< Yeremiya 14 >
1 Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
Which it came [the] word of Yahweh to Jeremiah on [the] matters of the droughts.
2 “Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
It is in mourning Judah and gates its they are languishing they are in mourning to the earth and [the] outcry of Jerusalem it has gone up.
3 Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
And noble [ones] their they have sent (servants their *Q(K)*) for water they have come to [the] cisterns not they have found water they have returned vessels their empty they are ashamed and they are humiliated and they have covered head their.
4 Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
For sake of the ground [which] it is cracked for not it has come rain in the land they are ashamed farmers they have covered head their.
5 Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
For also a doe in the field it has given birth and it has abandoned for not it is grass.
6 Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
And wild donkeys they have stood on [the] bare heights they have panted for breath like jackals they have failed eyes their for there not [is] vegetation.
7 Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
Though iniquities our they have testified against us O Yahweh act for [the] sake of name your for they are many apostasies our to you we have sinned.
8 Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
O hope of Israel deliverer its in a time of distress why? are you like a sojourner in the land and like a traveler [who] he has turned aside to spend [the] night.
9 Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
Why? are you like a person astounded like a warrior [who] not he is able to save and you [are] in midst our O Yahweh and name your on us it is called may not you abandon us.
10 Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
Thus he says Yahweh of the people this thus they have loved to wander feet their not they have restrained and Yahweh not he has accepted them now he will remember iniquity their so he may punish sins their.
11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
And he said Yahweh to me may not you pray for the people this for good.
12 Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
For they will fast not I [will be] listening to cry of entreaty their even if they will offer up a burnt offering and a grain offering not I [will be] accepting them for by the sword and by famine and by pestilence I [will be] bringing to an end them.
13 Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
And I said alas! - O Lord Yahweh here! the prophets [are] saying to them not you will see sword and famine not it will happen to you for peace of reliability I will give to you in the place this.
14 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
And he said Yahweh to me falsehood the prophets [are] prophesying in name my not I sent them and not I appointed them and not I spoke to them a vision of falsehood and divination (and an idol *Q(K)*) (and [the] deceitfulness of *Q(k)*) own heart their they [are] prophesying to you.
15 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
Therefore thus he says Yahweh on the prophets who are prophesying in name my and I not I sent them and they [are] saying sword and famine not it will happen in the land this by the sword and by famine they will meet their end the prophets those.
16 Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
And the people whom they [are] prophesying to them they will be thrown out in [the] streets of Jerusalem because of - the famine and the sword and not a burier [will belong] to them them wives their and sons their and daughters their and I will pour out on them wickedness their.
17 “Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
And you will speak to them the word this let them run down eyes my tear[s] night and by day and may not they cease for a breaking great she has been broken [the] virgin of [the] daughter of people my a wound made sick very.
18 Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
If I went out the field and there! [those] slain of a sword and if I went the city and there! diseases of famine for both prophet as well as priest they have gone about to a land and not they know.
19 Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
¿ Really have you rejected Judah or? Zion does it abhor self your why? have you struck us and not [belongs] to us healing we waited eagerly for peace and there not [was] good and for a time of healing and there! terror.
20 Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
We know O Yahweh wickedness our [the] iniquity of ancestors our for we have sinned to you.
21 Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
May not you spurn for [the] sake of name your may not you treat with contempt [the] throne of glory your remember may not you break covenant your with us.
22 Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.
¿ [are] there Among [the] vanities of the nations [those who] send rain and or? the heavens do they give copious showers ¿ not you [is] it O Yahweh God our so we may wait eagerly for you for you you have done all these [things].