< Yeremiya 10 >

1 Inu Aisraeli, imvani zimene Yehova akunena.
Listen to the word that the Lord has spoken concerning you, O house of Israel.
2 Yehova akuti, “Musatsatire makhalidwe a anthu a mitundu ina kapena kuchita mantha ndi zizindikiro zamlengalenga, ngakhale anthu a mitundu ina amachita nazo mantha.
Thus says the Lord: “Do not choose to learn according to the ways of the Gentiles. And do not be willing to dread the signs of heaven, which the Gentiles fear.
3 Pakuti miyambo ya mitundu inayo ndiyachabechabe. Iwo amakadula mtengo ku nkhalango ndipo mmisiri amawusema ndi sompho.
For the laws of the people are empty. For the work of the hand of the craftsman has cut a tree from the forest with an axe.
4 Amakongoletsa chosemacho ndi siliva ndi golide; kenaka amachikhomerera ndi misomali kuti chisagwedezeke.
He has adorned it with silver and gold. He has put it together with nail and hammer, so that it will not fall apart.
5 Mafano awo ali ngati mtengo wakanjedza woopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka. Mafanowo sangathe nʼkuyankhula komwe ndipo ayenera kunyamulidwa popeza sangathe nʼkuyenda komwe. Musachite nawo mantha popeza sangathe kukuchitani choyipa ndiponso alibe mphamvu yochitira chabwino chilichonse.”
They have been fabricated in the likeness of a palm tree, and they will not speak. They must be carried to be moved, because they do not have the ability to walk. Therefore, do not be willing to fear them, for they can do neither evil nor good.”
6 Palibe wofanana nanu, Inu Yehova; Inu ndinu wamkulu, ndipo dzina lanu lili ndi mphamvu yayikulu.
O Lord, there is nothing similar to you. You are great, and your name is great in strength.
7 Ndani amene angaleke kukuopani, inu Mfumu ya mitundu ya anthu? Chimenechi ndicho chokuyenerani. Pakati pa anthu anzeru onse komanso mafumu onse a mitundu ya anthu, palibe wina wofanana nanu.
Who will not fear you, O King of the nations? For honor is yours. Among all the wise of the nations, and within all their kingdoms, there is nothing similar to you.
8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.
Together, they will all be proven to be unwise and foolish. The doctrine of their vanity is made of wood.
9 Siliva wosula amabwera naye kuchokera ku Tarisisi ndipo golide amachokera naye ku Ufazi. Mafanowo ndi ntchito ya anthu aluso ndi odziwa kuzokota golide. Tsono mafanowo amawaveka zovala za mtundu wamtambo ndi pepo. Yonseyo ndi ntchito ya anthu a luso.
Rolled silver is brought from Tarshish, and gold from Uphaz. It is the work of a craftsman, and of the hand of a coppersmith. Hyacinth and purple is their clothing. All these things are the work of artists.
10 Koma Yehova ndiye Mulungu woona; Iyeyo ndiye Mulungu wamoyo, Mfumu yamuyaya. Akakwiya, dziko limagwedezeka; anthu a mitundu ina sangathe kupirira ukali wakewo.
But the Lord is the true God. He is the living God and the everlasting King. Before his indignation, the earth will shake. And the Gentiles will not be able to withstand his threats.
11 “Awuze anthu awa kuti, ‘Milungu iyi, imene sinalenge dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, idzawonongeka pa dziko lapansi ndi pansi pa thambo.’”
“And so, you shall speak to them in this way: The gods that have not made heaven and earth, let them perish from the earth and from among those places which are under heaven.
12 Koma Mulungu analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
He made the earth by his power, he prepared the world in his wisdom, and he stretched out the heavens with his understanding.
13 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba; Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene osungirako.
At his voice, he grants a multitude of waters in the heavens, and he lifts up the clouds from the ends of the earth. He causes the lightning with the rain, and he leads forth the wind from his storehouses.
14 Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Every man has become a fool concerning knowledge; every artist has been confounded by his graven image. For what he has formed is false, and there is no spirit in these things.
15 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa, mafanowo adzawonongedwa.
These things are empty, and they are a work deserving of ridicule. In the time of their visitation, they will perish.
16 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse kuphatikizapo Israeli, mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Jacob’s portion is not like their portion. For his portion is from the One who formed all things. And Israel is the staff of his inheritance. The Lord of hosts is his name.
17 Sonkhanitsani katundu wanu, inu amene mukukhala mʼlinga la ankhondo.
Gather your shame from the earth, you who are living under siege.”
18 Pakuti Yehova akuti, “Tsopano Ine ndidzachotsa anthu onse amene akukhala mʼdziko lino; adzakhala pa mavuto mpaka adzamvetsa.”
For thus says the Lord: “Behold, in this turn, I will cast the inhabitants of the land far away. And I will afflict them no matter where they may be found.”
19 Aliyense ankangoti, “Mayo ine, chifukwa cha kupweteka kwanga! Chilonda changa nʼchachikulu!” Koma ine ndinkaganiza kuti, “Ndithu, ili ndi vuto langa basi, choncho ndingolipirira.”
Woe to me, concerning my destruction! My wound is very grievous. And yet I said: Clearly, this infirmity is mine, and I will carry it.
20 Tenti yanga yawonongeka, zingwe zake zonse zaduka. Ana anga andisiya ndipo kulibenso. Palibenso amene adzandimangire tenti, kapena kufunyulula nsalu yake.
My tent has been destroyed. All my cords have been broken. My sons have gone away from me; they did not remain. There is no one to stretch out my tent any more, nor to set up my curtains.
21 Abusa ndi opusa ndipo sanapemphe nzeru kwa Yehova; choncho palibe chimene anapindula ndipo nkhosa zawo zonse zabalalika.
For the pastors have acted foolishly, and they have not sought the Lord. Because of this, they have not understood, and all their flock has been dispersed.
22 Tamvani! kukubwera mphekesera, phokoso lalikulu la gulu la a ankhondo likumveka kuchokera kumpoto! Lidzasandutsa bwinja mizinda ya ku Yuda, malo okhala nkhandwe.
Behold, the sound of a voice approaches, a great commotion from the land of the north: so that he may make the cities of Judah into a wilderness and into a dwelling place for serpents.
23 Inu Yehova, ndikudziwa kuti moyo umene munthu ali nawo si wake; munthuyo sangathe kuwongolera mayendedwe ake.
I know, O Lord, that the way of man is not his own. Neither is it given to man to walk and to direct his own steps.
24 Inu Yehova, langizeni, komatu mwachilungamo, osati ndi mkwiyo wanu, mungandiwononge kotheratu.
Correct me, O Lord, yet truly, do so with judgment, and not in your fury. Otherwise, you will reduce me to nothing.
25 Tsanulirani ukali wanu pa mitundu ya anthu amene sakudziwani, ndiye kuti mitundu ya anthu amene satama pa dzina lanu mopemba. Iwo aja anasakaza Yakobo; amusakaza kotheratu ndipo awononga dziko lake.
Pour out your indignation upon the nations that have not known you, and upon the provinces that have not invoked your name. For they have fed upon Jacob, and devoured him, and consumed him, and they have utterly destroyed his honor.

< Yeremiya 10 >