< Yeremiya 1 >

1 Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
Amazwi kaJeremiya, indodana kaHilikhiya wabapristi ababeseAnathothi elizweni lakoBhenjamini;
2 Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
okwafika kuye ilizwi leNkosi ensukwini zikaJosiya indodana kaAmoni, inkosi yakoJuda, ngomnyaka wetshumi lantathu wokubusa kwakhe.
3 Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
Lafika futhi ensukwini zikaJehoyakhimi indodana kaJosiya, inkosi yakoJuda, kwaze kwaba sekupheleni komnyaka wetshumi lanye kaZedekhiya indodana kaJosiya, inkosi yakoJuda, kwaze kwaba sekuthunjweni kweJerusalema enyangeni yesihlanu.
4 Yehova anayankhula nane kuti,
Kwasekufika kimi ilizwi leNkosi lisithi:
5 “Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
Ngingakakubumbi esiswini ngakwazi, njalo ungakaphumi esizalweni ngakwehlukanisa; ngakubeka waba ngumprofethi ezizweni.
6 Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
Ngasengisithi: Hawu Nkosi Jehova! Khangela, angikwazi ukukhuluma, ngoba ngingumntwana.
7 Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
Kodwa iNkosi yathi kimi: Ungatsho ukuthi: Ngingumntwana; ngoba uzakuya kubo bonke engikuthuma kubo, lakho konke engikulaya khona uzakukhuluma.
8 Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Ungesabi ubuso babo, ngoba mina ngilawe ukukophula, itsho iNkosi.
9 Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
INkosi yasiselula isandla sayo, yathinta umlomo wami; iNkosi yasisithi kimi: Khangela, ngibekile amazwi ami emlonyeni wakho.
10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
Bona, ngikubekile lamuhla phezu kwezizwe laphezu kwemibuso, ukusiphuna, lokudiliza, lokubhubhisa, lokuphosela phansi, ukwakha, lokuhlanyela.
11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi: Ubonani, Jeremiya? Ngasengisithi: Ngibona uswazi lwesihlahla se-alimondi.
12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
INkosi yasisithi kimi: Ubone kuhle, ngoba ngizalinda ilizwi lami ukuze ngilenze.
13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
Njalo ilizwi leNkosi lafika kimi ngokwesibili lisithi: Ubonani? Ngasengisithi: Ngibona imbiza ebilayo, njalo ubuso bayo bungasenyakatho.
14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
INkosi yasisithi kimi: Okubi kuzaqutshulwa kuvela enyakatho phezu kwabo bonke abakhileyo belizwe.
15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
Ngoba khangela, ngibiza insapho zonke zemibuso yenyakatho, itsho iNkosi; njalo zizafika, zimise ngasinye isihlalo salo sobukhosi ekungeneni kwamasango eJerusalema, zimelene lemiduli yayo yonke inhlangothi zonke, zimelene lemizi yonke yakoJuda.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
Ngizakhuluma izigwebo zami zimelene labo ngenxa yabo bonke ububi babo, abangidelileyo, batshisela abanye onkulunkulu impepha, bakhonza imisebenzi yezandla zabo.
17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
Wena-ke, bopha ukhalo lwakho, usukume, ukhulume kibo konke mina engikulaya khona. Ungethuki ngenxa yobuso babo, hlezi ngikwethuse phambi kwabo.
18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
Ngoba khangela, mina ngikubekile lamuhla ube ngumuzi ovikelweyo, njalo ube yinsika yensimbi, njalo ube yimiduli yethusi, ukumelana lelizwe lonke, ukumelana lamakhosi akoJuda, ukumelana leziphathamandla zayo, ukumelana labapristi bayo, lokumelana labantu belizwe.
19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Njalo bazakulwa bemelene lawe; kodwa kabayikukwehlula; ngoba ngilawe, itsho iNkosi, ukukophula.

< Yeremiya 1 >