< Yeremiya 13 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.”
Сия глаголет Господь ко мне: иди и стяжи себе чресленик льняный и препояши того на чреслех твоих, и в воду да не внесеши того.
2 Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.
И стяжах чресленик по словеси Господню и обложих окрест чресл моих.
3 Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti,
И бысть слово Господне ко мне вторицею, рекущее:
4 “Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”
возми чресленик, егоже стяжал еси, иже есть окрест чресл твоих, и востани и иди ко Евфрату, и скрый того тамо во разселине каменне.
5 Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.
И идох и скрых того во Евфрате, якоже заповеда мне Господь.
6 Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.”
И бысть по днех мнозех, и рече Господь ко мне: востани и иди ко Евфрату, и возми оттуду чресленик, егоже заповедах тебе скрыти тамо.
7 Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.
И идох ко Евфрату и раскопах, и взях чресленик от места, идеже скрых его, и се, изгнил бе (чресленик), яко ни на чтоже быти потребну ему.
8 Pamenepo Yehova anandiwuza kuti,
И бысть слово Господне ко мне, рекущее: сия глаголет Господь:
9 “Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
тако согнити сотворю гордыню Иудину и гордыню Иерусалимлю, многую гордыню сию людий сих строптивых,
10 Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu.
иже не хотят послушати словес Моих, ходящих во строптивстве сердца своего и шедших вслед богов чуждих, да служат им и да покланяются им: и будут якоже чресленик той, иже ни к чему потребен.
11 Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.
Зане, якоже придержится чресленик ко чреслом мужа, тако прилепих Мне (весь) дом Израилев и весь дом Иудин, рече Господь: да будут Мне в люди имениты, и в хвалу и в славу, и не послушаша Мене.
12 “Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’
И речеши к людем сим словеса сия: тако рече Господь Бог Израилев: всяк мех исполнится вина. И будет, аще рекут к тебе: еда ведяще не увемы, яко всяк мех исполнится вина?
13 Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu.
И речеши к ним: сия глаголет Господь: се, Аз исполню всех обитателей земли сея, и царей их седящих от колена Давидова на престоле их, и священники и пророки, и Иуду и всех обитающих во Иерусалиме пиянством,
14 Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’”
и расточу их, мужа и брата его, и отцы их и сыны их вкупе: не пожелаю, рече Господь, не пощажу, и не умилосердюся, еже не погубити их.
15 Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu, musadzitukumule, pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
Слышите и внемлите, и не возноситеся, яко Господь глаголал есть.
16 Lemekezani Yehova Mulungu wanu asanagwetse mdima, mapazi anu asanayambe kupunthwa mʼchisisira chamʼmapiri. Asanasandutse kuwala mukuyembekezerako kukhala mdima wandiweyani.
Дадите Господу Богу вашему славу прежде даже не смеркнется и прежде даже не преткнутся нозе ваши ко горам темным: и пождете света, и тамо сень смертная, и положени будут во мрак.
17 Koma ngati simumvera, ndidzalira kwambiri chifukwa cha kunyada kwanu. Mʼmaso mwanga mwadzaza ndi misozi yowawa chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.
Аще же не послушаете, в тайне восплачется душа ваша от лица гордыни и плачя восплачет, и изведут очи ваши слезы, яко сотрено есть стадо Господне.
18 Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti, “Tsikani pa mipando yaufumuyo, pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo zagwa pansi.”
Рцыте царю и владыкам: смиритеся, сядите, яко взятся от главы вашея венец славы вашея.
19 Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo, watengedwa yense ukapolo.
Грады южнии затворени суть, и несть отверзаяй: преведен есть весь Иуда, совершиша преселение совершенное.
20 Tukula maso ako kuti uwone amene akubwera kuchokera kumpoto. Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti, nkhosa zanu zokongola zija?
Воздвигни очи твои, Иерусалиме, и виждь приходящыя от севера: где стадо даное тебе, овцы славы твоея?
21 Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira? Kodi sudzamva zowawa ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
Что речеши, егда посетят тя? И ты научил еси их на тя учением в началство: еда не оымут тя болезни яко жену родящую?
22 Ndipo ngati udzadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?” Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri kuti zovala zanu zingʼambike ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
Аще же речеши в сердцы твоем: почто приидоша ми сия? За множество беззакония твоего откровена суть задняя твоя, да обруганы будут стопы твоя.
23 Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake, kapena kambuku kusintha mawanga ake? Inunso amene munazolowera kuchita zoyipa simungathe kusintha.
Аще пременит Ефиоплянин кожу свою, и рысь пестроты своя, и вы можете благотворити научившеся злу.
24 “Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
И развею их, яко стеблие носимое ветром в пустыню.
25 Limeneli ndiye gawo lanu, chilango chimene ndakukonzerani chifukwa chondiyiwala Ine ndi kutumikira milungu yabodza, akutero Yehova.
Сей жребий твой и часть непокорства твоего на Мя, глаголет Господь, яко забыл еси Мя и надеялся на лжу:
26 Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso kuti umaliseche wanu uwonekere.
темже и аз обнажу бедры твоя противу лица твоего, и явится срамота твоя
27 Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu ndi ziwerewere zanu, zochitika pa mapiri ndi mʼminda. Tsoka iwe Yerusalemu! Udzakhala wosayeretsedwa pa zachipembedzo mpaka liti?”
и прелюбодейство твое, и ржание твое и отчуждение блуда твоего: на горах и на селех видех мерзости твоя. Горе тебе, Иерусалиме, яко не очистился еси, последуя мне. Доколе еще?

< Yeremiya 13 >