< Yakobo 2 >
1 Abale anga, okhulupirira Yesu Khristu waulemerero, musaonetse tsankho.
My brethren, you must not make distinctions between one man and another while you are striving to maintain faith in the Lord Jesus Christ, who is our glory.
2 Tangoganizirani, pakati panu patabwera munthu atavala mphete yagolide ndi zovala zapamwamba, ndipo winanso wosauka nʼkulowa atavala sanza.
For suppose a man comes into one of your meetings wearing gold rings and fine clothes, and there also comes in a poor man wearing shabby clothes,
3 Ngati musamala kwambiri munthu wovala bwinoyu uja, nʼkumuwuza kuti, “Khalani pa mpando wabwinowu,” koma wosauka uja nʼkumuwuza kuti, “Ima apo,” kapena “Khala pansi pafupi ndi chopondapo mapazi angawa,”
and you pay court to the one who wears the fine clothes, and say, "Sit here; this is a good place;" while to the poor man you say, "Stand there, or sit on the floor at my feet;"
4 kodi simunachite tsankho pakati panu ndi kukhala oweruza a maganizo oyipa?
is it not plain that in your hearts you have little faith, seeing that you have become judges full of wrong thoughts?
5 Tamverani abale anga okondedwa, kodi Mulungu sanasankhe amene dziko lapansi limawaona ngati amphawi kuti akhale olemera mʼchikhulupiriro ndi kulowa ufumu umene Iye analonjeza kwa amene amamukonda?
Listen, my dearly-loved brethren. Has not God chosen those whom the world regards as poor to be rich in faith and heirs of the Kingdom which He has promised to those that love Him?
6 Koma mwakhala mukunyoza amphawi. Kodi si anthu olemerawa amene akukudyerani masuku pamutu? Si anthu amenewa amene amakukokerani ku bwalo la milandu?
But you have put dishonour upon the poor man. Yet is it not the rich who grind you down? Are not they the very people who drag you into the Law courts? --
7 Kodi si omwewa amene amachita chipongwe dzina la wolemekezeka, limene inu mumatchulidwa?
and the very people who speak evil of the noble Name by which you are called?
8 Ngati musungadi lamulo laufumu lija lopezeka mʼMalemba lakuti, “Konda mnansi wako monga iwe mwini,” ndiye kuti mukuchita bwino.
If, however, you are keeping the Law as supreme, in obedience to the Commandment which says "You are to love your fellow man just as you love yourself," you are acting rightly.
9 Koma mukamaonetsa tsankho mukuchimwa, ndipo ndinu wochimwa monga wophwanya lamulo.
But if you are making distinctions between one man and another, you are guilty of sin, and are convicted by the Law as offenders.
10 Pakuti amene amasunga Malamulo onse, akangophwanya fundo imodzi yokha, waphwanya Malamulo onse.
A man who has kept the Law as a whole, but has failed to keep some one command, has become guilty of violating all.
11 Pakuti amene anati “Usachite chigololo” ndi yemweyonso anati “Usaphe.” Ngati suchita chigololo koma umapha, ndiwe wophwanya Malamulo.
For He who said, "Do not commit adultery," also said, "Do not commit murder," and if you are a murderer, although not an adulterer, you have become an offender against the Law.
12 Muziyankhula ndi kuchita zinthu monga anthu amene mudzaweruzidwe ndi lamulo limene limapereka ufulu,
Speak and act as those should who are expecting to be judged by the Law of freedom.
13 chifukwa munthu woweruza mopanda chifundo, nayenso adzaweruzidwa mopanda chifundo. Chifundo chimapambana pa chiweruzo.
For he who shows no mercy will have judgement given against him without mercy; but mercy triumphs over judgement.
14 Abale anga, phindu lake nʼchiyani ngati munthu anena kuti ali ndi chikhulupiriro koma chopanda ntchito zabwino? Kodi chikhulupiriro choterechi chingamupulumutse?
What good is it, my brethren, if a man professes to have faith, and yet his actions do not correspond? Can such faith save him?
15 Tangoganizirani, mʼbale kapena mlongo amene ali ndi usiwa, ndipo alibe chakudya cha tsiku ndi tsiku.
Suppose a Christian brother or sister is poorly clad or lacks daily food,
16 Ngati mmodzi wa inu amuwuza kuti, “Pita ndi mtendere, ukafundidwe ndipo ukakhute,” koma osamupatsa zimene akuzisowa, phindu lake nʼchiyani pamenepa?
and one of you says to them, "I wish you well; keep yourselves warm and well fed," and yet you do not give them what they need; what is the use of that?
17 Chomwechonso, chikhulupiriro chokha chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.
So also faith, if it is unaccompanied by obedience, has no life in it--so long as it stands alone.
18 Koma wina anganene kuti, “Inuyo muli ndi chikhulupiriro koma ine ndili ndi ntchito zabwino.” Onetsani chikhulupiriro chanu chopanda ntchito zabwino ndipo ineyo ndidzakuonetsani chikhulupiriro changa pochita ntchito zabwino.
Nay, some one will say, "You have faith, I have actions: prove to me your faith apart from corresponding actions and I will prove mine to you by my actions.
19 Mumakhulupirira kuti kuli Mulungu mmodzi yekha. Mumachita bwino. Komatu ngakhale ziwanda zimakhulupirira zimenezi ndipo zimanjenjemera ndi mantha.
You believe that God is one, and you are quite right: evil spirits also believe this, and shudder."
20 Munthu wopusa iwe, kodi ukufuna umboni woti chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino nʼchakufa?
But, idle boaster, are you willing to be taught how it is that faith apart from obedience is worthless? Take the case of Abraham our forefather.
21 Kodi Abrahamu kholo lathu sanatengedwe kukhala wolungama chifukwa cha zimene anachita pamene anapereka mwana wake Isake pa guwa lansembe?
Was it, or was it not, because of his actions that he was declared to be righteous as the result of his having offered up his son Isaac upon the altar?
22 Tsono mukuona kuti chikhulupiriro chake ndi ntchito zabwino zinkachitika pamodzi, ndipo chikhulupiriro chake chinasanduka chenicheni chifukwa cha ntchito zake zabwino.
You notice that his faith was co-operating with his actions, and that by his actions his faith was perfected;
23 Ndipo Malemba akunena kuti, “Abrahamu anakhulupirira Mulungu ndipo anatengedwa kukhala wolungama,” ndipo anatchedwa bwenzi la Mulungu.
and the Scripture was fulfilled which says, "And Abraham believed God, and his faith was placed to his credit as righteousness," and he received the name of 'God's friend.'
24 Tsono mukuona kuti munthu amasanduka wolungama ndi ntchito zabwino osati ndi chikhulupiriro chokha ayi.
You all see that it is because of actions that a man is pronounced righteous, and not simply because of faith.
25 Nʼchimodzimodzinso, kodi wadama uja, Rahabe, sanasanduke wolungama chifukwa cha zomwe anachita pamene anapereka malo ogona kwa azondi aja ndi kuwathawitsira mbali ina?
In the same way also was not the notorious sinner Rahab declared to be righteous because of her actions when she welcomed the spies and hurriedly helped them to escape another way?
26 Monga thupi lopanda mzimu ndi lakufa, chomwechonso chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.
For just as a human body without a spirit is lifeless, so also faith is lifeless if it is unaccompanied by obedience.