< Yeremiya 11 >
1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
[the] word which to be to(wards) Jeremiah from with LORD to/for to say
2 “Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
to hear: hear [obj] word [the] covenant [the] this and to speak: speak them to(wards) man: anyone Judah and upon to dwell Jerusalem
3 Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
and to say to(wards) them thus to say LORD God Israel to curse [the] man which not to hear: hear [obj] word [the] covenant [the] this
4 Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
which to command [obj] father your in/on/with day to come out: send I [obj] them from land: country/planet Egypt from furnace [the] iron to/for to say to hear: hear in/on/with voice my and to make: do [obj] them like/as all which to command [obj] you and to be to/for me to/for people and I to be to/for you to/for God
5 Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
because to arise: establish [obj] [the] oath which to swear to/for father your to/for to give: give to/for them land: country/planet to flow: flowing milk and honey like/as day: today [the] this and to answer and to say amen LORD
6 Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
and to say LORD to(wards) me to call: call out [obj] all [the] word [the] these in/on/with city Judah and in/on/with outside Jerusalem to/for to say to hear: hear [obj] word [the] covenant [the] this and to make: do [obj] them
7 Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
for to testify to testify in/on/with father your in/on/with day to ascend: establish I [obj] them from land: country/planet Egypt and till [the] day: today [the] this to rise and to testify to/for to say to hear: obey in/on/with voice my
8 Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
and not to hear: obey and not to stretch [obj] ear their and to go: walk man: anyone in/on/with stubbornness heart their [the] bad: evil and to come (in): bring upon them [obj] all word [the] covenant [the] this which to command to/for to make: do and not to make: do
9 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
and to say LORD to(wards) me to find conspiracy in/on/with man: anyone Judah and in/on/with to dwell Jerusalem
10 Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
to return: turn back upon iniquity: crime father their [the] first which to refuse to/for to hear: hear [obj] word my and they(masc.) to go: follow after God another to/for to serve: minister them to break house: household Israel and house: household Judah [obj] covenant my which to cut: make(covenant) with father their
11 Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
to/for so thus to say LORD look! I to come (in): bring to(wards) them distress: harm which not be able to/for to come out: come from her and to cry out to(wards) me and not to hear: hear to(wards) them
12 Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
and to go: went city Judah and to dwell Jerusalem and to cry out to(wards) [the] God which they(masc.) to offer: offer to/for them and to save not to save to/for them in/on/with time distress: harm their
13 Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
for number city your to be God your Judah and number outside Jerusalem to set: make altar to/for shame altar to/for to offer: offer to/for Baal
14 “Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
and you(m. s.) not to pray about/through/for [the] people [the] this and not to lift: loud about/through/for them cry and prayer for nothing I to hear: hear in/on/with time to call: call to they to(wards) me about/through/for distress: harm their
15 “Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
what? to/for beloved my in/on/with house: temple my to make: do she [the] plot [to] [the] many and flesh holiness to pass from upon you for distress: harm your then to exult
16 Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
olive luxuriant beautiful fruit appearance to call: call by LORD name your to/for voice: sound tumult great: large to kindle fire upon her and to shatter branch his
17 Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
and LORD Hosts [the] to plant [obj] you to speak: promise upon you distress: harm in/on/with because of distress: evil house: household Israel and house: household Judah which to make: do to/for them to/for to provoke me to/for to offer: offer to/for Baal
18 Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
and LORD to know me and to know [emph?] then to see: see me deed their
19 Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
and I like/as lamb tame to conduct to/for to slaughter and not to know for upon me to devise: devise plot to ruin tree in/on/with food his and to cut: eliminate him from land: country/planet alive and name his not to remember still
20 Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
and LORD Hosts to judge righteousness to test kidney and heart to see: see vengeance your from them for to(wards) you to reveal: reveal [obj] strife my
21 “Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
to/for so thus to say LORD upon human Anathoth [the] to seek [obj] soul: life your to/for to say not to prophesy in/on/with name LORD and not to die in/on/with hand our
22 koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
to/for so thus to say LORD Hosts look! I to reckon: punish upon them [the] youth to die in/on/with sword son: child their and daughter their to die in/on/with famine
23 Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”
and remnant not to be to/for them for to come (in): bring distress: harm to(wards) human Anathoth year punishment their