< Yesaya 9 >

1 Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
Car [il n'y a] point eu d'obscurité épaisse pour celle qui a été affligée, au temps que le premier se déchargea légèrement vers le pays de Zabulon, et vers le pays de Nephthali; et que le dernier s'appesantit sur le chemin de la mer, au deçà du Jourdain dans la Galilée des Gentils.
2 Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
Le peuple qui marchait dans les ténèbres a vu une grande lumière, et la lumière a relui sur ceux qui habitaient au pays de l'ombre de la mort.
3 Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
Tu as multiplié la nation, tu lui as accru la joie, ils se réjouiront devant toi, comme on se réjouit en la maison, comme on s'égaye quand on partage le butin.
4 Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
Car tu as mis en pièces le joug dont il était chargé, et le bâton dont on lui battait ordinairement les épaules, et la verge de son exacteur, comme au jour de Madian.
5 Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
Parce que tout choc de ceux qui se battent le fait avec tumulte, et que les vêtements sont vautrés dans le sang; mais ceci sera [comme] un embrasement, quand le feu dévore quelque chose.
6 Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
Car l'enfant nous est né, le Fils nous a été donné, et l'empire a été posé sur son épaule, et on appellera son nom, l'Admirable, le Conseiller, le [Dieu] Fort et puissant, le Père d'éternité, le Prince de paix.
7 Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
Il n'y aura point de fin à l'accroissement de l'empire, et à la prospérité sur le trône de David, et sur son règne, pour l'affermir et l'établir en jugement et en justice, dès maintenant et à toujours; la jalousie de l'Eternel des armées fera cela.
8 Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
Le Seigneur a envoyé la parole en Jacob, et elle est tombée en Israël.
9 Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
Et tout le peuple, [savoir] Ephraïm, et les habitants de Samarie le connaîtront, et [néanmoins] ils diront avec orgueil et avec un cœur hautain;
10 “Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
Les briques sont tombées, mais nous bâtirons de pierres de taille; les figuiers sauvages ont été coupés, mais nous les changerons en cèdres.
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
Après que l'Eternel aura élevé les ennemis de Retsin au-dessus de lui, il amènera aussi pêle-mêle les ennemis d'Israël;
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
La Syrie du côté d'Orient, et les Philistins du côté d'Occident, qui dévoreront Israël à gueule ouverte. Malgré tout cela il ne fera point cesser sa colère, mais sa main sera encore étendue.
13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
Parce que le peuple ne se sera point retourné jusqu'à celui qui le frappait, et qu'ils n'auront pas recherché l'Eternel des armées.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
A cause de cela l'Eternel retranchera d'Israël en un seul jour la tête et la queue, le rameau et le jonc.
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
L'Ancien et l'homme d'autorité; c'est la tête; et le Prophète enseignant mensonge, c'est la queue.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
Ceux donc qui font accroire à ce peuple qu'il est heureux, se trouveront des séducteurs; et ceux à qui on fait accroire qu'ils sont heureux, seront perdus.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
C'est pourquoi le Seigneur ne prendra point plaisir à ses jeunes gens d'élite, et n'aura point pitié de ses orphelins, ni de ses veuves; car tous, tant qu'ils sont, ce sont des hypocrites, et des malins, et toute bouche ne profère que des infamies. Malgré tout cela, il ne fera point cesser sa colère, mais sa main sera encore étendue.
18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
Car la méchanceté est embrasée comme un feu, elle dévorera les ronces et les épines, et s'allumera dans les lieux les plus épais de la forêt, qui se perdront en s'élevant, comme une fumée qui monte.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
La terre sera obscurcie à cause de la fureur de l'Eternel des armées, et le peuple sera comme la pâture du feu; l'un n'aura point compassion de l'autre.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
Il ravira à main droite, et il aura faim; il mangera à main gauche, et ils ne seront point rassasiés; chacun mangera la chair de son bras.
21 Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Manassé [dévorera] Ephraïm, et Ephraïm [dévorera] Manassé; eux ensemble seront contre Juda. Malgré tout cela il ne fera point cesser sa colère, mais sa main sera encore étendue.

< Yesaya 9 >