< Yeremiya 13 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.”
Так промовив до мене Господь: „Іди й купи собі льняно́го пояса, і підпережи́ ним свої сте́гна, але в воду не клади́ його“.
2 Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.
І купив я того пояса за Господнім словом, та й підпереза́в свої сте́гна.
3 Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti,
І було мені слово Господнє удруге, говорячи:
4 “Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”
„Візьми того пояса, якого купив, що на сте́гнах твоїх, і встань, іди до Ефрату, та й сховай його там у розщі́лині ске́лі“.
5 Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.
І пішов я, і сховав його в Ефраті, як Господь наказав був мені.
6 Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.”
І сталося по багатьох днях, і сказав мені Господь: „Устань, іди до Ефрату, і візьми звідти того пояса, що Я наказав був тобі сховати його там“.
7 Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.
І пішов я до Ефрату, і викопав, і взяв того пояса з місця, де я сховав був його, — аж ось той пояс незда́тний!
8 Pamenepo Yehova anandiwuza kuti,
І було мені слово Господнє, говорячи:
9 “Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
„Так говорить Господь: Отак зни́щу Я Юдину гордість та гордість велику Єрусалиму,
10 Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu.
цього злого наро́да, що не хоче він слухатися Моїх слів, що ходить за впертістю серця свого! І пішов він в сліди інших богі́в, щоб служити їм та поклонятися їм. І станеться він, як цей пояс, — до нічо́го незда́тний!
11 Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.
Бо як приляга́є цей пояс до сте́гон чоловіка, так притверди́в Я до себе ввесь Ізраїлів дім та ввесь Юдин дім, — говорить Госпо́дь, — щоб стали наро́дом Мені і йме́нням, і хвало́ю та пишното́ю, — та вони не послухались!
12 “Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’
І скажеш до них оце слово: Так говорить Господь, Бог Ізраїлів: усякий бурдю́к вином наповня́ється. І відкажуть тобі: „Чи ми справді не знаєм, що всякий бурдю́к вином наповня́ється?“
13 Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu.
І скажеш до них: Так говорить Господь: Ось напо́вню Я п'я́нством усіх ме́шканців кра́ю цього́, і царів, що сидять на Давидовім троні, і священиків, і пророків, і всіх ме́шканців Єрусалиму.
14 Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’”
І розіб'ю́ їх одно́го об о́дного, ра́зом батькі́в та сині́в, говорить Господь, — Не зми́луюся, і не змилосе́рджусь, і не пожалію, щоб їх не пони́щити!
15 Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu, musadzitukumule, pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
Послухайте ви та візьміть до ушей, — не виви́щуйтеся, бо Господь це сказав!
16 Lemekezani Yehova Mulungu wanu asanagwetse mdima, mapazi anu asanayambe kupunthwa mʼchisisira chamʼmapiri. Asanasandutse kuwala mukuyembekezerako kukhala mdima wandiweyani.
Дайте Господу, Богові вашому, славу, поки не зробить Він те́мно, і по́ки на те́мних гора́х не спіткну́ться вам ноги! І будете ви сподіва́тися сві́тла, а Він зробить це те́мрявою та вчинить імло́ю.
17 Koma ngati simumvera, ndidzalira kwambiri chifukwa cha kunyada kwanu. Mʼmaso mwanga mwadzaza ndi misozi yowawa chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.
А коли ви цього́ не послу́хаєте, буде плакати таємно душа моя з вашої го́рдости, й око моє проливатиме сльо́зи, і зайде́ться сльозою, бо ста́до Господнє займу́ть у поло́н!
18 Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti, “Tsikani pa mipando yaufumuyo, pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo zagwa pansi.”
Скажіть до царя й до царе́вої матері: Сідайте додо́лу, бо з голів ваших спала корона вашої слави!
19 Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo, watengedwa yense ukapolo.
Півде́нні міста позами́кані будуть, і не буде, хто б їх відчини́в, — ви́гнаний буде ввесь Юда, вигнаний буде цілко́м!
20 Tukula maso ako kuti uwone amene akubwera kuchokera kumpoto. Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti, nkhosa zanu zokongola zija?
Зведіть ваші о́чі, й побачте отих, що прихо́дять із пі́вночі: де череда́ та, що да́на тобі, ота́ра пишно́ти твоєї?
21 Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira? Kodi sudzamva zowawa ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
Що ти скажеш, о до́чко Сіону, як Він над тобою пана́ми поставить отих, яких ти навчила була́ за дові́рених бути, — чи ж му́ки не схо́плять тебе, немов ту породі́ллю?
22 Ndipo ngati udzadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?” Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri kuti zovala zanu zingʼambike ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
коли ж скажеш у серці своєму: „Чому́ такі речі спітка́ли мене?“— за числе́нні провини твої відкриті подо́лки твої, ого́лені ноги твої силомі́ць!
23 Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake, kapena kambuku kusintha mawanga ake? Inunso amene munazolowera kuchita zoyipa simungathe kusintha.
Чи му́рин відмі́нить коли свою шкі́ру, а панте́ра — ті пля́ми свої? Тоді зможете й ви чинити добре, навче́ні чинити лихе́!
24 “Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
Тому́ розпоро́шу їх, мов ту поло́ву, що з вітром з пустині летить:
25 Limeneli ndiye gawo lanu, chilango chimene ndakukonzerani chifukwa chondiyiwala Ine ndi kutumikira milungu yabodza, akutero Yehova.
Оце жеребо́к твій, це у́діл, який Я відмі́ряв тобі, — говорить Господь, — бо забула Мене та наді́ялася на непра́вду!
26 Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso kuti umaliseche wanu uwonekere.
І закочу́ теж подо́лки твої над обличчя твоє, — і пока́жеться га́ньба твоя:
27 Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu ndi ziwerewere zanu, zochitika pa mapiri ndi mʼminda. Tsoka iwe Yerusalemu! Udzakhala wosayeretsedwa pa zachipembedzo mpaka liti?”
твої перелю́бства й іржа́ння твої, сором блу́ду твого на полі на па́гірках, — Я бачив гидо́ти твої. Горе тобі, Єрусалиме, що не очи́стишся! Доки ж іще?“

< Yeremiya 13 >