< Yeremiya 12 >
1 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
Праведен си, Господи, когато се съдя с Тебе; Но пак не разисквам с Тебе за съдбите Ти, - Защо успява пътят на нечестивите? Защо са охолни всички, които постъпват коварно?
2 Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
Насадил си ги и те даже се закорениха; Растат, даже и принасят плод; Ти си близо в устата им, А далеч от сърцата им.
3 Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
Но ти, Господи, ме познаваш; Виждаш ме, и изпитваш какво е сърцето ми спрямо Тебе; Отдели ги като овце за клане, И приготви ги за деня, когато ще бъдат заклани.
4 Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
До кога ще жалее страната, И ще съхне тревата на цялата земя? Загинаха животните и птиците Поради нечестието на жителите й, Защото рекоха: Той няма да види сетнината ни.
5 Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
Ако тичаш с пешаците, и те те изморят, Тогава как ще се надваряш с конете? И макар че в мирна страна си в безопасност, Но какво би направил в прииждането на Иордан?
6 Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
Защото братята ти и бащиният ти дом, - Даже и те се обходиха коварно към тебе, Да! и те извикаха подир тебе велегласно; Но не ги вярвай, даже ако ти говорят добро.
7 “Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
Напуснах дома Си, отхвърлих наследството Си, Предадох възлюблената на душата Ми в ръката на неприятелите й.
8 Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
Наследството Ми стана за Мене като лъв в гората; То издаде гласа си против Мене; Затова го намразих.
9 Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
Наследството Ми е за Мене като пъстра хищна птица; Хищните птици от всяка страна са против него. Идете, съберете всичките полски зверове, Докарайте ги да го изпоядат.
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
Много овчари развалиха лозето Ми, Потъпкаха Моя дял, Обърнаха любимия Ми дял в непроходима пустиня.
11 Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
Обърнаха го в пустота; Той, като запустен, жалее пред Мене; Цялата страна е опустошена, Защото няма кой да вземе това присърце.
12 Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
По всичките голи височини на пустинята дойдоха разорители; Защото ножът Господен пояжда От единия край на страната до другия; Никоя твар няма мир.
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
Сеяха жито, но са пожънали тръни; Трудиха се, но никак не се ползуват; Посрамете се, прочее, от тия си произведения Поради пламенния гняв на Господа.
14 “Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
Така говори Господ Против всичките ми зли съседи, Които посягат на наследството, което дадох на людете Си Израиля, като казва: Ето, ще ги изтръгна от земята им, И ще изтръгна Юдовия дом отсред тях;
15 Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
И след като ги изтръгна, Пак ще им покажа милост, И ще ги върна, всеки човек в наследството му, И всеки човек в земята му.
16 Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
И ако научат добре обходата на Моите люде, Да се кълнат в Моето име, казвайки - заклевам се в живота на Господа! (Както те научиха моите люде да се кълнат във Ваала), Тогава и те ще бъдат утвърдени всред людете Ми.
17 Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.
Но ако не послушат, Съвсем ще изтръгна и ще изтребя оня народ, Казва Господ.