< Yeremiya 10 >
1 Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
Hør det ord Herren har talt til eder, Israels hus!
2 Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
Så sier Herren: Venn eder ikke til hedningenes vei, og reddes ikke for himmelens tegn, fordi hedningene reddes for dem!
3 Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
For folkenes skikker er tomhet. De feller et tre i skogen, og treskjæreren lager det til med øksen;
4 Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
med sølv og gull pryder de det; med spiker og hammer fester de det, så det ikke skal falle.
5 Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
Som en dreiet søile er de ting som blir laget, og de kan ikke tale; bæres må de; for de kan ikke gå! Frykt ikke for dem! For de kan ikke gjøre ondt, og å gjøre godt står heller ikke i deres makt.
6 Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
Det er ingen som du, Herre! Stor er du, og stort er ditt navn ved ditt velde.
7 Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
Hvem skulde ikke frykte dig, du folkenes konge! Dig tilkommer det; for blandt alle folkenes vismenn og i alle deres riker er det ingen som du.
8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
Men alle sammen er de ufornuftige, de er dårer. En tom lære! Tre er det,
9 Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
uthamret sølv innført fra Tarsis og gull fra Ufas, et verk av treskjærerens og av gullsmedens hender; blått og rødt purpur er deres klædning, et verk av kunstforstandige menn er de alle sammen.
10 Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
Men Herren er Gud i sannhet, han er en levende Gud og en evig konge; for hans vrede bever jorden, og hedningefolkene kan ikke utholde hans harme.
11 “Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
Således skal I si til dem: De guder som ikke har gjort himmelen og jorden, de skal bli borte fra jorden og ikke finnes under himmelen.
12 Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
Han er den som skapte jorden ved sin kraft, som grunnfestet jorderike ved sin visdom og spente ut himmelen ved sin forstand.
13 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
Ved sin torden lar han vannene i himmelen bruse, han lar dunster stige op fra jordens ende, sender lyn med regn og fører vind ut av sine forrådskammer.
14 Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Hvert menneske blir ufornuftig, uten forstand, hver gullsmed har skam av det utskårne billede; for hans støpte billeder er løgn, og det er ingen ånd i dem.
15 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
De er tomhet, et verk som vekker spott; på sin hjemsøkelses tid skal de gå til grunne.
16 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Ikke er han som er Jakobs del, lik dem; for han er den som har skapt alle ting, og Israel er den ætt som er hans arv; Herren, hærskarenes Gud, er hans navn.
17 Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
Sank ditt gods sammen fra landet, du som bor i kringsatte byer!
18 Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
For så sier Herren: Se, jeg vil slynge landets innbyggere bort denne gang, og jeg vil trenge dem så de skal kjenne det.
19 Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
Ve mig for et slag jeg har fått! Mitt sår er ulægelig! Men jeg sier: Ja, dette er en plage, og jeg må bære den.
20 Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
Mitt telt er ødelagt, og alle mine snorer er slitt av; mine barn har gått bort fra mig og er ikke mere; det er ingen som slår op mitt telt mere eller henger op mine tepper.
21 Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
For hyrdene var uforstandige og søkte ikke Herren; derfor fór de ikke vist frem, og hele deres hjord blev adspredt.
22 Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
Det lyder et budskap! Se, det kommer, og stort bulder fra landet i nord, og Judas byer skal gjøres til en ørken, til en bolig for sjakaler.
23 Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
Jeg vet, Herre, at et menneske ikke selv råder for sin vei, at det ikke står til vandringsmannen å styre sin gang.
24 Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
Tukt mig, Herre, men med måte, ikke i din vrede, forat du ikke skal gjøre mig liten og arm!
25 Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.
Utøs din harme over hedningene, som ikke kjenner dig, og over de ætter som ikke påkaller ditt navn! For de har fortært Jakob, fortært ham og gjort ende på ham, og hans bolig har de lagt øde.