< Yeremiya 12 >

1 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
Ulungile wena Nkosi, lapho ngiphikisana lawe; kanti ngizakhuluma lawe ngezahlulelo zakho. Kungani indlela yabakhohlakeleyo iphumelela? Kungani behlezi kuhle bonke abenza inkohliso ngenkohliso?
2 Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
Ubahlanyele, yebo, bagxilile impande; bayaqhubeka, yebo, bathele izithelo; useduze emlonyeni wabo, kanti ukhatshana lezinso zabo.
3 Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
Kodwa wena, Nkosi, uyangazi, ungibonile, wahlola inhliziyo yami ngakuwe. Bahudule njengezimvu zokuhlatshwa, ubehlukanisele usuku lokuhlatshwa.
4 Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
Koze kube nini ilizwe lilila, lohlaza lweganga lonke lubuna? Ngenxa yobubi babakhileyo kulo izinyamazana lenyoni ziyabhubha; ngoba bathi: Kayiyikubona isiphetho sethu.
5 Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
Uba ugijime labezinyawo, bakudinisa, pho, ungancintisana njani lamabhiza? Uba uthembela elizweni elilokuthula, pho, uzakwenza njani ekukhukhumaleni kweJordani?
6 Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
Ngoba ngitsho abafowenu lendlu kayihlo, ngitsho labo bakuphatha ngenkohliso, yebo, bona bayamemeza emva kwakho ngokugcweleyo; ungabakholwa, loba bekhuluma izinto ezinhle kuwe.
7 “Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
Ngiyidelile indlu yami, ngilitshiyile ilifa lami; nginikele othandiweyo womphefumulo wami esandleni sezitha zakhe.
8 Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
Ilifa lami kimi linjengesilwane ehlathini; lingiphumisele ilizwi; ngakho-ke ngilizondile.
9 Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
Ilifa lami kimi linjengenyoni elamabalabala edla inyama, inyoni ezidla inyama ziyihanqile zimelene layo; wozani, libuthe zonke izilo zeganga, lizilethe ukuthi zidle.
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
Abelusi abanengi basichithile isivini sami, banyathelele phansi isabelo sami, basenzile isabelo sami esiloyisekayo saba yinkangala elunxiwa.
11 Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
Basenze saba lunxiwa, sililela kimi silunxiwa; ilizwe lonke lilunxiwa, ngoba kakulamuntu okubeka enhliziyweni.
12 Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
Abachithi bafikile phezu kwawo wonke amadundulu enkangala; ngoba inkemba yeNkosi izakudla kusukela komunye umkhawulo welizwe kusiya komunye umkhawulo welizwe; kakulakuthula kuyo yonke inyama.
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
Bahlanyele ingqoloyi, kodwa bazavuna ameva; bazihluphe, kabayikuzuza; njalo lizakuba lenhloni ngezivuno zenu, ngenxa yokuvutha kolaka lweNkosi.
14 “Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
Itsho njalo iNkosi: Mayelana labo bonke omakhelwane bami ababi abathinta ilifa engenze isizwe sami uIsrayeli ukuthi sidle ilifa lalo: Khangela, ngizabasiphuna elizweni labo, ngiyisiphune indlu yakoJuda isuke phakathi kwabo.
15 Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
Kuzakuthi-ke emva kokubasiphuna kwami, ngizabuya ngibe lesihawu kubo, ngibabuyise, kube ngulowo lalowo elifeni lakhe, langulowo lalowo elizweni lakhe.
16 Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
Kuzakuthi-ke uba bezazifunda ngokukhuthala izindlela zabantu bami, ukuthi bafunge ngebizo lami bathi: Kuphila kukaJehova; njengalokho bafundisa abantu bami ukufunga ngoBhali, khona bezakwakhiwa phakathi kwabantu bami.
17 Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.
Kodwa uba bengalaleli, ngizasisiphuna lesosizwe, ngisisiphune ngisibhubhise, itsho iNkosi.

< Yeremiya 12 >