< Yeremiya 11 >
1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini, lisithi:
2 “Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
Zwanini amazwi alesisivumelwano, likhulume ebantwini bakoJuda lakubahlali beJerusalema.
3 Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
Njalo uthi kibo: Itsho njalo INkosi uNkulunkulu kaIsrayeli: Uqalekisiwe umuntu ongalaleli amazwi alesisivumelwano,
4 Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
engawalayela oyihlo ngosuku engibakhupha ngalo elizweni leGibhithe, esithandweni sensimbi, ngisithi: Lalelani ilizwi lami, liwenze njengakho konke engililaya khona; ngalokho lizakuba ngabantu bami, lami ngibe nguNkulunkulu wenu,
5 Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
ukuze ngimise isifungo engasifunga kuboyihlo ukuthi ngibanike ilizwe eligeleza uchago loluju, njengalamuhla. Ngasengiphendula ngathi: Ameni, Nkosi.
6 Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
INkosi yasisithi kimi: Memezela wonke lamazwi emizini yakoJuda lezitaladeni zeJerusalema, usithi: Zwanini amazwi alesisivumelwano, liwenze.
7 Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
Ngoba ngafakaza lokufakaza kuboyihlo ngosuku engabakhuphula ngalo elizweni leGibhithe, kuze kube lamuhla, ngivuka ngovivi ngifakaza, ngisithi: Lalelani ilizwi lami.
8 Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
Kodwa kabalalelanga, kababekanga indlebe yabo, kodwa bahamba, ngulowo lalowo ngobulukhuni benhliziyo yabo embi. Ngakho ngizaletha phezu kwabo wonke amazwi alesisivumelwano, engabalaya ukuthi bawenze, kodwa kabawenzanga.
9 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
INkosi yasisithi kimi: Kutholakele ugobe phakathi kwabantu bakoJuda, laphakathi kwabahlali beJerusalema.
10 Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
Sebebuyele eziphambekweni zabokhokho babo, abala ukuzwa ilizwi lami; bona balandela abanye onkulunkulu ukuze babakhonze; indlu yakoIsrayeli lendlu yakoJuda zisephulile isivumelwano sami engasenza laboyise.
11 Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
Ngakho itsho njalo iNkosi: Khangela, ngizaletha okubi phezu kwabo, abangeke baphume kukho; lapho bekhala kimi, kangiyikubezwa.
12 Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
Khona imizi yakoJuda labahlali beJerusalema bezahamba bakhale kubonkulunkulu ababatshisela impepha, kodwa kabayikubasindisa lokubasindisa ngesikhathi sobubi babo.
13 Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
Ngoba njengenani lemizi yakho babenjalo onkulunkulu bakho, Juda, lanjengenani lezitalada zeJerusalema limisile amalathi kulokhu okuyangisayo, amalathi okutshisela uBhali impepha.
14 “Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
Ngakho wena ungabakhulekeli lababantu, futhi ungabaphakamiseli ukukhala kumbe umkhuleko, ngoba kangiyikuzwa ngesikhathi sokukhala kwabo kimi ngenxa yenhlupheko yabo.
15 “Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
Othandekayo wami ulani endlini yami, lokhu enze amanyala labanengi, lenyama engcwele isiyedlule kuwe yini? Lapho usenza okubi, kulapho uthokoza.
16 Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
INkosi yabiza ibizo lakho ngokuthi: Isihlahla somhlwathi esiluhlaza esihle ngezithelo ezinhle; ngomsindo wenhlokomo enkulu izasithungela ngomlilo, lengatsha zaso zephuke.
17 Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
Ngoba iNkosi yamabandla, eyakuhlanyelayo, ikhulumile okubi ngawe, ngenxa yobubi bendlu yakoIsrayeli lobendlu yakoJuda, abakwenzileyo bemelene labo ngokwabo ukungicunula ngokutshisela uBhali impepha.
18 Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
INkosi yasingazisa ukuthi ngazi; wasungitshengisa izenzo zabo.
19 Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
Kodwa mina nganginjengewundlu kumbe inkabi kusiwa ekuhlatshweni; ngoba ngangingazi ukuthi baceba amacebo bemelene lami, besithi: Asichithe isihlahla lesithelo saso; asimqume asuke elizweni labaphilayo, ukuze ibizo lakhe lingabe lisakhunjulwa.
20 Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
Kodwa, wena Nkosi yamabandla, umahluleli olungileyo, ohlola izinso lenhliziyo, kangibone impindiselo yakho kibo; ngoba ngembule udaba lwami kuwe.
21 “Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
Ngakho itsho njalo iNkosi ngamadoda eAnathothi, adinga impilo yakho, esithi: Ungaprofethi ngebizo leNkosi, ukuze ungafi ngesandla sethu.
22 koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
Ngakho itsho njalo INkosi yamabandla: Khangela, ngizawajezisa; amajaha azakufa ngenkemba, amadodana awo lamadodakazi awo azakufa ngendlala,
23 Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”
njalo kakuyikuba lensali kuwo; ngoba ngizaletha okubi phezu kwamadoda eAnathothi, ngomnyaka wempindiselo yawo.