< Yesaya 9 >
1 Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
Тотушь ынтунерикул ну ва ымпэрэци вешник пе пэмынтул ын каре акум есте неказ. Дупэ кум ын времуриле трекуте а акоперит ку окарэ цара луй Забулон ши цара луй Нефтали, ын времуриле виитоаре ва акопери ку славэ цинутул де лынгэ маре, цара де динколо де Йордан, Галилея нямурилор.
2 Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
Попорул каре умбла ын ынтунерик веде о маре луминэ; песте чей че локуяу ын цара умбрей морций рэсаре о луминэ.
3 Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
Ту ынмулцешть попорул, ый дай марь букурий; ши ел се букурэ ынаинтя Та кум се букурэ ла сечериш, кум се веселеште ла ымпэрциря прэзий.
4 Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
Кэч жугул каре апэса асупра луй, тоягул каре-й ловя спинаря, нуяуа челуй че-л асупря, ле-ай сфэрымат, ка ын зиуа луй Мадиан.
5 Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
Кэч орьче ынкэлцэминте пуртатэ ын ынвэлмэшяла луптей ши орьче хайнэ де рэзбой тэвэлитэ ын сынӂе вор фи арункате ын флэкэрь, ка сэ фие арсе де фок.
6 Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
Кэч ун Копил ни С-а нэскут, ун Фиу ни с-а дат ши домния ва фи пе умэрул Луй; Ыл вор нуми: Минунат, Сфетник, Думнезеу таре, Пэринтеле вешничиилор, Домн ал пэчий.
7 Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
Ел ва фаче ка домния Луй сэ кряскэ ши о паче фэрэ сфыршит ва да скаунулуй де домние ал луй Давид ши ымпэрэцией луй, о ва ынтэри ши о ва сприжини прин жудекатэ ши неприхэнире, де акум ши-н вечь де вечь. Ятэ че ва фаче рывна Домнулуй оштирилор.
8 Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
Домнул тримите ун кувынт ымпотрива луй Иаков, кувынт каре каде асупра луй Исраел.
9 Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
Тот попорул ва авя куноштинцэ де ел, Ефраим ши локуиторий Самарией, каре спун ку мындрие ши ынгымфаре:
10 “Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
„Ау кэзут ниште кэрэмизь, дар вом зиди ку петре чоплите, ау фост тэяць ниште смокинь дин Еӂипт, дар ый вом ынлокуи ку чедри.”
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
Де ачея Домнул ва ридика ымпотрива лор пе врэжмаший луй Рецин ши ва стырни пе врэжмаший лор:
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
пе сириений де ла рэсэрит, пе филистений де ла апус, ши вор мынка пе Исраел ку гура плинэ; ку тоате ачестя, мыния Луй ну се потолеште ши мына Луй есте тот ынтинсэ.
13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
Кэч нич попорул ну се ынтоарче ла Чел че-л ловеште ши ну каутэ пе Домнул оштирилор.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
Де ачея Домнул ва смулӂе дин Исраел капул ши коада, рамура де финик ши трестия ынтр-о сингурэ зи.
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
(Бэтрынул ши дрегэторул сунт капул, ши пророкул каре ынвацэ пе оамень минчунь есте коада.)
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
Чей че повэцуеск пе попорул ачеста ыл дук ын рэтэчире ши чей че се ласэ повэцуиць де ей сунт пердуць.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Де ачея нич Домнул н-ар путя сэ се букуре де тинерий лор, нич сэ айбэ милэ де орфаний ши вэдувеле лор, кэч тоць сунт ниште нелеӂюиць ши ниште рэй ши тоате гуриле лор спун мишелий. Ку тоате ачестя, мыния Луй ну се потолеште ши мына Луй есте тот ынтинсэ.
18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
Кэч рэутатя арде ка ун фок, каре мэнынкэ мэрэчинь ши спинь, апринде десишул пэдурий, дин каре се ыналцэ стылпь де фум.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
Де мыния Домнулуй оштирилор, цара паркэ ар фи апринсэ ши попорул есте ка арс де фок; нимень ну круцэ пе фрателе сэу,
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
фиекаре жефуеште ын дряпта ши рэмыне флэмынд, мэнынкэ ын стынга ши ну се сатурэ. Ла урмэ ышь мэнынкэ фиекаре карня брацулуй сэу:
21 Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Манасе мэнынкэ пе Ефраим, Ефраим – пе Манасе ши амындой, ымпреунэ, пе Иуда. Ку тоате ачестя, мыния Луй ну се потолеште ши мына Луй есте тот ынтинсэ.