< Yeremiya 12 >
1 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
Tu demeures juste, ô Éternel, quand je conteste avec toi; toutefois je parlerai de jugements avec toi. Pourquoi la voie des méchants prospère-t-elle? Pourquoi sont-ils en paix tous ceux qui agissent perfidement?
2 Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
Tu les as plantés, ils ont pris racine. Ils avancent, même ils fructifient. Tu es près de leur bouche, mais loin de leur cœur.
3 Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
Mais toi, Éternel! tu me connais, tu me vois, et tu éprouves quel est mon cœur envers toi. Traîne-les comme des brebis qu'on doit égorger, et prépare-les pour le jour du carnage!
4 Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
Jusqu'à quand le pays sera-t-il dans le deuil, et l'herbe de tous les champs sera-t-elle desséchée? A cause de la malice de ses habitants, les bêtes et les oiseaux disparaissent. Car ils disent: Il ne verra pas notre fin.
5 Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
Si tu as couru avec les gens de pied et qu'ils t'aient lassé, comment lutteras-tu d'ardeur avec les chevaux? Et si tu n'es en assurance que dans une terre de paix, que feras-tu devant l'orgueil du Jourdain?
6 Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
Car même tes frères et la maison de ton père, même ceux-là sont perfides envers toi, même ceux-là crient à plein gosier derrière toi. Ne les crois pas, quand même ils te parleront amicalement.
7 “Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
J'ai abandonné ma maison; j'ai délaissé mon héritage; j'ai livré ce que mon âme aimait, aux mains de ses ennemis.
8 Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
Mon héritage a été pour moi comme un lion dans la forêt; il a jeté son cri contre moi; c'est pourquoi je l'ai pris en haine.
9 Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
Mon héritage m'est-il un oiseau de diverses couleurs, que les oiseaux de proie fassent cercle autour de lui? Allez, rassemblez toutes les bêtes des champs; amenez-les pour le dévorer.
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
De nombreux bergers ont ravagé ma vigne; ils ont foulé mon partage; ils ont réduit mon beau partage en un désert affreux.
11 Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
On en fait une solitude; il est désolé, il est en deuil devant moi. Tout le pays devient désolé, car personne n'y a rien pris à cœur.
12 Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
Sur tous les lieux élevés du désert les destructeurs viennent; car l'épée de l'Éternel dévore le pays d'un bout à l'autre; il n'y a de paix pour personne.
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
Ils ont semé du froment, et ils moissonnent des épines; ils se sont fatigués sans profit. Soyez honteux de vos récoltes, à cause de l'ardeur de la colère de l'Éternel!
14 “Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
Ainsi a dit l'Éternel contre tous mes mauvais voisins, qui mettent la main sur l'héritage que j'ai fait hériter à mon peuple d'Israël: Voici, je vais les arracher de leur pays, et j'arracherai la maison de Juda du milieu d'eux.
15 Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
Mais il arrivera qu'après les avoir arrachés, j'aurai encore compassion d'eux, et je les ferai retourner chacun à son héritage et chacun à sa terre.
16 Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
Et il arrivera que, s'ils apprennent les voies de mon peuple, s'ils jurent par mon nom, et disent: L'Éternel est vivant! comme ils ont enseigné à mon peuple à jurer par Baal, ils seront établis au milieu de mon peuple.
17 Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.
Mais s'ils n'écoutent pas, j'arracherai entièrement une telle nation, et je la ferai périr, dit l'Éternel.