< Yeremiya 15 >
1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
Et l'Eternel me dit: quand Moïse et Samuel se tiendraient devant moi, je n'aurais pourtant point d'affection pour ce peuple; chasse-les de devant ma face, et qu'ils sortent.
2 Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
Que s'ils te disent: où sortirons-nous? Tu leur répondras: ainsi a dit l'Eternel: ceux qui [sont destinés] à la mort [iront] à la mort; et ceux qui [sont destinés] à l’épée [iront] à l’épée; et ceux qui [sont destinés] à la famine, [iront] à la famine; et ceux qui [sont destinés] à la captivité [iront] en captivité.
3 “Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
J'établirai aussi sur eux quatre espèces de [punitions], dit l'Eternel, l'épée pour tuer, et les chiens pour traîner, et les oiseaux des cieux, et les bêtes de la terre pour dévorer et pour détruire.
4 Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
Et je les livrerai à être agités par tous les Royaumes de la terre, à cause de Manassé fils d'Ezéchias, Roi de Juda, pour les choses qu'il a faites dans Jérusalem.
5 “Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
Car qui serait ému de compassion envers toi, Jérusalem? ou qui viendrait se condouloir avec toi? ou qui se détournerait pour s'enquérir de ta prospérité?
6 Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
Tu m'as abandonné, dit l'Eternel, et tu t'en es allée en arrière; c'est pourquoi j'étendrai ma main sur toi, et je te détruirai; je suis las de me repentir.
7 Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
Je les vannerai avec un van aux portes du pays; j'ai désolé [et] fait périr mon peuple, et ils ne se sont point détournés de leur voie.
8 Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
J'ai multiplié ses veuves plus que le sable de la mer, je leur ai amené sur la mère de leur jeunesse un destructeur en plein midi, j'ai fait tomber subitement sur elle l'ennemi et les frayeurs.
9 Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
Celle qui en avait enfanté sept est devenue languissante, elle a rendu l'esprit, son soleil lui est couché pendant qu'il était encore jour, elle a été rendue honteuse et confuse; et je livrerai son reste à l'épée devant leurs ennemis, dit l'Eternel.
10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
Malheur à moi, ô ma mère! de ce que tu m'as enfanté pour être un homme de débat, et un homme de querelle à tout le pays; je ne me suis obligé à personne, et personne ne s'est obligé à moi, et néanmoins chacun me maudit et me méprise.
11 Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
[Alors l'Eternel dit: ] ceux qui seront restés de toi ne viendront-ils pas à bien? et ne ferai-je pas que l'ennemi viendra au devant de toi au temps de la calamité, et au temps de la détresse?
12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
Le fer usera-t-il le fer de l'Aquilon, et l'acier?
13 Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
Je livrerai au pillage, sans en faire le prix, tes richesses et tes trésors; et cela à cause de tous tes péchés, et même par toutes tes contrées.
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
Et je ferai passer tes ennemis par un pays que tu ne connais point, car le feu a été allumé en ma colère, il sera allumé sur vous.
15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
Eternel, tu le connais, souviens-toi de moi, et me visite, et me venge de ceux qui me persécutent; ne m'enlève point, quand tu auras longtemps différé ta colère; connais que j'ai souffert opprobre pour l'amour de toi.
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
Tes paroles se sont-elles trouvées? je les ai [aussitôt] mangées; et ta parole m'a été en joie, et elle a été l'allégresse de mon cœur; car ton Nom est réclamé sur moi, ô Eternel! Dieu des armées.
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
Je ne me suis point assis au conventicule des railleurs, et je ne m'y suis point réjoui; mais je me suis tenu assis tout seul, à cause de ta main, parce que tu m'as rempli d'indignation.
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
Pourquoi ma douleur est-elle [rendue] continuelle, et ma plaie est-elle sans espérance? elle a refusé d'être guérie; me serais-tu bien comme une chose qui trompe? [comme] des eaux qui ne durent pas?
19 Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
C'est pourquoi ainsi a dit l'Eternel: si tu te retournes, je te ramènerai, et tu te tiendras devant moi; et si tu sépares la chose précieuse de la méprisable, tu seras comme ma bouche; qu'ils se retournent vers toi, mais toi ne retourne pas vers eux.
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
Et je te ferai être à l'égard de ce peuple une muraille d'acier bien forte; ils combattront contre toi, mais ils n'auront point le dessus contre toi, car je [suis] avec toi pour te garantir, et pour te délivrer, dit l'Eternel.
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”
Et je te délivrerai de la main des malins, et te rachèterai de la main des terribles.