< Yeremiya 1 >
1 Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
Paroles de Jérémie, fils de Hilkija, d'entre les sacrificateurs qui étaient à Anathoth, dans le pays de Benjamin.
2 Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
La parole de l'Éternel lui fut adressée au temps de Josias, fils d'Amon, roi de Juda, la treizième année de son règne;
3 Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
Et aussi au temps de Jéhojakim, fils de Josias, roi de Juda, jusqu'à la fin de la onzième année de Sédécias, fils de Josias, roi de Juda, jusqu'à ce que Jérusalem fut emmenée en captivité, au cinquième mois.
4 Yehova anayankhula nane kuti,
La parole de l'Éternel me fut adressée, en ces mots:
5 “Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
Avant que je te formasse dans le sein de ta mère, je t'ai connu; avant que tu sortisses de son sein, je t'ai sanctifié; je t'ai établi prophète pour les nations.
6 Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
Et je répondis: Ah! Seigneur Éternel, voici, je ne sais point parler; car je suis un enfant!
7 Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
Et l'Éternel me dit: Ne dis pas: je suis un enfant; car tu iras vers tous ceux à qui je t'enverrai, et tu diras tout ce que je te commanderai.
8 Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Ne les crains point, car je suis avec toi pour te délivrer, dit l'Éternel.
9 Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
Puis l'Éternel étendit sa main et toucha ma bouche. Et l'Éternel me dit: Voici, j'ai mis mes paroles dans ta bouche.
10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
Regarde, je t'ai établi aujourd'hui sur les nations et sur les royaumes, pour que tu arraches et que tu démolisses, pour que tu ruines et que tu détruises, pour que tu bâtisses et que tu plantes.
11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
Et la parole de l'Éternel me fut adressée, disant: Que vois-tu, Jérémie? Et je répondis: Je vois une branche d'amandier.
12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
Et l'Éternel me dit: Tu as bien vu; car je veille sur ma parole pour l'exécuter.
13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
Et la parole de l'Éternel me fut adressée une seconde fois, disant: Que vois-tu? Je répondis: Je vois une chaudière bouillante, du côté du Nord.
14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
Et l'Éternel me dit: C'est du Nord que le mal se déchaînera sur tous les habitants du pays.
15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
Car voici, je vais appeler toutes les tribus des royaumes du Nord, dit l'Éternel; ils viendront et mettront chacun leur trône à l'entrée des portes de Jérusalem, et contre toutes ses murailles à l'entour, et contre toutes les villes de Juda.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
Et je prononcerai mes jugements contre eux, à cause de toute leur méchanceté, parce qu'ils m'ont abandonné et ont offert des parfums à d'autres dieux et se sont prosternés devant l'ouvrage de leurs mains.
17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
Toi donc, ceins tes reins, lève-toi, et dis-leur tout ce que je te commanderai. Ne tremble pas devant eux, de peur que je ne te mette en pièces en leur présence.
18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
Car voici, je t'établis aujourd'hui comme une ville forte, comme une colonne de fer, et comme une muraille d'airain contre tout le pays: contre les rois de Juda, contre ses chefs, contre ses sacrificateurs et contre le peuple du pays.
19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Ils combattront contre toi, mais ne pourront te vaincre; car je suis avec toi, dit l'Éternel, pour te délivrer.