< Yeremiya 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
La parole adressée à Jérémie par l’Eternel était ainsi conçue:
2 “Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
"Ecoutez les termes de cette alliance, et vous les redirez aux gens de Juda et aux habitants de Jérusalem.
3 Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
Tu leur diras: Ainsi parle l’Eternel, Dieu d’Israël: Maudit soit l’homme qui n’écoutera pas les termes de cette alliance,
4 Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
que j’ai dictée à vos ancêtres à l’époque où je les ai fait sortir du pays d’Egypte, de ce creuset de fer, en disant: Ecoutez ma voix, conformez-vous à tous les ordres que je vous prescris, alors vous serez mon peuple et je serai votre Dieu;
5 Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
de manière à accomplir le serment que j’ai fait à vos ancêtres de leur donner un pays où coulent le lait et le miel, comme cela s’est réalisé aujourd’hui!" Je répondis par ces mots: "Amen, ô Eternel!"
6 Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
Et l’Eternel me dit: "Publie toutes ces paroles dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem, savoir: Ecoutez les termes de cette alliance, et mettez-les à exécution;
7 Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
car j’ai dûment averti vos ancêtres dès le jour où je les ai fait monter du pays d’Egypte jusqu’à ce jour, je les ai avertis chaque matin en disant: Ecoutez ma voix!
8 Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
Mais ils n’ont pas écouté, ils n’ont pas prêté l’oreille, ils ont suivi chacun les penchants de leur coeur pervers; aussi leur ai-je appliqué toutes les clauses du contrat que je leur avais ordonné de respecter et qu’ils n’ont pas respectées."
9 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
Et l’Eternel me dit: "Il s’est formé un complot parmi les gens de Juda et les habitants de Jérusalem.
10 Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
Ils sont retournés aux fautes de leurs premiers aïeux, qui avaient refusé d’obéir à mes paroles; eux aussi s’attachent à des dieux étrangers pour les servir: la maison d’Israël et la maison de Juda ont rompu l’alliance que j’avais contractée avec leurs ancêtres."
11 Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
C’Est pourquoi ainsi parle l’Eternel: "Voici, je fais fondre sur eux des calamités dont ils ne pourront s’échapper; alors ils crieront vers moi et je ne les écouterai point.
12 Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
Les villes de Juda et les habitants de Jérusalem pourront aller implorer les dieux auxquels ils brûlent de l’encens; mais ceux-ci seront impuissants à les secourir au temps de leur malheur.
13 Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
Car aussi nombreux que tes villes sont tes dieux, ô Juda; aussi nombreux que les rues de Jérusalem sont les autels élevés par vous à un culte honteux, les autels pour encenser Baal!
14 “Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
Quant à toi, ne prie pas en faveur de ce peuple; ne m’invoque ni ne me supplie pour lui, car je n’écouterai pas à l’heure où ils s’adresseront à moi à cause de leurs maux.
15 “Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
Que vient faire mon bien-aimé dans ma maison? Il commet des indignités en nombre! A quoi bon cette chair consacrée qui provient de tes mains? Quand tu fais le mal, alors tu triomphes!
16 Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
Dieu t’avait dénommé "olivier verdoyant, remarquable par la beauté de son fruit", mais, au bruit d’un terrible fracas, il y a mis le feu et ses rameaux ont volé en éclats.
17 Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
L’Eternel-Cebaot qui t’avait planté a décrété ta ruine, causée par le mal que se sont fait à elles-mêmes la maison d’Israël et la maison de Juda en m’irritant, en encensant Baal.
18 Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
L’Eternel m’a instruit; je sais, depuis que tu m’as rendu témoin de leurs oeuvres,
19 Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
que j’étais, moi, semblable à une brebis docile qu’on mène à l’abattoir; ce que je ne savais pas, c’est que c’était contre moi qu’ils formaient de mauvais desseins: "Allons, détruisons l’arbre dans sa sève, extirpons-le de la terre des vivants, et que son nom ne soit plus mentionné!"
20 Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
Mais l’Eternel-Cebaot est un Juge intègre, sondant les reins et le coeur: je verrai la vengeance que tu tireras d’eux, car c’est à toi que je confie ma cause.
21 “Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
C’Est pourquoi ainsi parle l’Eternel-Cebaot au sujet des gens d’Anatot qui en veulent à ta vie et te disent: "Ne prophétise plus au nom de l’Eternel, si tu ne veux pas mourir de notre main!"
22 koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
Oui, ainsi parle l’Eternel-Cebaot: "Je vais sévir contre eux: les jeunes gens périront par le glaive, leurs fils et leurs filles périront par la famine.
23 Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”
Il ne leur demeurera aucun reste, quand je ferai arriver la catastrophe sur les gens d’Anatot, l’année de leur châtiment."

< Yeremiya 11 >