< Yeremiya 13 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.”
Yahvé m'a dit: « Va, achète-toi une ceinture de lin, mets-la à ta taille, et ne la mets pas dans l'eau. »
2 Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.
Et j'ai acheté une ceinture, selon la parole de Yahvé, et je l'ai mise à ma taille.
3 Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti,
La parole de Yahvé me fut adressée pour la seconde fois, en ces termes:
4 “Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”
« Prends la ceinture que tu as achetée et qui est à ta taille, lève-toi, va jusqu'à l'Euphrate, et là, cache-la dans une fente du rocher. »
5 Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.
Je suis donc allé le cacher près de l'Euphrate, comme Yahvé me l'avait ordonné.
6 Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.”
Au bout de plusieurs jours, Yahvé me dit: « Lève-toi, va vers l'Euphrate, et prends là la ceinture que je t'ai ordonné d'y cacher. »
7 Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.
Puis je suis allé jusqu'à l'Euphrate, j'ai creusé, et j'ai retiré la ceinture du lieu où je l'avais cachée; et voici, la ceinture était en ruine. Elle n'avait servi à rien.
8 Pamenepo Yehova anandiwuza kuti,
Alors la parole de l'Éternel me fut adressée, en ces mots:
9 “Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
L'Éternel dit: C'est ainsi que je détruirai l'orgueil de Juda et la grande fierté de Jérusalem.
10 Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu.
Ce peuple méchant, qui refuse d'entendre mes paroles, qui marche dans l'obstination de son cœur, et qui est allé après d'autres dieux pour les servir et se prosterner devant eux, sera comme cette ceinture, qui ne sert à rien.
11 Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.
Car, comme la ceinture s'attache à la taille d'un homme, ainsi j'ai fait s'attacher à moi toute la maison d'Israël et toute la maison de Juda, dit Yahvé, pour qu'elles soient pour moi un peuple, un nom, une louange et une gloire, mais elles n'ont pas voulu écouter.
12 “Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’
C'est pourquoi tu leur diras cette parole: « L'Éternel, le Dieu d'Israël, dit: Tout récipient doit être rempli de vin ». Ils te diront: « Ne savons-nous pas que tout récipient doit être rempli de vin? »
13 Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu.
Alors dis-leur: « L'Éternel dit: Voici que je vais remplir d'ivresse tous les habitants de ce pays, les rois assis sur le trône de David, les prêtres, les prophètes, et tous les habitants de Jérusalem.
14 Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’”
Je les écraserai les uns contre les autres, les pères et les fils ensemble, dit l'Éternel: « Je n'aurai ni pitié, ni épargne, ni compassion, pour ne pas les détruire. »'"
15 Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu, musadzitukumule, pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
Écoutez, et prêtez l'oreille. Ne sois pas fier, car Yahvé a parlé.
16 Lemekezani Yehova Mulungu wanu asanagwetse mdima, mapazi anu asanayambe kupunthwa mʼchisisira chamʼmapiri. Asanasandutse kuwala mukuyembekezerako kukhala mdima wandiweyani.
Rendez gloire à Yahvé votre Dieu, avant qu'il ne provoque l'obscurité, et avant que vos pieds ne trébuchent sur les montagnes sombres, et pendant que vous cherchez la lumière, il la transforme en ombre de la mort, et en fait une obscurité profonde.
17 Koma ngati simumvera, ndidzalira kwambiri chifukwa cha kunyada kwanu. Mʼmaso mwanga mwadzaza ndi misozi yowawa chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.
Mais si vous ne voulez pas l'entendre, mon âme pleurera en secret votre orgueil. Mon œil pleurera amèrement, et ruisselant de larmes, car le troupeau de Yahvé a été emmené en captivité.
18 Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti, “Tsikani pa mipando yaufumuyo, pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo zagwa pansi.”
Dis au roi et à la reine mère, « Humiliez-vous. Asseyez-vous, car vos couronnes sont tombées, même la couronne de ta gloire.
19 Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo, watengedwa yense ukapolo.
Les villes du Sud sont fermées, et il n'y a personne pour les ouvrir. Juda est emmené en captivité: tous. Ils sont entièrement emportés captifs.
20 Tukula maso ako kuti uwone amene akubwera kuchokera kumpoto. Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti, nkhosa zanu zokongola zija?
Lève les yeux, et voir ceux qui viennent du nord. Où est le troupeau qui vous a été donné, votre beau troupeau?
21 Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira? Kodi sudzamva zowawa ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
Que direz-vous lorsqu'il établira à votre tête ceux que vous avez vous-même appris à être vos amis? Les douleurs ne vous saisiront-elles pas, comme une femme en travail?
22 Ndipo ngati udzadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?” Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri kuti zovala zanu zingʼambike ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
Si tu dis dans ton cœur, « Pourquoi ces choses sont-elles venues sur moi? » Vos jupes sont découvertes à cause de la grandeur de votre iniquité, et vos talons subissent des violences.
23 Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake, kapena kambuku kusintha mawanga ake? Inunso amene munazolowera kuchita zoyipa simungathe kusintha.
L'Éthiopien peut-il changer de peau, ou le léopard ses taches? Alors puissiez-vous aussi faire le bien, qui ont l'habitude de faire le mal.
24 “Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
« C'est pourquoi je les disperserai comme le chaume qui passe par le vent du désert.
25 Limeneli ndiye gawo lanu, chilango chimene ndakukonzerani chifukwa chondiyiwala Ine ndi kutumikira milungu yabodza, akutero Yehova.
C'est votre lot, la part que je vous ai mesurée, dit Yahvé, « parce que tu m'as oublié, et se sont confiés au mensonge. »
26 Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso kuti umaliseche wanu uwonekere.
C'est pourquoi je découvrirai aussi tes jupes sur ton visage, et votre honte apparaîtra.
27 Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu ndi ziwerewere zanu, zochitika pa mapiri ndi mʼminda. Tsoka iwe Yerusalemu! Udzakhala wosayeretsedwa pa zachipembedzo mpaka liti?”
J'ai vu vos abominations et vos adultères. et ton hennissement, la débauche de ta prostitution, sur les collines dans le champ. Malheur à toi, Jérusalem! Vous ne serez pas purifié. Combien de temps cela va-t-il encore durer? »

< Yeremiya 13 >