< Yesaya 1 >

1 Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
Umbono omayelana ngoJuda leJerusalema owabonwa ngu-Isaya indodana ka-Amozi ensukwini zokubusa kuka-Uziya, loJothamu, lo-Ahazi loHezekhiya amakhosi akoJuda.
2 Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
Zwanini, mazulu! Lalelani, mhlaba! Ngoba uThixo usekhulumile: “Ngondla abantwana ngabakhulisa, kodwa sebengihlamukele.
3 Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
Inkabi iyamazi umniniyo, lobabhemi uyasazi isibaya somnikazi wakhe, kodwa u-Israyeli kazi, abantu bami kabaqedisisi.”
4 Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
Maye kuso isizwe esonayo, abantu abathwele amacala, inzalo yabenza okubi, abantwana abaxhwalileyo! Sebemlahlile uThixo; bamdelele oNgcwele ka-Israyeli, bamfulathela.
5 Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
Kungani kumele litshaywe futhi? Kungani liqhubeka ngokuhlamuka? Ikhanda lakho lonke lilimele, yonke inhliziyo yakho ihlukuluziwe.
6 Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
Kusukela ngaphansi kwentende yonyawo lwakho kusiya esicholo sekhanda lakho akukho kuphelela, kodwa izilonda lemvivinya kuphela, kanye lamanxeba; akugeziswanga, akubotshwanga kumbe kwathanjiswa ngamafutha.
7 Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
Ilizwe lenu lichithekile, amadolobho enu atshiswa ngomlilo, umhlaba wenu uphundlwa ngabezizweni, phambi kwenu uqobo, uchitheka njengalapho udilizwa ngabezizweni.
8 Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
Indodakazi yaseZiyoni isele njengedumba esivinini, njengendlwana ensimini yamajodo, njengedolobho elihonqolozelweyo.
9 Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
Aluba uThixo uSomandla kasitshiyelanga abalutshwana abasindayo, sasizakuba njengeSodoma; sasizafana leGomora.
10 Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
Zwanini ilizwi likaThixo, lina babusi baseSodoma, lalelani umthetho kaNkulunkulu wethu, lina bantu baseGomora!
11 Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
“Ubunengi bemihlatshelo yenu buyini kimi?” kutsho uThixo. “Ngileminikelo yokutshiswa edlula efunekayo, eyenqama lamahwahwa ezifuyo ezinonisiweyo; igazi lenkunzi, lelamawundlu lelembuzi kalingithokozisi.
12 Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
Lapho lisiza phambi kwami, ngubani othe linyathele amaguma ami na?
13 Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
Yekelani ukuletha iminikelo eyize! Impepha yenu iyisinengiso kimi. Angingeke ngibekezelele imbuthano yenu yobubi, eyokuThwasa kweNyanga, amaSabatha lemihlangano.
14 Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
Umphefumulo wami uyawazonda amadili enu okuthwasa kwezinyanga lemikhosi yenu emisiweyo. Sekube ngumthwalo kimi; sengikhathele ngokukuthwala.
15 Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
Lapho lichaya izandla zenu likhuleka, ngizalifihlela amehlo ami; loba selikhuleka imikhuleko eminengi, angiyikulalela. Izandla zenu zigcwele igazi!
16 sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
Gezani libe ngabahlambulukileyo. Susani izenzo zenu ezimbi phambi kobuso bami; yekelani ukwenza okubi.
17 phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
Fundani ukwenza okulungileyo; funani ukwahlulela okuhle. Khuthazani abancindezelweyo. Vikelani izintandane; lamulelani umfelokazi.
18 Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
Wozani, siqondisane sindawonye,” kutsho uThixo. “Lanxa izono zenu zibomvu gebhu, zizakuba mhlophe njengonqwaqwane, loba zibomvu njengegazi, zizakuba njengoboya bezimvu.
19 Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
Nxa livuma njalo lilalela, lizakudla okuhle kwelizwe;
20 koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
kodwa nxa linqaba, lihlamuka, lizadliwa yinkemba.” Ngoba umlomo kaThixo usukhulumile.
21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
Khangelani ukuthi idolobho elithembekileyo seliphenduke laba yisifebe kanjani! Lake lagcwala ngokufaneleyo; ukulunga kwakuhlala kulo, kodwa khathesi sekuhlala ababulali!
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
Isiliva senu sesingamanyele, iwayini lenu elihle selihlanganiswe lamanzi.
23 Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
Ababusi benu bangabahlamuki, abangane bamasela; bonke bathanda izivalamlomo, bafune izipho. Izintandane kabazivikeli; indaba yomfelokazi kayifiki kibo.
24 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
Ngakho-ke iNkosi, uThixo uSomandla, uMninimandla ka-Israyeli, uthi: “Yebo! Ngizabhodlisela ezitheni zami, ngibuye ngiphindisele kwabayizitha zami.
25 Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
Ngizaphakamisela isandla sami kini; ngizawahlambulula ngokupheleleyo amanyele enu, ngisuse lakho konke ukungcola kwenu.
26 Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
Ngizabuyisa abehluleli benu njengezinsukwini zakudala, labeluleki benu njengasekuqaleni. Muva uzabizwa ngokuthi iDolobho Lokulunga, iDolobho Elithembekileyo.”
27 Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
IZiyoni izahlengwa ngemfanelo, abaphendukayo bayo bahlengwe ngokulunga.
28 Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
Kodwa abahlamuki lezoni bazachithwa, lalabo abalahla uThixo bazabhubha.
29 “Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
“Lizayangeka ngenxa yezihlahla zomʼokhi ezingcwele elazithokozisa ngazo. Lizadana ngamasimu elawakhethayo.
30 Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
Lizafana lomʼokhi olamahlamvu asebuna, lanjengensimu engelamanzi.
31 Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”
Indoda elamandla izafana lencwathi, umsebenzi wayo ufane lenhlansi; kokubili kuzakutsha kanyekanye, kungekho ozacitsha umlilo.”

< Yesaya 1 >