< Yesaya 9 >

1 Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
اما این تاریکی برای قوم خدا که در تنگی هستند تا ابد باقی نخواهد ماند. خدا سرزمین قبایل زبولون و نفتالی را در گذشته خوار و ذلیل ساخته بود، اما در آینده او تمام این سرزمین را از دریای مدیترانه گرفته تا آن سوی اردن و تا خود جلیل که بیگانگان در آن زندگی می‌کنند، مورد احترام قرار خواهد داد.
2 Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
مردمانی که در تاریکی راه می‌روند، نوری عظیم خواهند دید، و بر آنان که در دیار ظلمت غلیظ ساکن بودند، نوری خواهد تابید.
3 Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
ای خداوند، تو خوشی قوم خود را افزودی و به ایشان شادمانی بخشیدی. آنها همچون کسانی که با شادی محصول را درو می‌کنند، و مانند آنانی که با خوشحالی غنایم را بین خود تقسیم می‌نمایند، در حضور تو شادمانی می‌کنند.
4 Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
زیرا تو یوغی را که بر گردن آنها بود شکستی و ایشان را از دست قوم تجاوزگر رهانیدی، همچنانکه در گذشته مدیانی‌ها را شکست داده، قومت را آزاد ساختی.
5 Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
تمام اسلحه‌ها و لباسهای جنگی که به خون آغشته‌اند خواهند سوخت و از بین خواهند رفت.
6 Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
زیرا فرزندی برای ما به دنیا آمده! پسری به ما بخشیده شده! او بر ما سلطنت خواهد کرد. نام او «عجیب»، «مشیر»، «خدای قدیر»، «پدر جاودانی» و «سرور سلامتی» خواهد بود.
7 Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
او بر تخت پادشاهی داوود خواهد نشست و بر سرزمین او تا ابد سلطنت خواهد کرد. پایهٔ حکومتش را بر عدل و انصاف استوار خواهد ساخت، و گسترش فرمانروایی صلح‌پرور او را انتهایی نخواهد بود. خداوند لشکرهای آسمان چنین اراده فرموده و این را انجام خواهد داد.
8 Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
خداوند برضد خاندان یعقوب سخن گفته، او قوم اسرائیل را مجازات خواهد کرد،
9 Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
و تمام قوم که در سامره و سایر شهرها هستند خواهند فهمید که او این کار را کرده است؛ زیرا این قوم مغرور شده‌اند و می‌گویند:
10 “Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
«هر چند خشتهای خانه‌های ما ریخته، ولی با سنگها آنها را بازسازی خواهیم کرد. هر چند درختان انجیر ما بریده شده‌اند، اما به جای آنها درختان سرو خواهیم کاشت.»
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
خداوند دشمنان اسرائیل را علیه او برانگیخته است.
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
او سوری‌ها را از شرق و فلسطینی‌ها را از غرب فرستاده تا اسرائیل را ببلعند. با این حال، خشم خداوند فروکش نکرده و دست او همچنان برای مجازات دراز است.
13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
اما اسرائیل توبه نمی‌کند و به سوی خداوند لشکرهای آسمان برنمی‌گردد.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
بنابراین، خداوند در یک روز مردم اسرائیل و رهبرانشان را مجازات خواهد کرد و سر و دم این قوم را خواهد برید!
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
ریش‌سفیدان و اشراف اسرائیل سر قوم هستند و انبیای کاذبش دم آن.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
اینها که هادیان قوم هستند قوم را به گمراهی و نابودی کشانده‌اند.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
خداوند جوانانشان را مجازات خواهد کرد و حتی بر بیوه‌زنان و یتیمانشان نیز رحم نخواهد نمود، زیرا همهٔ ایشان خدانشناس و شرور و دروغگو هستند. به این سبب است که هنوز خشم خدا فروکش نکرده و دست او برای مجازات ایشان دراز است.
18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
شرارت این قوم باعث شده غضب خداوند لشکرهای آسمان افروخته گردد و مانند آتشی که خار و خس را می‌سوزاند و تمام جنگل را فرا می‌گیرد و دود غلیظی به آسمان می‌فرستد، همه را بسوزاند. مردم مانند هیزم می‌سوزند و حتی برادر به برادر کمک نمی‌کند.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
لقمه را از دست یکدیگر می‌قاپند و می‌خورند اما سیر نمی‌شوند. از شدت گرسنگی حتی بچه‌های خودشان را نیز می‌خورند!
21 Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
قبیلهٔ منسی و قبیلهٔ افرایم بر ضد یکدیگر، و هر دو بر ضد یهودا برخاسته‌اند. ولی با وجود این خشم خداوند فروکش نمی‌کند و دست او هنوز برای مجازات ایشان دراز است.

< Yesaya 9 >