< Yeremiya 15 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
Afei Awurade ka kyerɛɛ me se, “Sɛ mpo, Mose ne Samuel begyinaa mʼanim a anka me koma rentɔ nkɔ saa nnipa yi so. Ma womfi mʼani so! Ma wɔnkɔ!
2 Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
Na sɛ wobisa wo se, ‘Ɛhe na yɛnkɔ’ a, ka kyerɛ wɔn se, ‘Sɛɛ na Awurade se: “‘Wɔn a wɔahyɛ owu ama wɔn no, bɛkɔ owu mu; wɔn a wɔahyɛ afoa ama wɔn no bɛtotɔ wɔ afoa ano; wɔn a wɔahyɛ ɔkɔm ama wɔn no, ɔkɔm bɛde wɔn; wɔn a wɔahyɛ nnommumfa ama wɔn no bɛkɔ nnommum mu.’
3 “Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
“Mede adesɛefo ahorow anan bɛba wɔn so,” Awurade na ose, “afoa a ebekunkum wɔn, akraman a wɔbɛtwe wɔn ase akɔ, wim nnomaa ne asase so mmoa a wɔbɛtetew wɔn nam asɛe wɔn.
4 Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
Mɛma wɔayɛ akyiwade ama asase so ahenni nyinaa, esiane nea Yudahene Hesekia babarima Manase yɛɛ wɔ Yerusalem nti.
5 “Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
“Hena na obehu wo mmɔbɔ, Yerusalem? Hena na obegyam wo? Hena na obegyina abisa sɛnea wo ho te?
6 Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
Woapo me,” Awurade na ose. “Wugu akyirisan so ara. Ɛno nti mɛteɛ me nsa wɔ wo so na masɛe wo. Me yam renhyehye me mma wo bio.
7 Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
Mede nhuhuwso apampaa behuhuw wɔn so wɔ asase no kuropɔn apon ano. Mede owu ne ɔsɛe bɛba me nkurɔfo so, efisɛ wɔnsakraa wɔn akwan ɛ.
8 Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
Mɛma wɔn akunafo adɔɔso asen mpoano nwea. Mede ɔsɛefo bɛba owigyinae, abɛhaw wɔn mmerante nanom; mpofirim mede ɔyaw ne ehu bɛba wɔn so.
9 Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
Ɔbeatan a wawo ason bɛtɔ beraw, na wagyaa mu. Ne wia bɛtɔ wɔ bere a ade nsaa ɛ; wobegu nʼanim ase abrɛ no ase. Mede nkae no bɛma afoa wɔ wɔn atamfo anim,” Awurade na ose.
10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
Ao, me na a wowoo me, onipa a asase no sofo nyinaa ne me ham, di aperepere! Memfɛm obi biribi na memmɔɔ bosea mfii obi hɔ ɛ, nanso obiara dome me.
11 Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
Awurade kae se, “Nokware megye wo ama botae pa bi; ampa ara mɛma wʼatamfo apa wo kyɛw wɔ amanehunu ne ahohia mmere mu.
12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
“Onipa betumi abu dade mu dade a efi atifi fam, anaa kɔbere?
13 Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
“Mo ahode ne mo nnwetɛbona mede bɛma sɛ wɔmfom a wɔrentua ka, esiane mo nnebɔne nyinaa wɔ mo man no mu nti.
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
Mede mo bɛyɛ nkoa ama mo atamfo wɔ ɔman a munnim so so, mʼabufuw bɛma ogya adɛw na ɛbɛhyew mo.”
15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
Wote ase, Awurade; kae me na hwɛ me so. Tɔ wɔn a wɔtaa me no so were. Wowɔ abodwokyɛre, mma me nwu; hwɛ sɛnea wo nti wɔbɔ me ahohora.
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
Wo nsɛm bae no, midii; ɛyɛɛ mʼahosɛpɛw ne me koma apɛde, na wo din da me so, Ao, Asafo Awurade Nyankopɔn.
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
Mantena wɔn a wogye wɔn ani fekuw mu, ne wɔn annye wɔn ani; metew me ho tenae, efisɛ wo nsa daa me so na wʼabufuw hyɛɛ me ma.
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
Adɛn nti na me yaw to ntwa da na mʼapirakuru ayɛ akisikuru a ano yɛ den? Wopɛ sɛ woyɛ sɛ nnaadaa asuwa ma me, sɛ asuti a ɛyow ana?
19 Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
Enti sɛɛ na Awurade se, “Sɛ wosakra wʼadwene a megye wo ato mu bio na woasom me; sɛ nsɛm a edi mu fi wʼanom, na ɛnyɛ nsɛm huhuw a, wobɛyɛ me kasamafo. Ma saa nnipa yi nnan mmra wo nkyɛn, na wo de, ɛnsɛ sɛ wodan kɔ wɔn nkyɛn.
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
Mede wo bɛyɛ ɔfasu ama saa nnipa yi, bammɔ fasu a wɔde kɔbere ato; wɔne wo bedi asi nanso wɔrenni wo so nkonim, efisɛ me ne wo wɔ hɔ sɛ meyi wo na magye wo nkwa,” Awurade, na ose.
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”
“Megye wo nkwa afi amumɔyɛfo nsam na mayi wo afi atirimɔdenfo nsam.”

< Yeremiya 15 >