< Yeremiya 1 >

1 Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
Jeremian Hilkian pojan sanat, joka oli Anatotin papeista, Benjaminin maata,
2 Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
Jolle Herran sana tapahtui Josian Amonin pojan, Juudan kuninkaan aikana, kolmantenatoistakymmenentenä hänen valtakuntansa vuonna;
3 Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
Ja sitte Josian pojan, Jojakimin, Juudan kuninkaan aikana, Zedekian Josian pojan, ensimäisen vuoden loppuun toistakymmentä, niin Jerusalemin vankiuteen asti, viidentenä kuukautena.
4 Yehova anayankhula nane kuti,
Ja Herran sana tapahtui minulle ja sanoi:
5 “Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
Minä tunsin sinun jo ennenkuin minä sinun valmistin äitis kohdussa, ja pyhitin sinun ennenkuin sinä äidistäs synnyitkään, ja panin sinun kansain prophetaksi.
6 Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
Mutta minä sanoin: voi Herra, Herra! katso en minä kelpaa saarnaamaan; sillä minä olen nuori.
7 Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
Niin Herra sanoi minulle: älä sano: minä olen nuori; mutta sinun pitää kaikkiin niihin menemän, mihin minä sinun lähetän, ja puhuman kaikkia, mitä minä sinulle käsken.
8 Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Älä pelkää heitä; sillä minä olen tykönäs, ja pelastan sinun, sanoo Herra.
9 Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
Ja Herra ojensi kätensä ja tarttui minun suuhuni; ja Herra sanoi minulle: katso, minä panen minun sanani sinun suuhus.
10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
Katso, minä panen sinun tänäpänä kansain ja valtakuntain päälle, repimään, särkemään, hukuttamaan ja kukistamaan: rakentamaan ja istuttamaan.
11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
Ja Herran sana tapahtui minulle ja sanoi: Jeremia, mitäs näet? Minä sanoin: Minä näen mandelpuisen sauvan.
12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
Ja Herra sanoi minulle: oikein sinä olet nähnyt, sillä minä tahdon kiiruhtaa, tehdäkseni minun sanani.
13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
Ja Herran sana tapahtui toisen kerran minulle ja sanoi: mitäs näet? Minä sanoin: minä näen kiehuvaisen padan, joka näkyy pohjan puoleen.
14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
Ja Herra sanoi minulle: pohjasta on paha tuleva kaikkein maan asuvaisten päälle.
15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
Sillä katso, minä kutsun kaikki valtakuntain sukukunnat, jotka ovat pohjassa, sanoo Herra; ja he tulevat ja kukin asettaa istuimensa Jerusalemin portin eteen, ja ympäri kaikkia hänen muurejansa, ja kaikkia Juudan kaupungeita,
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
Ja minä annan oikeuden käydä heidän päällensä kaiken heidän pahuutensa tähden; että he ovat minun hyljänneet, ja muille jumalille suitsuttaneet, ja kumartaneet omaa käsialaansa.
17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
Niin vyötä nyt kupees, nouse ja saarnaa heille kaikki, mitä minä sinun käsken; älä pelkää heitä, etten minä sinua surmaisi heidän edessänsä.
18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
Ja katso, minä teen tänäpänä sinun vahvaksi kaupungiksi, rautapatsaaksi ja vaskimuuriksi koko maassa: Juudan kuninkaita ja hänen ruhtinaitansa vastaan, hänen pappejansa ja maan kansaa vastaan.
19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Ja he sotivat sinua vastaan, ei kuitenkaan heidän pidä sinua voittaman; sillä minä olen sinun tykönäs, sanoo Herra, vapahtamassa sinua.

< Yeremiya 1 >