< Yeremiya 12 >

1 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
Thou indeed, O Lord, art just, if I plead with thee, but yet I will speak what is just to thee: Why doth the way of the wicked prosper: why is it well with all them that transgress, and do wickedly?
2 Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
Thou hast planted them, and they have taken root: they prosper and bring forth fruit: thou art near in their mouth, and far from their reins.
3 Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
And thou, O Lord, hast known me, thou hast seen me, and proved my heart with thee: gather them together as sheep for a sacrifice, and prepare them for the day of slaughter.
4 Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
How long shall the land mourn, and the herb of every field wither for the wickedness of them that dwell therein? The beasts and the birds are consumed: because they have said: He shall not see our last end.
5 Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
If thou hast wearied with running with footmen, how canst thou contend with horses? and if thou hast been secure in a land of peace, what wilt thou do in the swelling of the Jordan?
6 Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
For even thy brethren, and the house of thy father, even they have fought against thee, and have cried after thee with full voice: believe them not when they speak good things to thee.
7 “Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
I have forsaken my house, I have left my inheritance: I have given my dear soul into the land of her enemies.
8 Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
My inheritance is become to me as a lion in the wood: is hath cried out against me, therefore have I hated it.
9 Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
Is my inheritance to me as a speckled bird? Is it as a bird died throughout? come ye, assemble yourselves, all the beasts of the earth, make haste to devour.
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
Many pastors have destroyed my vineyard, they have trodden my portion under foot: they have changed my delightful portion into a desolate wilderness.
11 Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
They have laid it waste, and it hath mourned for me. With desolation is all the land made desolate; because there is none that considereth in the heart.
12 Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
The spoilers are come upon all the ways of the wilderness, for the sword of the Lord shall devour from one end of the land to the other end thereof: there is no peace for all flesh.
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
They have sown wheat, and reaped thorns: they have received an inheritance, and it shall not profit them: you shall be ashamed of your fruits, because of the fierce wrath of the Lord.
14 “Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
Thus saith the Lord against all my wicked neighbors, that touch the inheritance that I have shared out to my people Israel: Behold I will pluck them out of their land, and I will pluck the house of Juda out of the midst of them.
15 Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
And when I shall have plucked them out, I will return, and have mercy on them: and I will bring them back, every man to his inheritance, and every man to his land.
16 Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
And it shall come to pass, if they will be taught, and will learn the ways of my people, to swear by my name: The Lord liveth, as they have taught my people to swear by baal: that they shall be built up in the midst of my people.
17 Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.
But if they will not hear, I will utterly pluck out and destroy that nation, saith the Lord.

< Yeremiya 12 >