< Yeremiya 1 >
1 Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
Слова́ Єремі́ї, сина Хілкійїного, з священиків, що в Анато́ті, у Веніяминовому кра́ї,
2 Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
що було́ до нього Господнє слово за днів Йосії, Амонового сина, Юдиного царя, тринадцятого року його царюва́ння.
3 Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
І було воно й за днів Єгоякима, сина Йосіїного, Юдиного царя, аж до кінця одина́дцятого року Седекії, сина Йосіїного, Юдиного царя, аж до ви́ходу Єрусалиму на вигна́ння в п'ятому місяці.
4 Yehova anayankhula nane kuti,
„І прийшло мені слово Господнє, гово́рячи:
5 “Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
Ще поки тебе вформува́в в утро́бі матерній, Я пізнав був тебе, і ще поки ти вийшов із нутра́, тебе посвятив, дав тебе за пророка наро́дам!
6 Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
А я відповів: О, Господи, Боже, таж я промовля́ти не вмію, бо я ще юна́к!
7 Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
Господь же мені відказав: „Не кажи: „Я юнак“, бо ти пі́деш до всіх, куди тільки пошлю́ Я тебе, і скажеш усе, що тобі накажу́.
8 Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Не лякайсь перед ними, бо Я бу́ду з тобою, щоб тебе рятува́ти, говорить Господь!
9 Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
І простя́г Господь руку Свою, і доторкну́всь моїх уст та й до мене сказав: Ось Я дав в твої у́ста слова Мої!
10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
Дивись, — Я сьогодні призна́чив тебе над наро́дами й царствами, щоб вирива́ти та бу́рити, і щоб губити та руйнувати, щоб будувати й насаджувати!
11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
І було мені слово Господнє, гово́рячи: Що́ ти бачиш, Єреміє? А я відказав: Я бачу мигдале́ву галу́зку.
12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
І сказав мені Господь: Ти добре бачиш, бо Я пильную Свого слова, щоб спра́вдилось воно.
13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
І було мені слово Господнє подруге таке: Що́ ти бачиш? А я відказав: Я бачу кипля́че горня́, а пе́ред його зве́рнений з пі́вночі на південь.
14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
І сказав мені Господь: З пі́вночі відкриється зло на всіх ме́шканців землі.
15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
Бо ось Я покличу всі роди́ни царств на пі́вночі, — говорить Господь, — і вони поприхо́дять, і поставлять кожен свого трона при вході до єрусалимських брам, і навколо при всіх мурах його та при всіх юдиних міста́х.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
І бу́ду суди́тися з ними за всю їхню безбожність, що вони покинули Мене, і кадили іншим бога́м, і вклонялись чина́м своїх рук.
17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
А ти підпе́режеш сте́гна свої та й устанеш, і бу́деш говорити їм усе, що Я накажу́ тобі; не бійся перед ними, щоб Я не злякав тебе перед ними!
18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
Бо Я ось сьогодні поставив тебе містом тверди́нним, і залізним стовпо́м, і мідяними му́рами проти всієї цієї землі, проти царів Юди, проти його князі́в, проти його священиків та проти наро́ду цієї землі.
19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
І будуть вони воювати з тобою, та не переможуть тебе, бо Я із тобою, — говорить Господь, — щоб тебе рятува́ти!“