< Yesaya 1 >

1 Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
The visioun, ether profesie, of Ysaie, the sone of Amos, which he siy on Juda and Jerusalem, in the daies of Osie, of Joathan, of Achas, and of Ezechie, kyngis of Juda.
2 Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
Ye heuenes, here, and thou erthe, perseyue with eeris, for the Lord spak. Y haue nurschid and Y haue enhaunsid sones; sotheli thei han dispisid me.
3 Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
An oxe knew his lord, and an asse knew the cratche of his lord; but Israel knewe not me, and my puple vndurstood not.
4 Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
Wo to the synful folk, to the puple heuy in wickidnesse, to the weiward seed, to the cursid sones; thei han forsake the Lord, thei han blasfemyd the hooli of Israel, thei ben aliened bacward.
5 Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
On what thing schal Y smyte you more, that encreessen trespassyng? Ech heed is sijk, and ech herte is morenynge.
6 Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
Fro the sole of the foot til to the nol, helthe is not ther ynne; wounde, and wannesse, and betyng bolnynge is not boundun aboute, nether curid bi medicyn, nether nurschid with oile.
7 Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
Youre lond is forsakun, youre citees ben brent bi fier; aliens deuouren youre cuntrei bifore you, and it schal be disolat as in the distriyng of enemyes.
8 Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
And the douytir of Sion, `that is, Jerusalem, schal be forsakun as a schadewynge place in a vyner, and as an hulke in a place where gourdis wexen, and as a citee which is wastid.
9 Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
If the Lord of oostis hadde not left seed to vs, we hadden be as Sodom, and we hadden be lijk as Gomorre.
10 Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
Ye princes of men of Sodom, here the word of the Lord; and ye puple of Gommorre, perseyue with eeris the lawe of youre God.
11 Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
Wherto offren ye to me the multitude of youre sacrifices? seith the Lord. Y am ful; Y wolde not the brent sacrifices of wetheris, and the ynnere fatnesse of fatte beestis, and the blood of calues, and of lambren, and of buckis of geet.
12 Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
Whanne ye camen bifore my siyt, who axide of youre hondis these thingis, that ye schulden go in myn hallys?
13 Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
Offre ye no more sacrifice in veyn; encense is abhomynacioun to me; Y schal not suffre neomenye, and sabat, and othere feestis.
14 Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
Youre cumpenyes ben wickid; my soule hatith youre calendis and youre solempnytees; tho ben maad diseseful to me, Y trauelide suffrynge.
15 Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
And whanne ye stretchen forth youre hondis, Y schal turne awei myn iyen fro you; and whanne ye multiplien preyer, Y schal not here; for whi youre hondis ben ful of blood.
16 sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
Be ye waischun, be ye clene; do ye awei the yuel of youre thouytis fro myn iyen; ceesse ye to do weiwardli, lerne ye to do wel.
17 phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
Seke ye doom, helpe ye hym that is oppressid, deme ye to the fadirles and modirles child, defende ye a widewe.
18 Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
And come ye, and repreue ye me, seith the Lord. Thouy youre synnes ben as blood reed, tho schulen be maad whijt as snow; and thouy tho ben reed as vermylioun, tho schulen be whijt as wolle.
19 Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
If ye wolen, and heren me, ye schulen ete the goodis of erthe.
20 koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
That if ye nylen, and ye terren me to wrathfulnesse, swerd schal deuoure you; for whi the mouth of the Lord spak.
21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
Hou is the feithful citee ful of dom maad an hoore? riytfulnesse dwellide ther ynne; but now menquelleris dwellen ther ynne.
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
Thi siluer is turned in to dros, ether filthe; thi wyn is medlid with watir.
23 Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
Thi princes ben vnfeithful, the felowis of theuys; alle louen yiftis, suen meedis; thei demen not to a fadirles child, and the cause of a widewe entrith not to hem.
24 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
For this thing, seith the Lord God of oostis, the stronge of Israel, Alas! Y schal be coumfortid on myn enemyes, and Y schal be vengid on myn enemyes.
25 Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
And Y schal turne myn hond to thee, and Y schal sethe out thi filthe to the cleene, and Y schal do awei al thi tyn.
26 Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
And Y schal restore thi iuges, as thei weren bifor to, and thi counselours, as in elde tyme. Aftir these thingis thou schalt be clepid the citee of the riytful, a feithful citee.
27 Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
Sion schal be ayen bouyt in dom, and thei schulen bringe it ayen in to riytfulnesse;
28 Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
and God schal al to-breke cursid men and synneris togidere, and thei that forsoken the Lord, schulen be wastid.
29 “Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
For thei schulen be aschamed of idols, to whiche thei maden sacrifice; and ye shulen be aschamid on the orcherdis, whiche ye chesiden.
30 Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
Whanne ye schulen be as an ook, whanne the leeues fallen doun, and as an orcherd with out watir.
31 Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”
And youre strengthe schal be as a deed sparcle of bonys, `ether of herdis of flex, and youre werk schal be as a quyk sparcle; and euer either schal be brent togidere, and noon schal be that schal quenche.

< Yesaya 1 >