< Yeremiya 16 >
1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
HERRENs Ord kom til mig således
2 “Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
Du skal ikke tage dig en Hustru og ikke have Sønner eller Døtre på dette Sted.
3 pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
Thi så siger HERREN om de Sønner og Døtre, der fødes på dette Sted, og om Mødrene, som føder dem, og Fædrene, som avler dem i dette Land:
4 adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
En smertefuld Død skal de dø; der skal ikke holdes Dødeklage over dem, og de skal ikke jordes; til Gødning på Marken skal de blive. De skal omkomme ved Sværd og Hunger; deres Lig skal være Hinmmmmelens Fugle og Jordens Dyr til Æde.
5 Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
Thi så sigem HERREN: Kom ikke i Sorgens Hus, gå ikke til Klage, vis dem ikke Medynk, thi jeg lager min Fred fra dette Folk, lyder det fra HERREN, både Nåde og Barmhjerlighed;
6 Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
og store og små skal dø i dette Land og ikke jordes. De skal ikke holde Dødeklage eller ridse Huden eller klippe sig for deres Skyld,
7 Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
bryde Brød til en, der har Sorg, til Trøst for den døde, eller kvæge ham med Trøstebæger for Fader og Moder.
8 “Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
Og kom ikke i et Gildehus for at sidde iblandt dem og spise og drikke;
9 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
thi så siger Hærskarers HERRE, Israels Gud: Se, for eders Øjne og i eders Dage gør jeg på dette Sted Ende på Fryderåb og Glædesråb, Brudgoms Røst og Bruds Røst.
10 “Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
Når du forkynder dette Folk alle disse Ord, og de siger til dig: "Hvorfor udtaler HERREN al den store Ulykke over os, og hvad er det for en Brøde og Synd, vi har gjort mod HERREN vor Gud?"
11 Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
svar dem så: Fordi eders Fædre forlod mig, lyder det fra HERREN, og holdt sig til andre Guder og dyrkede og tilbad dem; mig forlod de og holdt ikke min Lov;
12 Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
og I bærer eder værre ad end eders Fædre, thi se, I vandrer hver efter sit onde Hjertes Stivsind uden at høre mig;
13 Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
derfor slænger jeg eder bort fra dette Land til et Land, I ikke kender, så lidt som eders Fædre, og der skal I dyrke andre Guder både bag og Nat; thi jeg vil ikke give eder Nåde.
14 Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
Se, derfor skal Dage komme, lyder det fra HERREN, da det ikke mere hedder: "Så sandt HERREN lever, der førte Israeliterne op fra Ægypten!"
15 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
men: "Så sandt HERREN lever, der førte Israeliterne op fra Nordens Land og alle de Lande, til hvilke han havde stødt dem bort!" Og jeg fører dem hjem til deres Land, som jeg gav deres Fædre.
16 Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
Se, jeg sender Bud efter Fiskere i Mængde, lyder det fra HERREN, og de skal fiske dem; og siden sender jeg Bud efter Jægere i Mængde, og de skal jage dem fra hvert Bjerg, hver Høj og Klippernes Kløfter.
17 Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
Thi mine Øjne er rettet på alle deres Veje; de er ikke skjult for mig, og deres Brøde er ikke dulgt for mine Øjne.
18 Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
Og først giver jeg dem tvefold Gengæld for deres Brøde og Synd, fordi de vanhelligede mit Land med deres væmmelige Guders Ådsler og fyldte min Arvelod med deres Vederstyggeligheder.
19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
Herre, min Styrke, mit Værn, min Tilflugt i Nødens Stund! Til dig skal Folkeslag komme fra den vide Jord og sige: "Vore Fædre arved kun Løgn, Afguder, ingen af dem hjælper.
20 Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
Kan et Menneske lave sig Guder? De er dog ikke Guder!"
21 “Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.
Se, derfor lader jeg dem mærke, denne Gang lader jeg dem mærke min Hånd og min Styrke; og de skal kende, at mit Navn er HERREN.