< Yeremiya 10 >

1 Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
Ecoutez la parole que Yahweh vous adresse, maison d’Israël:
2 Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
Ainsi parle Yahweh: N’apprenez pas la voie des nations, et ne soyez pas effrayés par les signes du ciel, comme les nations s’en effraient;
3 Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
Car les coutumes des nations ne sont que vanité; c’est du bois qu’on coupe dans la forêt, un ouvrage de la main du sculpteur, façonné avec le ciseau,
4 Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
que l’on décore avec l’argent et l’or. On le fixe avec des clous à coups de marteau, pour qu’il ne bouge pas.
5 Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
Ces dieux-là sont comme une colonne faite au tour; car on les porte, ils ne marchent pas. Ne les craignez point: ils ne font pas de mal; ils ne peuvent pas davantage faire du bien.
6 Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
Nul n’est semblable à vous, Yahweh; vous êtes grand, et votre nom est grand en puissance.
7 Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
Qui ne vous craindrait, Roi des nations! c’est à vous que la crainte est due. Car, parmi tous les sages des nations et dans tous leurs royaumes, nul n’est pareil à vous.
8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
Tous ensemble ils sont stupides et fous; enseignement de vanité; c’est du bois!
9 Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
Argent battu amené de Tharsis, et or d’Ophaz; œuvre de sculpture et de main d’orfèvre! On les revêt de pourpre violette et rouge; tous ne sont qu’ouvrage d’artistes.
10 Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
Mais Yahweh est Dieu en vérité; lui, il est un Dieu vivant et un Roi éternel; à sa colère la terre tremble, et les nations ne soutiennent pas son courroux.
11 “Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
Voici comment vous leur parlerez: « Les dieux qui n’ont pas fait le ciel et la terre seront exterminés de la terre et de dessous le ciel. »
12 Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
Il a fait la terre par sa force, affermi le monde par sa sagesse, et par son intelligence il a étendu les cieux.
13 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
A sa voix, les eaux s’amassent dans les cieux; il fait monter les nuages des extrémités de la terre; il fait briller les éclairs d’où jaillit l’averse, et fait sortir le vent de ses réservoirs.
14 Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Tout homme est stupide, hors de sens; tout artisan a honte de son idole, car son image fondue n’est que mensonge; il n’y a pas de souffle en elle.
15 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
Elle est une vanité, une œuvre de tromperie; au jour de leur châtiment, elle périra.
16 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Telle n’est pas la part de Jacob; car Lui, il a formé l’univers, et Israël est la tribu de son héritage; son nom est Yahweh des armées.
17 Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
Ramasse à terre ton bagage, toi qui es assiégée!
18 Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
Car ainsi parle Yahweh: Voici que cette fois, je vais lancer au loin les habitants du pays; je les serrerai de près, afin que l’ennemi les atteigne.
19 Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
Malheur à moi à cause de ma meurtrissure! Ma plaie est douloureuse; mais je le dis: « Oui, c’est là mon mal, et je le supporterai.
20 Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
Ma tente est dévastée, tous mes cordages sont rompus; mes fils m’ont quittée, ils ne sont plus; je n’ai plus personne pour redresser ma tente, relever mes pavillons. »
21 Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
Ah! les pasteurs sont stupides; ils n’ont pas cherché Yahweh; aussi n’ont-ils pas prospéré, et tout leur troupeau a été dispersé.
22 Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
Un bruit, une rumeur! Voici qu’elle vient, un grand tumulte arrive du pays du septentrion, pour faire des villes de Juda un désert, un repaire de chacals.
23 Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
Je le sais, ô Yahweh, ce n’est pas à l’homme qu’appartient sa voie, ce n’est pas à l’homme qui marche de diriger ses pas.
24 Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
Châtiez-moi, Yahweh, mais selon la justice, et non dans votre colère, pour me réduire à néant.
25 Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.
Versez votre fureur sur les nations qui ne vous connaissent pas, sur les peuples qui n’invoquent pas votre nom; car ils ont dévoré Jacob, ils l’ont dévoré, ils l’achèvent, et ils dévastent sa demeure.

< Yeremiya 10 >