< Yeremiya 16 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
Потом дође ми реч Господња говорећи:
2 “Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
Немој се женити, и да немаш синове ни кћери на том месту.
3 pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
Јер овако говори Господ за синове и кћери што се роде на том месту и за матере њихове које их роде, и за оце њихове који их роде у тој земљи:
4 adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
Љутом ће смрћу помрети, неће бити оплакани нити ће се погрепсти, биће гној по земљи, и од мача и од глади изгинуће, и мртва ће телеса њихова бити храна птицама небеским и зверима земаљским.
5 Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
Јер овако говори Господ: Не улази у кућу у којој је жалост, и не иди да плачеш нити их жали; јер сам узео мир свој од тог народа, говори Господ, милост и жаљење.
6 Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
Помреће мали и велики у овој земљи, неће бити погребени нити ће се оплакати, нити ће се ко резати ни главе стрићи за њима.
7 Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
Неће им се дати хлеба у жалости да се потеше за мртвим, нити ће их напојити из чаше ради утехе за оцем или за матером.
8 “Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
Тако не улази у кућу у којој је жалост да седиш с њима да једеш и пијеш.
9 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
Јер овако вели Господ над војскама, Бог Израиљев: Ево, ја ћу учинити да на овом месту пред вашим очима и за ваших дана не буде гласа радосног ни гласа веселог, гласа жениковог ни гласа невестиног.
10 “Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
А кад кажеш том народу све ове речи, ако ти кажу: Зашто изрече Господ све то велико зло на нас? И какво је безакоње наше или какав је грех наш, којим згрешисмо Господу Богу свом?
11 Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
Тада им реци: Јер оци ваши оставише мене, говори Господ, и идоше за другим боговима и служише им и клањаше им се, а мене оставише и закон мој не држаше;
12 Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
А ви још горе чините него оци ваши, јер ето идете сваки по мисли срца свог злог не слушајући мене.
13 Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
Зато ћу вас избацити из ове земље у земљу које не познасте ни ви ни оци ваши, и онде ћете служити другим боговима дан и ноћ докле вам не учиним милост.
14 Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
Зато, ево, иду дани, говори Господ, кад се неће више говорити: Тако да је жив Господ који је извео синове Израиљеве из земље мисирске;
15 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
Него: Тако да је жив Господ који је извео синове Израиљеве из земље северне и из свих земаља у које их беше разагнао! Јер ћу их опет довести у земљу њихову коју сам дао оцима њиховим.
16 Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
Гле, ја ћу послати многе рибаре, говори Господ, да их лове, и после ћу послати многе ловце да их лове по свакој гори и по сваком хуму и по раселинама каменим.
17 Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
Јер очи моје пазе на све путеве њихове, нису сакривени од мене, нити је безакоње њихово заклоњено од мојих очију.
18 Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
И платићу им прво двојином за безакоње њихово и за грех њихов, што оскврнише земљу моју стрвима гадова својих, и наследство моје напунише гнусобама својим.
19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
Господе, крепости моја и граде мој и уточиште моје у невољи, к Теби ће доћи народи од крајева земаљских, и рећи ће: Доиста оци наши имаше лаж, и таштину и што ни мало не помаже.
20 Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
Еда ли ће човек начинити себи богове, који ипак нису богови?
21 “Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.
Зато, ево, ја ћу их научити сада, показаћу им руку своју и силу своју, да познаду да ми је име Господ.

< Yeremiya 16 >