< Yeremiya 16 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
The word of Jehovah came to me, saying:
2 “Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
Take thee not a wife; Have no sons or daughters in this place!
3 pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
For thus saith Jehovah concerning the sons and the daughters That are born in this place, And concerning their mothers that bore them, And concerning their fathers that begat them in this land;
4 adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
By deadly diseases shall they die; They shall not be lamented nor buried; They shall become dung upon the face of the earth; By the sword also and by famine shall they be consumed, And their carcasses shall be food for the birds of heaven And the beasts of the earth.
5 Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
For thus saith Jehovah: Enter not into the house of wailing; Go not to lament; Comfort them not! For I have taken away my peace from this people, saith Jehovah, My kindness and mercy.
6 Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
The great and the small in this land shall die; They shall not be buried nor lamented; No one shall cut himself for them, Nor shall any one make himself bald for them.
7 Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
Men shall not break bread for them in their grief, To comfort them for the dead, Nor give them the cup of consolation to drink, On account of a lost father or mother.
8 “Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
Neither enter thou into the house of feasting, To sit down with them to eat and to drink!
9 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
For thus saith Jehovah of hosts, the God of Israel: Behold, I am about to cause to cease from this place, Before your eyes, in your days, The voice of joy and the voice of mirth, The voice of the bridegroom and the voice of the bride.
10 “Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
And when thou shalt have declared to this people all these things, and they shall say to thee, “Why hath Jehovah pronounced against us all this great evil? What is our iniquity, and what our sin, which we have committed against Jehovah our God?”
11 Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
Then shalt thou say to them: Because your fathers have forsaken me, saith Jehovah, And have walked after strange gods, And have served them and worshipped them, And have forsaken me, and not kept my law.
12 Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
And ye yourselves have done worse than your fathers; For, behold, ye walk every one after the perverseness of his evil heart, And do not hearken to me.
13 Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
Therefore will I cast you forth from this land Into a land unknown to you and to your fathers; And there shall ye serve strange gods day and night; For I will show you no favor.
14 Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
Yet behold the days shall come, saith Jehovah, When men shall no more say, “As Jehovah liveth Who brought up the children of Israel from the land of Egypt,”
15 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
But, “As Jehovah liveth Who brought up the children of Israel from the land of the North, And from all the lands whither he had driven them.” For I will bring them again into their own land, Which I gave to their fathers.
16 Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
Behold, I will send many fishers, saith Jehovah, who shall fish them, And then will I send many hunters who shall hunt them From every mountain, and from every hill, and from the holes of the rocks.
17 Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
For mine eyes are upon all their ways; They are not concealed from my view, Nor is their iniquity hidden from mine eyes.
18 Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
And I will requite their former and their repeated iniquities and sins, Because they have polluted my land with carcasses offered to their idols, And filled my inheritance with their abominable things.
19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
O Jehovah, my strength and my fortress, My refuge in the day of distress! To thee shall the nations come from the ends of the earth, And shall say, “Truly our fathers inherited delusion, Vain and unprofitable things.
20 Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
Shall one make for himself gods Which are no gods?”
21 “Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.
Therefore, behold, I will this time cause them to feel, I will cause them to feel my hand and my might, And they shall know that my name is Jehovah.

< Yeremiya 16 >