< Yakobo 4 >
1 Nʼchiyani chimene chimayambitsa ndewu ndi mapokoso pakati panu? Kodi sizichokera ku zilakolako zimene zimalimbana mʼkati mwanu?
Nangmouh dawkvah, tarankâtuknae hoi kâyuenae naw teh nâhoi maw a tho vaw. Nange takthai dawk kâtânae lah kaawm e takngainae lung koehoi vaiyaw a tho vaw.
2 Mumalakalaka zinthu koma simuzipeza, choncho mumapha. Mumasirira zinthu koma simutha kuzipeza zimene mukufuna, choncho mumakangana ndi kumenyana. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.
Na noe awh ei, na hmu awh hoeh dawkvah tami na thei awh. Puenghoi na ngai ei, na tawn thai hoeh dawkvah, na kâyue na kâhem awh teh taran na kâtuk awh. Na tawnhoehnae teh na hei awh hoeh dawk doeh.
3 Koma ngakhale mumapempha simulandira, chifukwa mumapempha ndi zolinga zoyipa. Mumapempha kuti muzigwiritse ntchito pa zokusangalatsani nokha.
Hahoi, na hei awh ei, na hmawt thai awh hoeh. Bangkongtetpawiteh namamouh phunepnae koe hno hanelah dai na hei awh dawk doeh.
4 Inu anthu achigololo, kodi simukudziwa kuti kuchita ubwenzi ndi dziko lapansi ndi kudana ndi Mulungu? Choncho, aliyense wosankha kukhala bwenzi la dziko lapansi amasanduka mdani wa Mulungu.
Kamsoumhoehe napui tongpa yonnae dawk kaawm e napui tongpanaw, talaivan hoi kâhuikonae teh Cathut hoi kâtarannae doeh tie hah na panuek awh hoeh maw. Talaivan hoi kâhuiko ka ngai e tami teh Cathut e taran doeh.
5 Kapena mukuganiza kuti Malemba amanena popanda chifukwa kuti Mulungu amafunitsitsa mwansanje mzimu umene Iye anayika kuti uzikhala mwa ife?
Cathut ni maimouh thung vah na hruek pouh e Muitha teh dipmanae a tawn tie hah Cakathoung ni ayawmyin lah doeh a dei telah na pouk awh maw.
6 Koma amatipatsa chisomo chochuluka. Nʼchifukwa chake Malemba amati, “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma apereka chisomo kwa odzichepetsa.”
Hatei, Cathut ni na poe e lungmanae teh hot hlak patenghai a tha hoe ao rah. Cakathoung ni a dei patetlah kâphokâlen e tami hah a taran teh, ayâ rahim kârahnoum e tami hah yawhawinae a coe sak.
7 Dziperekeni nokha kwa Mulungu. Mukaneni Mdierekezi ndipo adzakuthawani.
Hatdawkvah, Cathut ngainae tarawi awh, kahraimathout hah ngang awh. Telah na tetpawiteh, kahraimathout ni na yawng takhai han.
8 Sendezani kufupi ndi Mulungu ndipo Iye adzasendeza kwa inu. Sambani mʼmanja mwanu, inu anthu ochimwa. Yeretsani mitima yanu, inu anthu okayikira.
Cathut teh hnai awh haw, ama ni na hnai awh van han. Tamikayonnaw na kut thoungsak awh. Lung ka sampheinaw na lung thoungsak awh.
9 Chitani chisoni chifukwa cha zimene mwachita, lirani misozi. Kuseka kwanu kusanduke kulira, ndipo chimwemwe chanu chisanduke chisoni.
Lungthoungnae, lungmathoenae, kanae hoi awm awh. Na panuiparingnae teh lungmathoenae lah, na lunghawinae hai lungmathoenae lah awm sak awh.
10 Dzichepetseni pamaso pa Ambuye ndipo Iye adzakukwezani.
Cathut hmalah kârahnoum awh. Hottelah na tet pawiteh, Cathut ni na tawm takhang han.
11 Abale musamanenane. Aliyense wonenera zoyipa mʼbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo. Pamene muweruza malamulo, ndiye kuti simukusunga malamulowo, koma mukuwaweruza.
Ka hmaunawnghanaw buet touh hoi buet touh kâ pathoe awh hanh, apihai a hmaunawngha ka pathoe e teh kâlawk ka pathoe e lah ao. Hottelah na sak pawiteh, nang teh kâlawk na ka tarawi e lah na awm hoeh. Lawk na ka ceng e lah doeh na o.
12 Pali mmodzi yekha Wopereka Malamulo ndi Woweruza. Ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuwononga. Kodi ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?
Kâlawk na kapoekung, lawkcengkung teh buet touh dueng doeh kaawm. Hote Bawipa ni na rungngang thai teh na raphoe thai. Nang teh bang patet e tami lah mouh na o teh, na tengpam e taminaw hah lawk khuet na ceng va.
13 Tsono tamverani, inu amene mumati, “Lero kapena mawa tipita ku mzinda wakutiwakuti, tikatha chaka chimodzi tikuchita malonda ndi kupanga ndalama.”
Sahnin na ou, tangtho na ou, kahlawng ka cei vaiteh awi haw vah kum tabang ka o han, hno kayo vaiteh, tangka moikapap ka hmu han telah ka pouk e naw, ka lawk heh thai awh haw.
14 Chifukwa chiyani mukutero? Inu simukudziwa zimene ziti zichitike mawa. Kodi moyo wanu ndi wotani? Inu muli ngati nkhungu imene imangooneka kwa kanthawi kochepa ndipo kenaka ndikuzimirira.
Tangtho na hringnae hah bangtelamaw ao han tie hai na panuek awh hoeh. Nangmae na hringnae teh bang patetlah maw ao. Nangmouh teh dawngdengca ka kamnuek niteh tang kahmat e a kahû patetlah doeh na o awh.
15 Koma inuyo muyenera kunena kuti, “Ambuye akalola, tikadzakhala ndi moyo, tidzachita zakutizakuti.”
Hatdawkvah, Bawipa a ngainae awm boilah, maimouh hai hring a boipawiteh, hottelah hoehpawiteh hettelah sak awh sei telah doeh na ti awh hanelah ao.
16 Koma mmene zililimu mumangodzitama ndi kudzikuza. Kudzitama konse kotereku ndi koyipa.
Hatei, atu nangmanaw teh namahoima na kâtalue awh teh na kâoup awh rah, hot patet e kâoupnae pueng teh kahawihoehe hno doeh.
17 Aliyense amene amadziwa zabwino zimene amayenera kuchita koma osazichita, ndiye kuti wachimwa.
Hatdawkvah, apipatet hai, hnokahawi sak hane a panue nahlangva, sak laipalah awm pawiteh, yo a yon toe.