< Yakobo 1 >
1 Yakobo, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu, kulembera mafuko khumi ndi awiri obalalikana ku mayiko osiyanasiyana. Landirani moni.
James, a servant of God and of the Lord Jesus Christ, to the twelve tribes which are scattered abroad, greeting.
2 Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu.
Count it all joy, my brethren, when ye fall into various temptations;
3 Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro.
knowing that the trying of your faith worketh endurance.
4 Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse.
But let endurance have a perfect work, that ye may be perfect and entire, wanting in nothing.
5 Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa.
But if any one of you is wanting in wisdom, let him ask of God, who giveth to all liberally, and upbraideth not; and it will be given him.
6 Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo.
But let him ask in faith, nothing doubting; for he that doubteth is like a wave of the sea driven by the wind and tossed.
7 Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye.
For let not that man think that he shall receive anything from the Lord,
8 Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.
a double-minded man as he is, unstable in all his ways.
9 Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa.
Let the brother of low degree glory in that he is exalted;
10 Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo.
but the rich, in that he is made low; because as the flower of the grass he will pass away.
11 Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.
For the sun rose with its burning heat, and withered the grass, and its flower fell off, and the beauty of its appearance perished; so also will the rich man fade away in his ways.
12 Wodala ndi munthu amene amapirira mʼmayesero, chifukwa akapambana adzalandira chipewa cha ulemerero chimene Mulungu analonjeza anthu amene amamukonda.
Blessed is the man that endureth temptation; for when he is approved, he will receive the crown of life, which He promised to them that love him.
13 Munthu akayesedwa asanene kuti, “Mulungu akundiyesa.” Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi choyipa kapena Iyeyo kuyesa munthu aliyense.
Let no one when he is tempted, say, I am tempted by God; for God cannot be tempted with evil, and he tempteth no one.
14 Koma munthu aliyense amayesedwa akakokedwa ndi zilakolako zake zoyipa ndi kukopedwa nazo.
But each one is tempted when by his own lust he is led away and enticed;
15 Pamenepo, chilakolako chikakula chimabala tchimo; ndipo tchimo likakhwima limabereka imfa.
then lust, having conceived, bringeth forth sin, and sin, when completed, bringeth forth death.
16 Musanyengedwe abale anga okondedwa.
Do not err, my beloved brethren.
17 Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba, kwa Atate mwini kuwala, amene sasintha ngati mthunzi woyendayenda.
Every good gift and every perfect gift is from above, coming down from the Father of the lights, with whom is no change, nor shadow from turning.
18 Iye anasankha kutibereka ife kudzera mʼmawu a choonadi, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, tikakhale ngati zipatso zoyamba.
Of his own will he begot us with the word of truth, that we should be a kind of first-fruits of his creatures.
19 Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima.
Wherefore, my beloved brethren, let every man be swift to hear, slow to speak, slow to wrath.
20 Pakuti mkwiyo wa munthu subweretsa chilungamo chimene amafuna Mulungu.
For the wrath of man worketh not the righteousness of God.
21 Choncho chotsani chizolowezi choyipa ndi khalidwe loyipa pakati panu, ndipo modzichepetsa landirani mawu amene anadzalidwa mwa inu, amene akhoza kukupulumutsani.
Wherefore put off all filthiness, and excess of wickedness, and receive with meekness the implanted word, which is able to save your souls.
22 Musamangomvetsera chabe mawu, ndi kumadzinyenga nokha. Chitani zimene mawuwo amanena.
But be doers of the word, and not hearers only, deceiving yourselves.
23 Munthu aliyense amene amangomva mawu koma osachita zimene mawuwo amanena, ali ngati munthu amene amayangʼana nkhope yake pa galasi.
For if any one is a hearer of the word, and not a doer, he is like a man beholding his natural face in a glass;
24 Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera.
for he beholds himself, and goes away, and immediately forgets what manner of man he was.
25 Koma munthu amene amayangʼana mwachidwi lamulo langwiro limene limapatsa ufulu ndi kupitiriza kutero, osayiwala chimene wamva koma kuchita adzadalitsika pa zimene amachita.
But he who looks into the perfect law of liberty, and remains there, being not a forgetful hearer, but a doer of the work, this man will be blessed in his deed.
26 Ngati wina amadziyesa ngati ndi wachipembedzo, koma chonsecho saletsa lilime lake, amadzinyenga yekha ndipo chipembedzo chakecho ndi cha chabechabe.
If any one thinks that he is religious, and bridles not his tongue, but deceives his own heart, this man's religion is vain.
27 Chipembedzo chimene Mulungu Atate athu amachivomereza kuti ndi changwiro ndi chopanda zolakwika ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto awo, ndi kudzisunga bwino kuopa kudetsedwa ndi dziko lapansi.
Pure religion and undefiled before God, the Father, is this, to visit the fatherless and widows in their affliction, and to keep one's self unspotted from the world.