< Yakobo 1 >

1 Yakobo, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu, kulembera mafuko khumi ndi awiri obalalikana ku mayiko osiyanasiyana. Landirani moni.
Jakovo, muhikana we Ireeza ni wa Simwine Jesu Kresite, ku mishovo ikwanisa iyanza ni yovele ahasene: Ni lumelisa.
2 Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu.
Mwihinde kiti ive kusanga, vakwangu, hamu hita mu matata mangi.
3 Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro.
Mwizi kuti kulikiwa kwe intumelo yenu kuleta ku lileta.
4 Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse.
Musiye ku lileta ku maniniza misevezi ya teni, ili kuti muve vakulite luli ni ku maniniza, ili kuti sanzi muvuli chimwi.
5 Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa.
Kono heva zumi kwenu hasaka vutali, avu kumbile kwa Ireeza, iye yoha chavungi mi nasa kanani, mi kavu hewe.
6 Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo.
Kono mumu siye a kumbile mwi Itumelo, na sa hakanyehi chimwi.
7 Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye.
Imi yense yo hakanyeha u kola ili lindinda mwi wate lika vutizwa luhuho ni li zimbuluka feela. Cwale uzo muntu sanzi ahupuli kuti mwa wane chimi kwa Ireeza.
8 Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.
Muntu wina vulyo wina mihupulo yovele, kawondeki mwi nzila zakwe.
9 Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa.
Misiye mwetu we njevwe alitembe ka chi tulo chikando chakwe,
10 Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo.
kono muhumane ali tembe cha kulikokoveza kwa chitolo chakwe, Mukuti kafwe sina impalisa ya mwinkanda ina mulyani.
11 Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.
Imi izuva lizwa niku hisa ni kuzumisa lyani. Impalisa iwa, mi vulotu vwayo vumani, che nzila iswana, muhumanehi mwa mannine ha kati kamusipili.
12 Wodala ndi munthu amene amapirira mʼmayesero, chifukwa akapambana adzalandira chipewa cha ulemerero chimene Mulungu analonjeza anthu amene amamukonda.
Wina imbuyoti muntu yo lileta kwi ntantuvo. Mi hakumba intantuvo, ava tambuli mushukwe wa vuhalo, vuva sepiswe kwavo vasaka Ireeza.
13 Munthu akayesedwa asanene kuti, “Mulungu akundiyesa.” Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi choyipa kapena Iyeyo kuyesa munthu aliyense.
Muntu halikwa senzi ati, “Na likwa Ireeza,” Mukuti Ireeza kalikwa cha vuvi, Mi kaliki muntu.
14 Koma munthu aliyense amayesedwa akakokedwa ndi zilakolako zake zoyipa ndi kukopedwa nazo.
Kono muntu ni muntu ulikwa che ntakazo yakwe, imu kwita ni kumu chengelela.
15 Pamenepo, chilakolako chikakula chimabala tchimo; ndipo tchimo likakhwima limabereka imfa.
Linu intakazo haimu chunina, i zala chivi. Mi chivi ha chikula, chizala ifu.
16 Musanyengedwe abale anga okondedwa.
Sanzi Mu chengwa, vakwangu va sakiwa.
17 Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba, kwa Atate mwini kuwala, amene sasintha ngati mthunzi woyendayenda.
Impo i ndotu ni impo ina hande izwa kwiwulu. i keza hansi kwuzwa kwe shetu we seli. Imi khakwe kakwina kuchinca kapa munzunde vakeñi chaku sanduka.
18 Iye anasankha kutibereka ife kudzera mʼmawu a choonadi, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, tikakhale ngati zipatso zoyamba.
Ireeza ava keti kutuha kupepa cha linzwii lye niti, ili kuti mufuta muselo we ntazi muzintu zonse za vapangi.
19 Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima.
Mwizi izi, va kwangu vasakiwa: muntu ni muntu azuwe cha vuhweluhwelu, kusa hwela kuku wamba, kulyeha kuvenga.
20 Pakuti mkwiyo wa munthu subweretsa chilungamo chimene amafuna Mulungu.
Kuvenga kwa muntu kaku sevezi ka kuluka kwa Ireeza.
21 Choncho chotsani chizolowezi choyipa ndi khalidwe loyipa pakati panu, ndipo modzichepetsa landirani mawu amene anadzalidwa mwa inu, amene akhoza kukupulumutsani.
chelyo ivaka musiye zina i kwe zonse, nichisina ko cha lunya. cha vuntu tu amuhele ka chishemo linzwii, liwola kuhaza luhuho lwetu.
22 Musamangomvetsera chabe mawu, ndi kumadzinyenga nokha. Chitani zimene mawuwo amanena.
Mutende zi lisaka linzwii isinyi ba lizuwa feela, kulichenga muvene.
23 Munthu aliyense amene amangomva mawu koma osachita zimene mawuwo amanena, ali ngati munthu amene amayangʼana nkhope yake pa galasi.
Mi heva zumi uzuwa linzwii kono kalitendisi, uswa uvu muntu yolilola muchimponi chifateho cha va pepwa kacho.
24 Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera.
Hamana kulivona uyenda kule mi haho uzivala mwekalile.
25 Koma munthu amene amayangʼana mwachidwi lamulo langwiro limene limapatsa ufulu ndi kupitiriza kutero, osayiwala chimene wamva koma kuchita adzadalitsika pa zimene amachita.
Kono muntu yo lilola chentokomelo kamulao wa kulukuluha, mi uzwila havusu kutenda, isinyi kuzuwa vulyo ni kuzivala, uzu muntu mwa tonolwefazwe ke Inkezo zakwe.
26 Ngati wina amadziyesa ngati ndi wachipembedzo, koma chonsecho saletsa lilime lake, amadzinyenga yekha ndipo chipembedzo chakecho ndi cha chabechabe.
Heva zumwi uli hupuela kuti mulumeli, kono ka sikululi lulimwi lwakwe, u chenda inkulo yakwe, mi chilumeli chakwe kachina intuso.
27 Chipembedzo chimene Mulungu Atate athu amachivomereza kuti ndi changwiro ndi chopanda zolakwika ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto awo, ndi kudzisunga bwino kuopa kudetsedwa ndi dziko lapansi.
Ku chena ni ku sanyazahala kwa chilumeli havusu vwa Ireeza ni Ishetu njovu: Kutusa vasena veshavo ni mbwela mu vukavo vwavo, kuli vavalela kuvuvi vwe inkanda.

< Yakobo 1 >