< Yeremiya 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Слово еже бысть от Господа ко Иеремии, глаголющее:
2 “Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
слышите словеса завета сего и глаголите ко мужем Иудиным и ко обитателем Иерусалимским,
3 Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
и речеши к ним: сия глаголет Господь Бог Израилев: проклят муж, иже не послушает словес завета сего,
4 Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
егоже заповедах отцем вашым в день, в оньже изведох их от земли Египетския, от пещи железныя, глаголя: услышите глас Мой и сотворите вся, елика заповедаю вам, и будете Мне в люди, и Аз буду вам в Бога:
5 Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
да утвержду клятву Мою, еюже кляхся отцем вашым, еже дати им землю точащую млеко и мед, якоже есть день сей. И отвещах и рекох: буди, Господи.
6 Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
И рече Господь ко мне: прочти вся словеса сия во градех Иудиных и вне Иерусалима, рекий: слышите словеса завета сего и сотворите та:
7 Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
яко свидетелствуя засвидетелствовах отцем вашым в день, в оньже изведох их от земли Египетския, даже до дне сего, заутра востая засвидетелствовах глаголя: слышите глас Мой.
8 Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
И не слышаша, ни приклониша уха своего, но идоша кийждо в стропотстве сердца своего злаго: и наведох на них вся словеса завета сего, егоже заповедах да сотворят, и не сотвориша.
9 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
И рече Господь ко мне: обретено есть совещание (на зло) в мужех Иудиных и во обитающих во Иерусалиме:
10 Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
возвратишася ко беззаконием первым отец своих, иже не хотеша слышати словес Моих, и се, тии поидоша по бозех чуждих, да служат им: и разори дом Израилев и дом Иудин завет Мой, егоже завещах со отцы их.
11 Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
Сего ради сия глаголет Господь: се, Аз наведу на них злая, от нихже изыти не возмогут, и возопиют ко Мне, и не услышу их:
12 Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
и пойдут грады Иудины и обитателе Иерусалима и возопиют ко богом, имже тии кадят, иже не спасут их во время скорбей их.
13 Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
По числу бо градов твоих беху бози твои, Иудо, и по числу путий Иерусалимских постависте олтари студныя, олтари на каждение Ваалу.
14 “Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
Ты же не молися о людех сих и не проси о них в мольбе и молитве: не услышу бо во время вопля их ко Мне и во время озлобления их.
15 “Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
Почто возлюбленная в дому Моем сотвори мерзости (многи)? Еда обеты и мяса святая отимут от тебе лукавства твоя, или сими избежиши?
16 Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
Маслину благосенну, красну зраком нарече Господь имя твое, ко гласу обрезания ея: разгореся огнь в ней, велика скорбь на тебе, непотребны быша ветви ея.
17 Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
И Господь Сил, иже насади тебе, глаголал есть на тя зло за злая дому Израилева и дому Иудина, елика сотвориша себе ко прогневанию Мене кадяще Ваалу.
18 Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
Господи, скажи ми, и уразумею: тогда видех начинания их.
19 Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
Аз же, яко агня незлобиво ведомо на заколение, не разумех, яко на мя помыслиша помысл лукавый, глаголюще: приидите и вложим древо во хлеб его и истребим его от земли живущих, и имя его да не помянется ктому.
20 Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
Господь Саваоф, судяй праведно, испытуяй сердца и утробы, да вижду мщение Твое на них, яко к Тебе открых оправдание мое.
21 “Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
Сего ради сия глаголет Господь на мужы Анафофски ищущыя души моея, глаголющыя: да не пророчествуеши о имени Господни, аще ли же ни, умреши в руках наших.
22 koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
Сего ради сия глаголет Господь Сил: се, Аз посещу на них: юноши их мечем умрут, и сынове их и дщери их скончаются гладом,
23 Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”
и останка не будет от них, наведу бо злая на живущыя во Анафофе в лето посещения их.

< Yeremiya 11 >