< Yeremiya 10 >
1 Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
Écoutez la parole que vous dit l'Éternel, à vous, maison d'Israël!
2 Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
Ainsi parle l'Éternel: Ne pratiquez point la voie des nations, et des signes du ciel ne vous épouvantez pas, parce que les nations s'en épouvantent.
3 Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
Car le culte des nations est une vanité. C'est du bois coupé dans la forêt, travaillé par la main du sculpteur avec la hache;
4 Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
il le pare d'argent et d'or, le fixe avec des clous et des marteaux, pour qu'il ne vacille pas.
5 Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
Comme le palmier ils sont arrondis, mais ils ne parlent pas; on les porte; car ils ne marchent pas. N'ayez point peur d'eux, car ils ne sauraient nuire, et faire du bien n'est pas en leur puissance.
6 Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
Nul n'est ton égal, Éternel; tu es grand, et ton nom est grand en puissance.
7 Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
Qui ne te craindrait, Roi des nations? car cela t'appartient; car entre tous les sages des peuples, et dans tous leurs empires personne n'est ton égal.
8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
Et tous ensemble ils sont stupides et insensés: vaine doctrine! c'est du bois!
9 Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
L'argent battu est amené de Tarsis, et l'on apporte d'Uphaz l'or que travaillent le sculpteur et la main de l'orfèvre; la pourpre rouge et la pourpre bleue les habillent; ils sont tous un travail de l'ouvrier.
10 Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
Mais l'Éternel est un Dieu qui est vérité; Il est un Dieu vivant, et un Roi éternel; à sa colère la terre tremble, et les nations ne soutiennent point son courroux.
11 “Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
Vous leur parlerez en ces termes: Les dieux qui n'ont point fait le ciel et la terre, seront exterminés de la terre et de dessous les Cieux.
12 Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
Il a fait la terre par sa puissance, fondé le monde par sa sagesse, et déployé les Cieux par son intelligence.
13 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
Au son de sa voix les eaux s'amassent dans les Cieux, et Il attire les vapeurs des bouts de la terre, Il envoie les éclairs avant la pluie, et fait sortir les vents de ses magasins.
14 Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Tout homme est stupide faute de le connaître; pour chaque fondeur ses idoles sont un sujet de honte, car l'image fondue par lui est un mensonge, et elle ne respire pas.
15 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
C'est une vanité, une œuvre de la tromperie; au jour de leur châtiment elles seront détruites.
16 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Il ne leur ressemble pas Celui qui est la part de Jacob, car Il a tout formé, et Israël est sa tribu d'héritage, L'Éternel des armées est son nom.
17 Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
Enlève du pays tes bagages, ô toi qui es en état de siège!
18 Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
Car ainsi parle l'Éternel: Voici, cette fois je vais lancer avec la fronde les habitants du pays, et je les y serrerai, afin qu'ils atteignent.
19 Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
« Malheureuse! je suis brisée! ma plaie est douloureuse! Toutefois je dis: Oui, ce que j'ai à souffrir, je le subirai!
20 Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
Ma tente est détruite, et tous mes cordages sont rompus, mes fils m'ont quittée, je ne les ai plus; personne ne tendra plus ma tente, et ne relèvera mes pavillons.
21 Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
Car les pasteurs s'étaient abrutis, et ils n'ont point cherché l'Éternel: c'est pour cela qu'ils n'ont point prospéré, et que tout leur troupeau a été dispersé. »
22 Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
Une rumeur se fait entendre! le voici, il arrive avec un grand fracas de la région du Nord, pour réduire les villes de Juda en un désert, séjour des chacals.
23 Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
« Je sais, Éternel, que l'homme n'est pas maître de sa voie, que l'homme qui marche n'a pas le pouvoir de diriger ses pas.
24 Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
Châtie-moi, Éternel, mais équitablement, et non en ta colère, afin de ne pas m'anéantir.
25 Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.
Verse ta fureur sur les nations qui ne te connaissent pas, et sur les tribus qui n'invoquent point ton nom; car elles ont dévoré Jacob, elles l'ont dévoré et exterminé, et elles ont ravagé son séjour. »