< Yesaya 1 >

1 Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
This is the vision that Isaiah, son of Amoz, saw about Judah and Jerusalem in the reigns of Uzziah, Jotham, Ahaz, and Hezekiah, kings of Judah.
2 Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
Heavens, listen! Earth, pay attention! For the Lord has spoken! I brought up children, I cared for them, but they have rebelled against me.
3 Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
An ox knows its owner, and a donkey knows its feeding trough; but my people don't know me, they don't understand me.
4 Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
What a sinful nation—a people carrying such a load of guilt, an evil generation, corrupt children! They have abandoned the Lord. They have despised Israel's Holy One. They have become strangers. They have gone backwards.
5 Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
Are you wanting to be punished? Are you going to continue to rebel? The whole of your head is damaged, and your heart is totally giving out.
6 Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
You're injured from head to toe, bruised and sore, with open wounds that haven't been cleaned or bandaged or treated with olive oil.
7 Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
Your country has been devastated, your towns burned down, your fields stripped bare by foreigners right in front of you, as they turn it all into a wasteland.
8 Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
The daughter of Zion is left like a shack in a vineyard, like a hut in a cucumber field, like a city under attack.
9 Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
If the Lord Almighty hadn't let a few of us survive, we would have become like Sodom and Gomorrah.
10 Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
Listen to what the Lord has to say, you rulers of Sodom! Pay attention to the instructions of our God, you people of Gomorrah!
11 Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
What use are all your many sacrifices to me? asks the Lord. I am sick and tired of your burnt offerings of rams and the fat of sacrificial animals. I don't delight in the blood of bulls and lambs and goats!
12 Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
When you come to appear before me in worship, who asked you to proudly tramp around my courts?
13 Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
Don't bring me any more meaningless offerings; your incense is offensive to me. Your new moon festivals and Sabbath observations and your calling of special religious meetings—I can't stand them because they're evil, as are your solemn assemblies.
14 Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
I detest your new moon and yearly festivals with my whole being! They've become just a burden to me—I can't bear them anymore!
15 Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
When you hold up your hands to me in prayer, I'll look away. Even though you pray many prayers, I won't pay attention to them, because your hands are full of blood.
16 sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
Wash yourselves and clean yourselves up. Get rid of your sins—I don't want to see them! Stop doing evil!
17 phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
Learn to do good; strive for justice, condemn those who oppress others; support the rights of orphans, take up cases to defend widows.
18 Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
Come on, let's argue this out, says the Lord. Even though your sins are like scarlet, they will become white like snow. Even though they are red like crimson, they will become like wool.
19 Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
If you really want this, and if you do as you're told, then you yourselves will eat the best things that the land produces.
20 koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
But if you are defiant, and if you are rebellious, you'll be killed by the sword. This is what the Lord has declared!
21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
The city that used to be faithful has turned into a prostitute! Once she operated on principles of justice and followed what was right, but now only murderers live there.
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
Your silver has become worthless waste; you wine has been watered down.
23 Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
Your leaders are rebels, friends of thieves. They all love bribes and want to get kickbacks. They don't defend the rights of orphans, and refuse to take cases to help widows.
24 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
So this is what the Lord says, the Lord Almighty, the Mighty One of Israel: Ha! I will take satisfaction in punishing my enemies, by paying back those who hate me!
25 Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
I will turn against you. I will refine you in a furnace, removing all impurities.
26 Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
I will give you good leaders as you used to have before, wise counselors as you had in the beginning. After that you will once again be called the City of Integrity, the Faithful City.
27 Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
Zion will be rescued by justice, those who repent by doing right.
28 Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
But rebels and sinners will be destroyed together, and those who abandon the Lord will die.
29 “Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
You will be ashamed about how you enjoyed your pagan worship among the oak trees; you will be embarrassed because you chose the pleasure gardens of idols.
30 Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
As a result you will become like an oak whose leaves have withered, a dried-out garden that has no water.
31 Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”
Your strong people will become like tinder, and their work will become like a spark. They will burn together, and nobody will be able to put out the flames.

< Yesaya 1 >