< Yeremiya 15 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
و خداوند مرا گفت: «اگر‌چه هم موسی و سموئیل به حضور من می‌ایستادندجان من به این قوم مایل نمی شد. ایشان را ازحضور من دور انداز تا بیرون روند.۱
2 Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
و اگر به توبگویند به کجا بیرون رویم، به ایشان بگو: خداوندچنین می‌فرماید: آنکه مستوجب موت است به موت و آنکه مستحق شمشیر است به شمشیر وآنکه سزاوار قحط است به قحط و آنکه لایق اسیری است به اسیری.۲
3 “Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
و خداوند می‌گوید: برایشان چهار قسم خواهم گماشت: یعنی شمشیربرای کشتن و سگان برای دریدن و مرغان هوا وحیوانات صحرا برای خوردن و هلاک ساختن.۳
4 Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
وایشان را در تمامی ممالک جهان مشوش خواهم ساخت. به‌سبب منسی ابن حزقیا پادشاه یهودا وکارهایی که او در اورشلیم کرد.۴
5 “Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
زیرا‌ای اورشلیم کیست که بر تو ترحم نماید و کیست که برای تو ماتم گیرد و کیست که یکسو برود تا ازسلامتی تو بپرسد؟۵
6 Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
خداوند می‌گوید: چونکه تومرا ترک کرده، به عقب برگشتی من نیز دست خودرا بر تو دراز کرده، تو را هلاک ساختم زیرا که ازپشیمان شدن بیزار گشتم.۶
7 Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
و ایشان را دردروازه های زمین با غربال خواهم بیخت و قوم خود را بی‌اولاد ساخته، هلاک خواهم نمودچونکه از راههای خود بازگشت نکردند.۷
8 Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
بیوه‌زنان ایشان برایم از ریگ دریا زیاده شده‌اند، پس بر ایشان در وقت ظهر بر مادر جوانان تاراج کننده‌ای خواهم آورد و ترس و آشفتگی رابر شهر ناگهان مستولی خواهم گردانید.۸
9 Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
زاینده هفت ولد زبون شده، جان بداد و آفتاب او که هنوز روز باقی بود غروب کرد و او خجل و رسواگردید. و خداوند می‌گوید: من بقیه ایشان را پیش روی دشمنان ایشان به شمشیر خواهم سپرد.»۹
10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
وای بر من که تو‌ای مادرم مرا مرد جنگجوو نزاع کننده‌ای برای تمامی جهان زاییدی. نه به ربوا دادم ونه به ربوا گرفتم. معهذا هر یک از ایشان مرا لعنت می‌کنند.۱۰
11 Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
خداوند می‌گوید: «البته تورا برای نیکویی رها خواهم ساخت و هر آینه دشمن را در وقت بلا و در زمان تنگی نزد تومتذلل خواهم گردانید.۱۱
12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
آیا آهن می‌تواند آهن شمالی و برنج را بشکند؟۱۲
13 Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
توانگری وخزینه هایت را نه به قیمت، بلکه به همه گناهانت و در تمامی حدودت به تاراج خواهم داد.۱۳
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
و تورا همراه دشمنانت به زمینی که نمی دانی خواهم کوچانید زیرا که ناری در غضب من افروخته شده شما را خواهد سوخت.»۱۴
15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
‌ای خداوند تو این را می‌دانی پس مرا بیادآورده، از من تفقد نما و انتقام مرا از ستمکارانم بگیر و به دیرغضبی خویش مرا تلف منما و بدان که به‌خاطر تو رسوایی را کشیده‌ام.۱۵
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
سخنان تویافت شد و آنها را خوردم و کلام تو شادی وابتهاج دل من گردید. زیرا که به نام تو‌ای یهوه خدای صبایوت نامیده شده‌ام.۱۶
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
در مجلس عشرت کنندگان ننشستم و شادی ننمودم. به‌سبب دست تو به تنهایی نشستم زیرا که مرا ازخشم مملو ساختی.۱۷
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
درد من چرا دایمی است و جراحت من چرا مهلک و علاج ناپذیر می‌باشد؟ آیا تو برای من مثل چشمه فریبنده و آب ناپایدارخواهی شد؟۱۸
19 Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
بنابراین خداوند چنین می‌گوید: «اگربازگشت نمایی من بار دیگر تو را به حضور خودقایم خواهم ساخت و اگر نفایس را از رذایل بیرون کنی، آنگاه تو مثل دهان من خواهی بود وایشان نزد تو خواهند برگشت و تو نزد ایشان بازگشت نخواهی نمود.۱۹
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
و من تو را برای این قوم دیوار برنجین حصاردار خواهم ساخت و باتو جنگ خواهند نمود، اما بر تو غالب نخواهندآمد زیرا خداوند می‌گوید: من برای نجات دادن ورهانیدن تو با تو هستم.۲۰
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”
و تو را از دست شریران خواهم رهانید و تو را از کف ستمکیشان فدیه خواهم نمود.»۲۱

< Yeremiya 15 >