< Yakobo 5 >
1 Tsono tamverani, inu anthu achuma, lirani ndi kufuwula chifukwa cha zovuta zimene zidzakugwereni.
to bring now the/this/who rich to weep to wail upon/to/against the/this/who misery you the/this/who to arrive/invade
2 Chuma chanu chawola ndipo njenjete zadya zovala zanu.
the/this/who riches you to rot and the/this/who clothing you moth-eaten to be
3 Golide ndi siliva wanu zachita dzimbiri. Dzimbirilo lidzakhala umboni wokutsutsani ndi kuwononga mnofu wanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano otsiriza.
the/this/who gold you and the/this/who silver to corrode and the/this/who poison/rust it/s/he toward testimony you to be and to eat the/this/who flesh you as/when fire to store up in/on/among last/least day
4 Taonani, ndalama za malipiro zimene munakanika kulipira aganyu aja ankasenga mʼmunda mwanu zikulira mokutsutsani. Kulira kwa okololawo kwamveka mʼmakutu mwa Ambuye Wamphamvuzonse.
look! the/this/who wage the/this/who worker the/this/who to mow the/this/who country you the/this/who (to defraud *NK(o)*) away from you to cry and the/this/who outcry the/this/who to reap toward the/this/who ear lord: God hosts to enter
5 Mwakhala pa dziko lapansi pano moyo ofewa ndipo mwalidyera dziko lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lokaphedwa.
to self-indulge upon/to/against the/this/who earth: planet and to indulge to feed the/this/who heart you (as/when *K*) in/on/among day slaughter
6 Mwaweruza kuti ndi wolakwa ndipo mwapha munthu wosalakwa, amene sakutsutsana nanu.
to condemn to murder the/this/who just no to resist you
7 Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza.
to have patience therefore/then brother until the/this/who coming the/this/who lord: God look! the/this/who farmer to wait for the/this/who precious fruit the/this/who earth: planet to have patience upon/to/against (it/s/he *NK(o)*) until (if *k*) to take (rain *k*) early rain and late (rain)
8 Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera.
to have patience and you to establish the/this/who heart you that/since: since the/this/who coming the/this/who lord: God to come near
9 Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!
not to groan brother according to one another in order that/to not (to judge *N(K)O*) look! the/this/who judge before the/this/who door to stand
10 Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira.
example to take brother (me *K*) the/this/who suffering and the/this/who patience the/this/who prophet which to speak (in/on/among *no*) the/this/who name lord: God
11 Monga mukudziwa, tinawatenga ngati odalitsika anthu amene anapirira. Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mwaona zimene Ambuye anamuchitira potsiriza pake. Ambuye ndi wodzaza ndi chisoni ndi chifundo.
look! to bless the/this/who (to remain/endure *N(k)O*) the/this/who perseverance Job to hear and the/this/who goal/tax lord: God (to perceive: see *NK(o)*) that/since: that very compassionate to be the/this/who lord: God and compassionate
12 Koposa zonse, abale anga, musamalumbire. Polumbira osamatchula kumwamba kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. “Inde” wanu azikhala “Inde,” ndipo “Ayi” wanu azikhala “Ayi,” kuopa kuti mungadzapezeke olakwa.
before all then brother me not to swear neither the/this/who heaven neither the/this/who earth: planet neither another one oath to be then you the/this/who yes yes and the/this/who no no in order that/to not (by/under: under *N(k)O*) (judgment *NK(O)*) to collapse
13 Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Ayimbe nyimbo zolemekeza.
to endure one in/on/among you to pray be cheerful one to sing praise
14 Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye.
be weak: ill one in/on/among you to call to/summon the/this/who elder: Elder the/this/who assembly and to pray upon/to/against it/s/he to anoint it/s/he olive oil in/on/among the/this/who name the/this/who lord: God
15 Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa.
and the/this/who a vow/prayer the/this/who faith to save the/this/who be weary/sick: ill and to arise it/s/he the/this/who lord: God and if sin to be to do/make: do to release: forgive it/s/he
16 Choncho, ululiranani machimo anu ndi kupemphererana wina ndi mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama ndi lamphamvu ndipo limagwira ntchito.
to agree (therefore/then *NO*) one another (the/this/who sin *N(k)O*) and (to pray/wish for *NK(o)*) above/for one another that to heal much be strong petition just be active
17 Eliya anali munthu ngati ife. Iye anapemphera mwamphamvu kuti mvula isagwe ndipo sinagwedi kwa zaka zitatu ndi theka.
Elijah a human to be like me and prayer to pray the/this/who not to rain down and no to rain down upon/to/against the/this/who earth: planet year Three and month six
18 Kenaka anapempheranso, ndipo kumwamba kunagwetsa mvula, ndipo dziko lapansi linatulutsa zomera zake.
and again to pray and the/this/who heaven rain to give and the/this/who earth: planet to sprout the/this/who fruit it/s/he
19 Abale anga, ngati mmodzi wa inu apatuka pa choonadi ndipo wina wake ndi kumubweza,
brother (me *NO*) if one in/on/among you to lead astray away from the/this/who truth and to turn one it/s/he
20 kumbukirani izi: Aliyense wobweza wochimwa kuchoka ku cholakwa chake, adzamupulumutsa ku imfa ndi kukwirira machimo ambiri.
(to know *NK(O)*) that/since: that the/this/who to turn sinful out from error road it/s/he to save soul (it/s/he *no*) out from death and to cover multitude sin