fra Lavlandet og fra Bjergene og fra Sydlandet, de, som bringe Brændoffer og Slagtoffer og Madoffer og Virak, og som bringe Takoffer frem til Herrens Hus.
27 Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”
Men dersom I ikke høre mig om at helligholde Sabbatens Dag og om ikke at bære Byrder og gaa ind ad Portene i Jerusalem paa Sabbatens Dag, da vil jeg antænde en Ild i dens Porte, og den skal fortære Jerusalems Paladser og ikke udslukkes.

< Yeremiya 17 >